< Genesis 43 >
1 Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
And the famine [was] severe in the land.
2 Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
And it came to pass, when they had consumed the corn which they had brought from Egypt, their father said to them, Go again, buy us a little food.
3 Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
And Judah spoke to him, saying, The man did solemnly protest to us, saying, Ye shall not see my face, except your brother [be] with you.
4 Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
If thou wilt send our brother with us, we will go down and buy thee food:
5 Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
But if thou wilt not send [him], we will not go down, for the man said to us, Ye shall not see my face, except your brother [be] with you.
6 Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
And Israel said, Why dealt ye [so] ill with me, [as] to tell the man whether ye had yet a brother?
7 Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
And they said, The man asked us strictly concerning our state, and our kindred, saying, [Is] your father yet alive? have ye [another] brother? and we told him according to the tenor of these words: Could we certainly know that he would say, Bring your brother down?
8 Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
And Judah said to Israel, his father, Send the lad with me, and we will arise and go; that we may live, and not die, both we, and thou, [and] also our little ones.
9 Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
I will be surety for him; of my hand shalt thou require him: if I bring him not to thee, and set him before thee, then let me bear the blame for ever:
10 Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
For except we had delayed, surely now we had returned this second time.
11 Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
And their father Israel said to them, If [it must be] so now, do this; take of the best fruits in the land in your vessels, and carry to the man a present, a little balm, and a little honey, spices, and myrrh, nuts, and almonds:
12 Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
And take double money in your hand; and the money that was returned in the mouth of your sacks, carry [it] again in your hand; it may be it [was] an oversight:
13 Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
Take also your brother, and arise, go again to the man:
14 Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
And God Almighty give you mercy before the man, that he may send away your other brother, and Benjamin: If I be bereaved, I am bereaved.
15 Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
And the men took that present, and they took double money in their hand, and Benjamin; and arose, and went down to Egypt, and stood before Joseph.
16 Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
And when Joseph saw Benjamin with them, he said to the ruler of his house, Bring [these] men home, and slay, and make ready: for [these] men shall dine with me at noon.
17 Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
And the man did as Joseph commanded: and the man brought the men into Joseph's house.
18 Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
And the men were afraid, because they were brought into Joseph's house; and they said, Because of the money that was returned in our sacks at the first time, are we brought in; that he may seek occasion against us, and fall upon us, and take us for bond-men, and our asses.
19 Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
And they came near to the steward of Joseph's house, and they communed with him at the door of the house,
20 “Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
And said, O sir, we came down indeed at the first time to buy food:
21 koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
And it came to pass, when we came to the inn, that we opened our sacks, and behold, [every] man's money [was] in the mouth of his sack, our money in full weight: and we have brought it again in our hand.
22 Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
And other money have we brought down in our hands to buy food: we cannot tell who put our money in our sacks.
23 Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
And he said, Peace [be] to you, fear not: your God, and the God of your father, hath given you treasure in your sacks: I had your money. And he brought Simeon out to them.
24 Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
And the man brought the men into Joseph's house, and gave [them] water, and they washed their feet; and he gave their asses provender.
25 Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
And they made ready the present against Joseph should come at noon: for they heard that they should eat bread there.
26 Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
And when Joseph came home, they brought him the present which [was] in their hand into the house, and bowed themselves to him to the earth.
27 Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
And he asked them of [their] welfare, and said, [Is] your father well, the old man of whom ye spoke? [Is] he yet alive?
28 Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
And they answered, Thy servant, our father, [is] in good health, he [is] yet alive: and they bowed their heads and made obeisance.
29 Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
And he lifted up his eyes, and saw his brother Benjamin, his mother's son, and said, [Is] this your younger brother, of whom ye spoke to me? And he said, God be gracious to thee, my son.
30 Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
And Joseph made haste; for his bowels yearned towards his brother: and he sought [where] to weep; and he entered into [his] chamber, and wept there.
31 Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
And he washed his face, and went out, and refrained himself, and said, Set on bread.
32 Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
And they set on for him by himself, and for them by themselves, and for the Egyptians who ate with him, by themselves; because the Egyptians might not eat bread with the Hebrews; for that [is] an abomination to the Egyptians.
33 Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
And they sat before him, the first-born according to his birth-right, and the youngest according to his youth: and the men wondered one at another.
34 Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.
And he took [and sent] messes to them from before him: but Benjamin's mess was five times so much as any of theirs. And they drank, and were merry with him.