< Genesis 43 >
1 Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
The famine in Canaan got worse.
2 Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
Finally, when Jacob and his family had eaten all the grain they had brought from Egypt, Jacob said to them, “Go back to Egypt and buy some more grain for us!”
3 Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
But Judah said to him, “The man who sold us the grain warned us sternly, ‘I will not let you see me [SYN] again if you come and your younger brother is not with you.’
4 Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
So, if you will send our younger brother with us, we will go down to Egypt and buy some grain for you.
5 Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
But if you will not send him, we will not go down there, because that man said to us, ‘I will not let you see me again if your younger brother is not with you.’”
6 Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
Jacob asked, “Why did you cause me to have this trouble by telling the man that you had a younger brother?”
7 Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
One of them replied, “The man asked about us and about our family. He said, ‘Is your father still living? Do you have another brother?’ We had to answer his questions. (We could not know that he would say, ‘The next time that you come down here, bring your brother with you!’/How could we know that he would say, ‘The next time that you come down here, bring your brother with you!’)” [RHQ]
8 Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
Then Judah said to his father Jacob, “Send the boy with me, and we will go immediately, in order that we and you and our children may get grain and not die from hunger.
9 Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
I myself will guarantee that he will return. You can require me to do what I am promising [IDM]. If I do not bring him back to you safely, you can say forever that (I am to blame/it was my fault [that he did not return to you)].
10 Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
If we had not (wasted so much time/waited so long), by now we could have gone there and returned two times!”
11 Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
Then their father Jacob said to them, “If there is no other way, do this: Put in your sacks some of the best things that are grown in this land, and take them down to the man as a gift. Take some balm/perfume and honey and spices and myrrh/ointment, some pistachio nuts, and almonds.
12 Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
Take twice as much money as you took the previous time, because you must return the silver that someone put in the tops of your sacks. Perhaps it was a mistake that it was put in your sacks.
13 Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
Take your younger brother and go back to that man.
14 Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
I will pray that God Almighty will cause that man to act mercifully toward you, so that he will let your other brother, as well as Benjamin, come back here with you. But as for me, if my sons are taken from me, then I will not have my sons!”
15 Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
So the men took the gifts that Jacob said that they should take, and twice the amount of money that the grain would cost, and they also took Benjamin. They went down quickly to Egypt, and they stood in front of Joseph.
16 Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
When Joseph saw Benjamin with them, he said to the man who (was in charge of/supervised) things in his house, “Take these men to my house. Slaughter an animal and prepare a meal, because I want them to eat with me at noon.” [And he told him in what order they were to be seated].
17 Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
The man did as Joseph said. And he took them to Joseph’s house.
18 Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
But they were afraid because he was taking them to Joseph’s house. They were thinking, “He is taking us here because of the silver that was put in our sacks the first time that we came here. While we are eating, he will have his servants attack us and seize us and cause us to become his slaves, and also take our donkeys.”
19 Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
They went with the man who was in charge of things in Joseph’s house. When they arrived at the entrance of the house,
20 “Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
one of them said to him, “Please, sir, listen to me. We came down here previously and bought some grain.
21 koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
But at the place where we stopped for the night as we were returning home, we opened our sacks. We were astonished to see that in the top of each of our sacks was the exact amount of silver that we had paid for the grain! So we have brought it back with us.
22 Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
We have also brought more silver with us to buy more grain. We do not know who put the silver in our sacks.”
23 Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
The man replied, [“Relax]! Do not worry about it! I received the silver that you brought. Your God, the God your father worships, must have put it in your sacks.” And then he brought Simeon to them from the prison.
24 Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
Then he took them into Joseph’s house. He gave them water to wash their feet and gave them food for the donkeys.
25 Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
He told them that they were going to eat with Joseph at noon. So the men prepared their gifts to give to Joseph when he arrived.
26 Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
When Joseph came home, they presented to him the gifts that they had brought into the house. Then they bowed down to the ground in front of him.
27 Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
He asked them if they were (well/in good health), and then he asked, “How is the health of your old father, the one that you told me about? Is he still living?”
28 Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
One of them replied, “Yes, our father, [who is willing to be] your servant, is still alive, and he is well.” Then again they bowed down in front of him.
29 Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
Then he saw his [younger] brother Benjamin, his own mother’s other son. He asked them, “Is this your youngest brother, the one whom you told me about?” After they said “Yes,” he said to Benjamin, “Young man, I pray that God will act kindly toward you.”
30 Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
Joseph quickly left the room. He realized that he was about to cry because he (was full of emotion about his younger brother/loved his younger brother so much). He went into his private room and cried there.
31 Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
Then, after he washed the tears from his face, he came out, and controlling his emotions, he said to the servants, “Serve the food!”
32 Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
The people of Egypt considered that it was disgraceful for them to eat with Hebrews, so the servants served food to Joseph by himself, and served the other people of Egypt who ate with him by themselves, and they served Joseph’s older brothers and younger brother by themselves.
33 Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
His brothers were astonished to see that their seats were arranged according to their ages, from the oldest to the youngest!
34 Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.
And when their portions of food were served to them from Joseph’s table, Benjamin’s portion was five times as much as anyone else’s portion! So they ate food and drank wine with Joseph and became very cheerful.