< Genesis 43 >

1 Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
А гладът ставаше голям по земята.
2 Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
И като изядоха житото, което донесоха от Египет, баща им рече: Идете пак, купете ни малко храна.
3 Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
А Юда, като му говореше, каза: Човекът строго ни заръча, казвайки: Няма да видите лицето ми, ако брат ви не бъде с вас.
4 Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
Ако изпратиш брата ни с нас, ще слезем и ще ти купим храна;
5 Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
но ако не го изпратиш, няма да слезем; защото човекът ни рече: Няма да видите лицето ми, ако брат ви не бъде с вас.
6 Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
А Израил рече: Защо ми сторихте това зло та казахте на човека, че имате и друг брат?
7 Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
А те рекоха: Човекът разпита подробно за нас и за рода ни, като ни каза: Баща ви жив ли е още? имате ли и друг брат? И ние му отговорихме според тия негови думи. От где да знаем ние, че щеше да каже: Доведете брата си.
8 Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
Тогава, Юда рече на баща си, Израиля: Изпрати детето с мене, и да станем да отидем, за да живеем и да не измрем - и ние, ти и чадата ни.
9 Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
Аз отговарям за него; от моята ръка го искай; ако не ти го доведа и него представя пред тебе, тогава нека съм виновен пред тебе за винаги.
10 Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
Понеже, ако не бяхме се бавили, без друго до сега бихме се върнали втори път.
11 Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
Тогава, баща им Израил каза: Ако е тъй, това сторете: вземете в съдовете си от най-хубавите плодове на нашата земя - малко балсама и малко мед, аромати и смирна, фъстъци и бадеми - та ги занесете подарък на човека;
12 Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
вземете двойно повече пари в ръцете си, върнатите в чувалите ви пари, повърнете с ръцете си: може да е станало грешка.
13 Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
Вземете и брата си та станете и идете при човека.
14 Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
А Бог Всемогъщи да ви даде да придобиете благоволението на човека, та да пусне другия ви брат и Вениамина. А аз, ако е речено да остана без чада, нека остана без чада.
15 Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
Тогава човеците, като взеха тоя подарък, взеха двойно повече пари в ръцете си и Вениамина; и станаха та слязоха в Египет и представиха се на Иосифа.
16 Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
А Иосиф, като видя Вениамина с тях, рече на домакина си: Заведи тия човеци у дома ми и заколи каквото трябва и приготви; защото човеците ще обядват с мене на пладне.
17 Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
И човекът стори, каквото поръча Иосиф, и той въведе човеците в Иосифовия дом.
18 Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
А човеците се уплашиха, загдето ги поведоха в Иосифовия дом, и рекоха: Поради парите, върнати в чувалите ни първия път, ни повеждат, за да намери повод против нас, да ни нападне и да зароби нас и ослите ни.
19 Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
Затова те се приближиха при Иосифовия домакин и говориха му при вратата на дома, казвайки:
20 “Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
Послушай, господарю, слязохме първия път да си купим храна;
21 koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
а на връщане, когато дойдохме до мястото за пренощуване и отворихме чувалите си, ето, на всеки парите бяха в чувала му, парите ни напълно: затова ги донесохме обратно в ръцете си.
22 Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
Донесохме и други пари в ръцете си, за да купим храна; не знаем, кой тури парите ни в чувалите ни.
23 Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
А той каза: Бъдете спокойни, не бойте се; Бог ваш и Бог на баща ви, ви даде скритото в чувалите ви съкровище; аз получих парите ви. Тогава изведе при тях Симеона.
24 Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
И домакинът въведе човеците в Иосифовия дом и им даде вода та си умиха нозете; даде и храна за ослите им.
25 Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
А те приготвиха подаръка за Иосифа преди да дойде на пладне; защото чуха, че там щели да ядат хляб.
26 Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
И когато дойде Иосиф у дома, поднесоха му в къщи подаръка, който беше в ръцете им; и му се поклониха до земята.
27 Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
И след като ги разпита за здравето им, рече: Здрав ли е баща ви, старецът, за когото ми говорехте? Жив ли е още?
28 Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
А те казаха: Здрав е слугата ти, баща ни, жив е още. И наведоха се та се поклониха.
29 Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
И като подигна очи видя едноутробния си брат Вениамин и каза: Тоя ли е най-младият ви брат, за когото ми говорихте? И рече: Бог да бъде милостив към тебе, чадо мое.
30 Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
И Иосиф бързо се оттегли, защото сърцето му се развълнува за брат му; и като искаше да плаче, влезе в стаята си и плака там
31 Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
После уми лицето си и излезе и задържайки се рече: Сложете хляб.
32 Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
И сложиха отделно на него, отделно за тях и отделно за египтяните, които ядяха с него; защото не биваше египтяните да ядат хляб с евреите, понеже това е гнусота за египтяните.
33 Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
И насядаха пред него, първородният според първородството му, и най-младият според младостта му; и човеците се чудеха помежду си.
34 Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.
И Иосиф им пращаше от ястията си; а Вениаминовият дял беше пет пъти по-голям от дела на когото и да било от тях. И те пиха, пиха изобилно с него.

< Genesis 43 >