< Genesis 42 >

1 Yakobo atamva kuti ku Igupto kuli tirigu, anati kwa ana ake, “Nʼchifukwa chiyani mukungoyangʼanana wina ndi mnzake?
Gdy Jakub dowiedział się, że w Egipcie jest zboże, powiedział do swoich synów: Czemu się patrzycie jeden na drugiego?
2 Ine ndamva kuti ku Igupto kuli tirigu. Pitani kumeneko mukatigulireko kuti tisafe ndi njala.”
I mówił [im]: Oto słyszałem, że w Egipcie jest zboże. Jedźcie tam i kupcie [je] nam stamtąd, abyśmy żyli, a nie pomarli.
3 Choncho abale ake khumi a Yosefe anapita kukagula tirigu ku Igupto.
Dziesięciu braci Józefa wyruszyło więc do Egiptu, aby kupić zboże.
4 Koma Yakobo sanamulole Benjamini mngʼono wake wa Yosefe kuti apite nawo chifukwa anaopa kuti choyipa chingamuchitikire.
Ale Jakub nie posłał Beniamina, brata Józefa, z jego braćmi, bo powiedział: By nie spotkało go jakieś nieszczęście.
5 Choncho ana a Israeli aja anapita pamodzi ndi gulu la anzawo kukagula tirigu pakuti ku Kanaani kunalinso njala.
Synowie Izraela przybyli więc wraz z innymi, aby kupić [zboże], gdyż był głód w ziemi Kanaan.
6 Pakuti Yosefe anali nduna yayikulu yolamulira dziko la Igupto, ndiye kuti analinso amene ankagulitsa tirigu kwa anthu onse. Choncho abale ake a Yosefe nawonso anabwera, ndipo anamugwadira pansi.
A Józef był rządcą tej ziemi i to on sprzedawał [zboża] całej ludności tej ziemi. A gdy przyszli bracia Józefa, pokłonili mu się twarzą do ziemi.
7 Yosefe atangowaona abale ake anawazindikira, koma ananamizira kukhala ngati mlendo nawayankhula mwaukali kuwafunsa kuti, “Mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Ku dziko la Kanaani, tikudzagula chakudya.”
Gdy Józef ujrzał swych braci, poznał ich, lecz udawał przed nimi obcego i rozmawiał z nimi surowo. Zapytał ich: Skąd przyszliście? Odpowiedzieli: Z ziemi Kanaan, aby nakupić żywności.
8 Ngakhale Yosefe anawazindikira abale ake, koma iwo sanamuzindikire.
Józef rozpoznał swoich braci, ale oni go nie poznali.
9 Pamenepo anakumbukira maloto aja amene analota za iwo ndipo anati, “Inu ndinu akazitape! Mwabwera kudzazonda dziko lathu kuti muone pamene palibe chitetezo.”
I Józef przypomniał sobie sny, które mu się śniły o nich, i powiedział im: Jesteście szpiegami i przyszliście, aby wypatrzyć nieobronne miejsca tej ziemi.
10 Iwo anayankha, “Ayi mbuye wathu, antchito anufe tabwera kudzagula chakudya.
A [oni] mu odpowiedzieli: Nie, mój panie. Twoi słudzy przyszli, aby nakupić żywności.
11 Tonse ndife ana a munthu mmodzi. Ndife antchito anu okhulupirika osati akazitape.”
Wszyscy jesteśmy synami jednego człowieka. [Jesteśmy] uczciwi. Twoi słudzy nie są szpiegami.
12 Iye anawawuza kuti, “Ayi! Inu mwabwera kudzaona pamene palibe chitetezo mʼdziko muno.”
A [on] powiedział do nich: Nie, ale przyszliście wypatrzyć nieobronne miejsca tej ziemi.
13 Koma iwo anayankha, “Tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri. Abambo athu ndi mmodzi, ndipo kwathu ndi ku Kanaani. Panopo wotsiriza ali ndi abambo athu ndipo wina anamwalira.”
Powiedzieli: [Było] nas, twoich sług, dwunastu braci, synów jednego człowieka w ziemi Kanaan. Najmłodszy [jest] z naszym ojcem [w domu], a jednego już nie ma.
14 Yosefe anawawuza kuti, “Ndi momwe ndaneneramo: Inu ndinu akazitape.
Józef rzekł im: [Jest] tak, jak wam powiedziałem – jesteście szpiegami.
15 Ndiye ndikuyesani motere: Ine ndikulumbira pali Farao ndithu, inuyo simudzachoka malo ano mpaka wotsirizayo atabwera kuno.
Zostaniecie co do tego wybadani: Na życie faraona, nie wyjdziecie stąd, dopóki nie przyjdzie tu wasz młodszy brat.
16 Tumizani mmodzi wa inu akamutenge mʼbale wanuyo ndipo ena nonsenu musungidwa mʼndende, kuti titsimikize ngati zimene mukunenazi ndi zoona. Apo ayi, pali Farao ndithu, inu ndinu akazitape!”
Wyślijcie jednego z was, aby przyprowadził waszego brata, a wy zostaniecie w więzieniu, aż wasze słowa się potwierdzą, czy mówicie prawdę. A jeśli nie, na życie faraona, jesteście szpiegami.
17 Ndipo onse anawayika mʼndende kwa masiku atatu.
I oddał ich pod straż na trzy dni.
18 Pa tsiku lachitatu Yosefe anawawuza kuti, “Popeza ine ndimaopa Mulungu, ndipo inuyo ngati mukufuna kukhala ndi moyo muchite izi:
A trzeciego dnia Józef powiedział do nich: Zróbcie tak, a będziecie żyć, [bo] ja się boję Boga.
19 Ngati muli anthu achilungamo, mmodzi wa inu atsale mʼndende, pamene ena nonse mupite kwanu kuti muwatengere chakudya anthu akwanu kuli njalako.
Jeśli jesteście uczciwi, niech jeden z waszych braci pozostanie związany tu w więzieniu; a wy jedźcie i odnieście zboże, aby się pozbyć głodu z waszych domów.
20 Mukabwere naye kuno mngʼono wanu wotsirizayo kuti titsimikizire zimene munanena kuti musafe.” Ndipo anachita zomwezo.
I przyprowadźcie do mnie waszego najmłodszego brata, a wasze słowa sprawdzą się i nie umrzecie. I tak zrobili.
21 Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Ndithu ife tinalakwira mʼbale wathu uja popeza kuti ngakhale tinaona kuvutika kwake ndi kumva kulira kwake pamene ankatidandaulira kuti timuchitire chifundo, koma ife sitinamvere. Nʼchifukwa chake masautso awa atigwera.”
Mówili jeden do drugiego: Naprawdę zgrzeszyliśmy przeciwko naszemu bratu, bo widząc strapienie jego duszy, gdy nas błagał, nie wysłuchaliśmy go. Dlatego przyszło na nas to utrapienie.
22 Rubeni anayankha, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musamuchite kanthu mnyamata uja? Koma inu simunamvere! Tsopano tikulandira malipiro a magazi ake.”
Wtedy Ruben odpowiedział im: Czyż nie mówiłem wam: Nie grzeszcie przeciw chłopcu? A nie usłuchaliście. Oto teraz żąda się odpowiedzialności za jego krew.
23 Koma sanadziwe kuti Yosefe ankawamva popeza kuti ankagwiritsa ntchito wotanthauzira poyankhula naye.
Lecz oni nie wiedzieli, że Józef rozumie, bo rozmawiał z nimi przez tłumacza.
24 Yosefe anapita pambali payekha kukalira. Kenaka anabweranso nadzayankhula nawo. Iye anatenga Simeoni namumanga iwo akuona.
Wtedy odwrócił się od nich i zapłakał. Potem obrócił się do nich i rozmawiał z nimi. Wziął spośród nich Symeona i związał go na ich oczach.
25 Yosefe analamula kuti awadzazire matumba awo ndi tirigu, awayikiremo ndalama zawo momwemo ndiponso awapatse chakudya cha panjira. Izi anawachitiradi.
Potem Józef rozkazał, aby napełniono ich wory zbożem i każdemu z nich wrzucono do jego wora pieniądze, i [żeby] dano im żywność na drogę. I tak zrobiono.
26 Abale a Yosefe aja anasenzetsa abulu awo tirigu amene anagula uja ndipo ananyamuka ulendo wawo.
Wtedy oni włożyli zboża na swoje osły i odjechali stamtąd.
27 Atafika pamalo pena poti agone, mmodzi mwa iwo anatsekula thumba lake kuti atapemo chakudya cha bulu wake. Atangomasula anaona kuti ndalama zake zili pakamwa pa thumba.
I gdy [jeden z nich] rozwiązał swój wór, aby w gospodzie dać karmę swemu osłu, zobaczył swoje pieniądze; były bowiem na wierzchu jego wora.
28 Iye anati kwa abale akewo, “Ndalama zanga andibwezera, izi zili mʼthumba mwangamu.” Mitima yawo inachita ngati yachokamo ndipo anali ndi mantha ambiri, nati, “Ndi chiyani chimene Mulungu watichitira?”
I powiedział do swoich braci: Zwrócono mi pieniądze, oto są w moim worze. Wtedy zamarło im serce i przerazili się, mówiąc jeden do drugiego: Cóż to nam Bóg uczynił?
29 Atafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani anafotokoza zonse zimene zinawachitikira nati,
Potem przyszli do swego ojca Jakuba, do ziemi Kanaan, i opowiedzieli mu wszystko, co im się przydarzyło:
30 “Nduna yayikulu ya mʼdzikomo inatiyankhula mwa ukali kwambiri ndipo inkatiyesa kuti ndife akazitape.
Ten człowiek, pan tej ziemi, rozmawiał z nami surowo i wziął nas za szpiegów ziemi;
31 Koma tinamuwuza kuti, ‘Ndife anthu woona mtima osati akazitape.
Powiedzieliśmy mu: Jesteśmy uczciwi, nie jesteśmy szpiegami;
32 Ife tonse tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri, abambo mmodzi. Mmodzi anamwalira, ndipo wamngʼono ali ndi abambo athu ku Kanaani.’”
Było nas dwunastu braci, synów naszego ojca; jednego już nie ma, a najmłodszy [jest] teraz z naszym ojcem w ziemi Kanaan.
33 Ndipo nduna ija inati kwa ife, “Kuti ndidziwedi kuti ndinu anthu owona mtima muchite izi: Mmodzi mwa inu atsale ndi ine kuno, ndipo enanu mutenge chakudya ndi kubwerera kwanu kumene kuli njalako.
I ten człowiek, pan tej ziemi, powiedział do nas: Po tym poznam, że jesteście uczciwi; zostawcie jednego z waszych braci u mnie, weźcie zboże, aby pozbyć się głodu z waszych domów, i idźcie;
34 Koma mundibweretsere wotsirizayo kuti ndidziwedi kuti sindinu akazitape koma anthu achilungamo. Kenaka ndidzakubwezerani mʼbale wanuyu ndipo mukhoza kuchita malonda mʼdzikoli.”
Potem przyprowadźcie waszego najmłodszego brata do mnie, abym poznał, że nie jesteście szpiegami, ale [ludźmi] uczciwymi. Wtedy oddam wam waszego brata, a w tej ziemi będziecie mogli handlować.
35 Pamene amakhuthula matumba awo a tirigu aliyense anapeza kuti kathumba kake ka ndalama kali momwemo. Ataona zimenezi, iwo pamodzi ndi abambo awo anachita mantha kwambiri.
A gdy opróżniali swoje wory, każdy [znalazł] w swoim worze węzeł pieniędzy. Gdy wraz ze swoim ojcem zobaczyli węzły z pieniędzmi, przerazili się.
36 Abambo awo Yakobo anawawuza kuti, “Mwandilanda ana anga ine. Yosefe anamwalira ndipo Simeoni palibenso, ndiye tsopano mukufuna mutengenso Benjamini. Zonsezi zandigwera ine!”
Wtedy ich ojciec Jakub powiedział im: Osierociliście mnie. Nie ma Józefa i Symeona, a weźmiecie Beniamina; całe [zło] się na mnie zwaliło.
37 Koma Rubeni anati kwa abambo ake, “Ngati sindidzabwera naye kwa inu, mudzaphe ana anga aamuna awiri. Muperekeni mʼmanja mwangamu ndipo ndidzamusamala ndi kubwera naye kwa inu.”
Ruben powiedział do swego ojca: Zabij moich dwóch synów, jeśli go z powrotem nie przyprowadzę. Oddaj go pod moją opiekę, a ja ci go zwrócę.
38 Koma Yakobo anati, “Mwana wanga sapita nanu kumeneko; mkulu wake anamwalira ndipo watsala yekha. Ngati choyipa chitamuchitikira pa ulendo mukupitawu, ndiye kuti ndi mmene ndakalambiramu inu mudzandipha ndi chisoni chotere.” (Sheol h7585)
Ale on powiedział: Mój syn nie pójdzie z wami, gdyż jego brat umarł i tylko on jeden został. Jeśli przydarzy mu się nieszczęście na drodze, którą pójdziecie, w żalu doprowadzicie mnie, osiwiałego, do grobu. (Sheol h7585)

< Genesis 42 >