< Genesis 42 >

1 Yakobo atamva kuti ku Igupto kuli tirigu, anati kwa ana ake, “Nʼchifukwa chiyani mukungoyangʼanana wina ndi mnzake?
Da Jakob hørte, at der var Korn at få i Ægypten, sagde han til sine Sønner: "Hvad venter I efter?"
2 Ine ndamva kuti ku Igupto kuli tirigu. Pitani kumeneko mukatigulireko kuti tisafe ndi njala.”
Og han sagde: "Jeg hører, at der er Korn at få i Ægypten; drag ned og køb os noget, at vi kan blive i Live og undgå Døden!"
3 Choncho abale ake khumi a Yosefe anapita kukagula tirigu ku Igupto.
Så drog de ti af Josefs Brødre ned for at købe Korn i Ægypten;
4 Koma Yakobo sanamulole Benjamini mngʼono wake wa Yosefe kuti apite nawo chifukwa anaopa kuti choyipa chingamuchitikire.
men Jakob sendte ikke Josefs Broder Benjamin med hans Brødre, thi han tænkte, der kunde tilstøde ham en Ulykke.
5 Choncho ana a Israeli aja anapita pamodzi ndi gulu la anzawo kukagula tirigu pakuti ku Kanaani kunalinso njala.
Blandt dem, der kom for at købe Korn, var også Israels Sønner; thi der var Hungersnød i Kana'ans Land.
6 Pakuti Yosefe anali nduna yayikulu yolamulira dziko la Igupto, ndiye kuti analinso amene ankagulitsa tirigu kwa anthu onse. Choncho abale ake a Yosefe nawonso anabwera, ndipo anamugwadira pansi.
Og da Josef var Hersker i Landet, og han var den, der solgte Korn til alt Folket i Landet, så kom Josefs Brødre og kastede sig til Jorden for ham.
7 Yosefe atangowaona abale ake anawazindikira, koma ananamizira kukhala ngati mlendo nawayankhula mwaukali kuwafunsa kuti, “Mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Ku dziko la Kanaani, tikudzagula chakudya.”
Da Josef så sine Brødre, kendte han dem; men han lod fremmed over for dem, talte dem hårdt til og sagde til dem: "Hvorfra kommer I?" De svarede: "Fra Kana'ans Land for at købe Føde!"
8 Ngakhale Yosefe anawazindikira abale ake, koma iwo sanamuzindikire.
Josef kendte sine Brødre, men de kendte ikke ham.
9 Pamenepo anakumbukira maloto aja amene analota za iwo ndipo anati, “Inu ndinu akazitape! Mwabwera kudzazonda dziko lathu kuti muone pamene palibe chitetezo.”
Da kom Josef de Drømme i Hu. han havde drømt om dem; og han sagde til dem; "I er Spejdere, I kommer for at se, hvor Landet er åbent!"
10 Iwo anayankha, “Ayi mbuye wathu, antchito anufe tabwera kudzagula chakudya.
De svarede: "Nej, Herre, dine Trælle kommer for at købe Føde!
11 Tonse ndife ana a munthu mmodzi. Ndife antchito anu okhulupirika osati akazitape.”
Vi er alle Sønner af en og samme Mand; vi er ærlige Folk. dine Trælle er ikke Spejdere!"
12 Iye anawawuza kuti, “Ayi! Inu mwabwera kudzaona pamene palibe chitetezo mʼdziko muno.”
Men han sagde: "Jo vist så! I kommer for at se, hvor Landet er åbent!"
13 Koma iwo anayankha, “Tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri. Abambo athu ndi mmodzi, ndipo kwathu ndi ku Kanaani. Panopo wotsiriza ali ndi abambo athu ndipo wina anamwalira.”
De svarede: "Vi, dine Trælle. var tolv Brødre, Sønner af en og samme Mand i Kana'ans Land; den yngste er for Tiden hjemme hos vor Fader, og een er ikke mere!"
14 Yosefe anawawuza kuti, “Ndi momwe ndaneneramo: Inu ndinu akazitape.
Men Josef sagde til dem: "Det er, som jeg siger eder: I er Spejdere!
15 Ndiye ndikuyesani motere: Ine ndikulumbira pali Farao ndithu, inuyo simudzachoka malo ano mpaka wotsirizayo atabwera kuno.
Men nu skal I sættes på Prøve: Så sandt Farao lever, slipper I ikke herfra, uden at eders yngste Broder kommer hid!
16 Tumizani mmodzi wa inu akamutenge mʼbale wanuyo ndipo ena nonsenu musungidwa mʼndende, kuti titsimikize ngati zimene mukunenazi ndi zoona. Apo ayi, pali Farao ndithu, inu ndinu akazitape!”
Lad en af eder rejse hjem for at hente eders Broder, og imedens holdes I andre fangne; så vil det. vise sig, om eders Ord er Sandhed; og hvis ikke, så er I, så sandt, Farao lever, Spejdere!"
17 Ndipo onse anawayika mʼndende kwa masiku atatu.
Derpå holdt han dem i Forvaring tre Dage.
18 Pa tsiku lachitatu Yosefe anawawuza kuti, “Popeza ine ndimaopa Mulungu, ndipo inuyo ngati mukufuna kukhala ndi moyo muchite izi:
Men Tredjedagen sagde Josef til dem: "Vil I beholde Livet, så skal I gøre således, thi jeg er en Mand, der frygter Gud:
19 Ngati muli anthu achilungamo, mmodzi wa inu atsale mʼndende, pamene ena nonse mupite kwanu kuti muwatengere chakudya anthu akwanu kuli njalako.
Er I virkelig ærlige Folk, lad så en af eder blive tilbage som Fange i det Fængsel, som I sad i, medens I andre drager hjem med Korn til at stille Hungeren i eders Huse;
20 Mukabwere naye kuno mngʼono wanu wotsirizayo kuti titsimikizire zimene munanena kuti musafe.” Ndipo anachita zomwezo.
og bring så eders yngste Broder til mig, så skal eders Ord stå til Troende, og I skal slippe for at dø!" Og således gjorde de.
21 Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Ndithu ife tinalakwira mʼbale wathu uja popeza kuti ngakhale tinaona kuvutika kwake ndi kumva kulira kwake pamene ankatidandaulira kuti timuchitire chifundo, koma ife sitinamvere. Nʼchifukwa chake masautso awa atigwera.”
Da sagde de til hverandre: "Sandelig, nu må vi bøde for, hvad vi forbrød mod vor Broder, da vi så hans Sjælevånde, medens han bønfaldt os, og dog ikke hørte ham; derfor stedes vi nu i denne Vånde!"
22 Rubeni anayankha, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musamuchite kanthu mnyamata uja? Koma inu simunamvere! Tsopano tikulandira malipiro a magazi ake.”
Men Ruben tog til Orde og sagde til dem: "Sagde jeg eder ikke dengang: Forsynd eder ikke mod Drengen! Men I vilde ikke høre; se, nu kræves hans Blod!"
23 Koma sanadziwe kuti Yosefe ankawamva popeza kuti ankagwiritsa ntchito wotanthauzira poyankhula naye.
Således talte de. Men de vidste ikke, at Josef forstod det, thi han forhandlede med dem ved Tolk;
24 Yosefe anapita pambali payekha kukalira. Kenaka anabweranso nadzayankhula nawo. Iye anatenga Simeoni namumanga iwo akuona.
og han vendte sig bort fra dem og græd. Siden vendte han sig til dem og talte med dem; og han tog Simeon fra dem og lod ham fængsle for deres Øjne.
25 Yosefe analamula kuti awadzazire matumba awo ndi tirigu, awayikiremo ndalama zawo momwemo ndiponso awapatse chakudya cha panjira. Izi anawachitiradi.
Så gav Josef Befaling til at fylde deres Sække med Korn og lægge Pengene tilbage i hver enkelts Sæk og give dem Rejsekost; og således skete det.
26 Abale a Yosefe aja anasenzetsa abulu awo tirigu amene anagula uja ndipo ananyamuka ulendo wawo.
Så læssede de deres Korn på Æslerne og drog bort.
27 Atafika pamalo pena poti agone, mmodzi mwa iwo anatsekula thumba lake kuti atapemo chakudya cha bulu wake. Atangomasula anaona kuti ndalama zake zili pakamwa pa thumba.
Men da en af dem i Natteherberget åbnede sin Sæk for at give sit Æsel Foder, fik han Øje på sine Penge, der lå oven i Sækken;
28 Iye anati kwa abale akewo, “Ndalama zanga andibwezera, izi zili mʼthumba mwangamu.” Mitima yawo inachita ngati yachokamo ndipo anali ndi mantha ambiri, nati, “Ndi chiyani chimene Mulungu watichitira?”
og han sagde til sine Brødre: "Mine Penge er kommet igen; se, de er i min Sæk!" Da sank Hjertet i Livet på dem, og de så forfærdede på hverandre og sagde: "Hvad har Gud dog gjort imod os!"
29 Atafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani anafotokoza zonse zimene zinawachitikira nati,
Og da de kom hjem til deres Fader Jakob i Kana'ans Land, fortalte de ham alt, hvad der var hændet dem, og sagde:
30 “Nduna yayikulu ya mʼdzikomo inatiyankhula mwa ukali kwambiri ndipo inkatiyesa kuti ndife akazitape.
"Manden, der er Landets Herre, talte os hårdt til og holdt os i Forvaring, som var vi Folk, der vilde udspejde Landet;
31 Koma tinamuwuza kuti, ‘Ndife anthu woona mtima osati akazitape.
men vi sagde til ham: Vi er ærlige Folk og ikke Spejdere;
32 Ife tonse tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri, abambo mmodzi. Mmodzi anamwalira, ndipo wamngʼono ali ndi abambo athu ku Kanaani.’”
vi var tolv Brødre, Sønner af en og samme Fader; een er ikke mere, og den yngste er for Tiden hjemme hos vor Fader i Kana'ans Land.
33 Ndipo nduna ija inati kwa ife, “Kuti ndidziwedi kuti ndinu anthu owona mtima muchite izi: Mmodzi mwa inu atsale ndi ine kuno, ndipo enanu mutenge chakudya ndi kubwerera kwanu kumene kuli njalako.
Så sagde Manden, der er Landets Herre: Derpå vil jeg kende, at I er ærlige Folk: Lad en af eder blive hos mig, og tag I andre Korn til at stille Hungeren i eders Huse og drag hjem!
34 Koma mundibweretsere wotsirizayo kuti ndidziwedi kuti sindinu akazitape koma anthu achilungamo. Kenaka ndidzakubwezerani mʼbale wanuyu ndipo mukhoza kuchita malonda mʼdzikoli.”
Siden skal I bringe eders yngste Broder til mig, for at jeg kan kende, at I ikke er Spejdere, men ærlige Folk; så vil jeg udlevere eders Broder til eder, og I kan frit rejse i Landet."
35 Pamene amakhuthula matumba awo a tirigu aliyense anapeza kuti kathumba kake ka ndalama kali momwemo. Ataona zimenezi, iwo pamodzi ndi abambo awo anachita mantha kwambiri.
Da de nu tømte deres Sække, fandt hver sin Pengepose i sin Sæk; og da de og deres Fader så Pengeposerne, blev de forfærdede.
36 Abambo awo Yakobo anawawuza kuti, “Mwandilanda ana anga ine. Yosefe anamwalira ndipo Simeoni palibenso, ndiye tsopano mukufuna mutengenso Benjamini. Zonsezi zandigwera ine!”
Og deres Fader Jakob sagde til dem: "I gør mig barnløs; Josef er ikke mere, og Simeon er ikke mere, og nu vil I tage Benjamin; det går alt sammen ud over mig!"
37 Koma Rubeni anati kwa abambo ake, “Ngati sindidzabwera naye kwa inu, mudzaphe ana anga aamuna awiri. Muperekeni mʼmanja mwangamu ndipo ndidzamusamala ndi kubwera naye kwa inu.”
Så sagde Ruben til sin Fader: "Du må tage mine to Sønners Liv, hvis jeg ikke bringer ham til dig; betro ham til mig, og jeg skal bringe ham tilbage til dig!"
38 Koma Yakobo anati, “Mwana wanga sapita nanu kumeneko; mkulu wake anamwalira ndipo watsala yekha. Ngati choyipa chitamuchitikira pa ulendo mukupitawu, ndiye kuti ndi mmene ndakalambiramu inu mudzandipha ndi chisoni chotere.” (Sheol h7585)
Men han sagde: "Min Søn skal ikke rejse derned med eder, thi hans Broder er død, og han alene er tilbage; tilstøder der ham en Ulykke på den Rejse, I har for, så bringer I mine grå Hår ned i Dødsriget med Sorg!" (Sheol h7585)

< Genesis 42 >