< Genesis 41 >

1 Patapita zaka ziwiri zathunthu, Farao analota atayimirira mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo,
Kwasekusithi ekupheleni kweminyaka emibili egcweleyo uFaro waphupha; khangela-ke, emi emfuleni.
2 ndipo anangoona ngʼombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zooneka bwino ndi zonenepa zikutuluka mu mtsinje muja ndi kuyamba kudya msipu wa mu mawango.
Khangela-ke, emfuleni kwakhuphuka amankomokazi ayisikhombisa, ekhangeleka emahle, enonile enyameni; adla emihlangeni.
3 Kenaka ngʼombe zina zazikazi zisanu ndi ziwiri zosaoneka bwino ndi zowonda zinatulukanso mu mtsinje wa Nailo ndipo zinayimirira pambali pa zina zija zimene zinali mʼmphepete mwa mtsinje uja.
Khangela-ke, amanye amankomokazi ayisikhombisa akhuphuka emfuleni emva kwawo, ekhangeleka kubi, ecakile enyameni; ema eduze lamankomokazi ekhunjini lomfula.
4 Ndipo ngʼombe zosaoneka bwino ndi zowonda zija zinadya ngʼombe zonenepa zija. Kenaka Farao anadzidzimuka.
Amankomokazi akhangeleka kubi acakileyo enyameni adla amankomokazi akhangeleka kuhle anonileyo. UFaro wasephaphama.
5 Posakhalitsa anagonanso ndipo analota kachiwiri: Analota ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zathanzi labwino zitabala pa phata limodzi.
Walala futhi, waphupha ngokwesibili; khangela-ke, kwakhahlela izikhwebu eziyisikhombisa ehlangeni linye, ezigcweleyo zilungile.
6 Kenaka ngala zina zisanu ndi ziwiri zinaphuka. Izi zinali zowonda ndi zowauka ndi mphepo ya kummawa.
Khangela-ke, izikhwebu eziyisikhombisa ezicakileyo, zihangulwe ngumoya wempumalanga, zakhahlela emva kwazo.
7 Ngala zowonda zija zinameza ngala zathanzi ndi zonenepa zija. Farao anadzidzimuka ndipo anaona kuti anali maloto chabe.
Izikhwebu ezicakileyo zaginya izikhwebu ezipheleleyo ezigcweleyo. UFaro wasephaphama, khangela-ke, kwakuliphupho.
8 Mmawa, Farao anavutika mu mtima kotero anayitanitsa amatsenga ndi anzeru onse a mu Igupto. Iwo atabwera, iye anawawuza maloto ake, koma panalibe ndi mmodzi yemwe amene anatha kutanthauzira malotowo kwa Farao.
Kwasekusithi ekuseni umoya wakhe wakhathazeka; wathumela wabiza izangoma zonke zeGibhithe lazo zonke izazi zayo. UFaro wazilandisela iphupho lakhe; kodwa kwakungekho ongamchasisela wona uFaro.
9 Ndipo mkulu wa operekera zakumwa anati kwa Farao, “Lero ndakumbukira kulephera kwanga.
Induna yabaphathinkezo yasikhuluma kuFaro isithi: Lamuhla ngiyakhumbula amacala ami.
10 Paja nthawi ina Farao anapsera mtima antchito akefe, ndipo anatitsekera (ine ndi mkulu wa ophika buledi) mʼndende, mʼnyumba ya mkulu wa alonda.
UFaro wazithukuthelela inceku zakhe, wanginikela esitokisini, endlini yenduna yabalindi, mina lenduna yabaphekizinkwa;
11 Tsiku lina tonse awiri tinalota maloto, ndipo loto lililonse linali ndi tanthauzo lake.
njalo saphupha iphupho ngabusuku bunye, mina layo. Saphupha, ngamunye njengengcazelo yephupho lakhe.
12 Tsono momwemo munali mnyamata wina Wachihebri, wantchito wa mkulu wa alonda. Ife tinamufotokozera maloto athu, ndipo anatitanthauzira malotowo. Munthu aliyense anamupatsa tanthauzo la loto lake.
Kwakukhona lapho kanye lathi ijaha umHebheru, inceku yenduna yabalindi; sayilandisela yasichasisela amaphupho ethu, yachasisa ngamunye njengephupho lakhe.
13 Ndipo zinthu zinachitikadi monga mmene anatitanthauzira. Ine anandibwezera pa ntchito yanga ndipo winayo anapachikidwa.”
Kwasekusithi njengokusichasisela kwayo kwaba njalo; mina wangibuyisela esikhundleni sami, yena wamlengisa.
14 Choncho Farao anamuyitanitsa Yosefe, ndipo mofulumira anabwera naye kuchokera mʼdzenje muja. Ndipo atameta, ndi kusintha zovala, anapita kwa Farao.
UFaro wasethumela wabiza uJosefa; bamkhupha emgodini ngokuphangisa; esephucile wafaka ezinye izigqoko, wangena kuFaro.
15 Farao anati kwa Yosefe, “Ndinalota maloto ndipo palibe amene watha kunditanthauzira. Tsono ndawuzidwa kuti iwe ukamva loto umadziwanso kulimasulira.”
UFaro wasesithi kuJosefa: Ngiphuphile iphupho, kodwa kakho olichasisayo; njalo mina ngizwile ngawe ukuthi: Usizwa iphupho, uyalichasisa.
16 Yosefe anamuyankha Farao kuti, “Sindingathe koma Mulungu apereka yankho limene Farao akufuna.”
UJosefa wasemphendula uFaro esithi: Kakukho kimi. UNkulunkulu uzaphendula impilakahle kaFaro.
17 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, “Ndinalota nditayimirira mʼmphepete mwa mtsinje wa Nailo,
UFaro wasekhuluma kuJosefa wathi: Ephutsheni lami, khangela, ngangimi ekhunjini lomfula;
18 ndipo ngʼombe zisanu ndi ziwiri zonenepa ndi zooneka bwino zinatuluka mu mtsinje muja ndi kumadya msipu wa mu mawango.
njalo khangela, kwakhuphuka emfuleni amankomokazi ayisikhombisa, anonileyo enyameni, akhangeleka emahle, adla emihlangeni.
19 Kenaka, ngʼombe zina zisanu ndi ziwiri zinatuluka. Izi zinali zosaoneka bwino ndiponso zowonda ndipo sindinaonepo ngʼombe zosaoneka bwino chonchi mʼdziko lonse la Igupto.
Khangela-ke, amanye amankomokazi ayisikhombisa akhuphuka emva kwawo, ayangekileyo, akhangeleka emabi kakhulu, acakileyo enyameni; angizanga ngiwabone anjengawo ngobubi elizweni lonke leGibhithe.
20 Ngʼombe zosaoneka bwino ndi zowonda zija zinadya zisanu ndi ziwiri zonenepa zimene zinatuluka poyamba zija.
Kwathi amankomokazi acakileyo lamabi adla amankomokazi ayisikhombisa okuqala anonileyo.
21 Koma ngakhale ngʼombezi zinadya zinazo, palibe amene akanatha kuzindikira kuti zinatero popeza zinali zosaonekabe bwino monga poyamba. Ndipo ndinadzidzimuka.
Lapho esengene esiswini sawo, kakubonakalanga ukuthi angenile esiswini sawo, ngoba ekhangeleka kubi njengakuqala. Ngasengiphaphama.
22 “Nditagonanso kachiwiri, ndinalota ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zathanzi ndi zonenepa zitabala pa phata limodzi.
Ngasengibona ephutsheni lami, khangela-ke, izikhwebu eziyisikhombisa zikhahlela ehlangeni linye, zigcwele zilungile;
23 Kenaka panaphukanso ngala zina zisanu ndi ziwiri zofota, zowonda ndi zowauka ndi mphepo ya kummawa.
njalo khangela, izikhwebu eziyisikhombisa ezitshwabheneyo, ezicakileyo, ezihangulwe ngumoya wempumalanga zakhahlela emva kwazo.
24 Ngala zowondazo zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zabwino zija. Ndinawawuza amatsenga koma palibe ndi mmodzi yemwe anatha kundimasulira.”
Njalo izikhwebu ezicakileyo zaginya izikhwebu eziyisikhombisa ezilungileyo. Njalo ngakulandisela izangoma; kodwa kwakungekho esangichasiselayo.
25 Ndipo Yosefe anati kwa Farao, “Maloto awiriwa ndi ofanana ndipo ali ndi tanthauzo limodzi. Mulungu waululira Farao chimene atachite.
UJosefa wasesithi kuFaro: Iphupho likaFaro linye. Lokho uNkulunkulu akwenzayo, umazisile uFaro.
26 Ngʼombe zisanu ndi ziwiri zabwinozo ndi zaka zisanu ndi ziwiri. Ndipo ngala zisanu ndi ziwiri zabwinozo ndi zaka zisanu ndi ziwiri. Kutanthauza kwa maloto nʼkumodzi.
Amankomokazi ayisikhombisa alungileyo ayiminyaka eyisikhombisa; lezikhwebu eziyisikhombisa ezilungileyo ziyiminyaka eyisikhombisa. Iphupho linye.
27 Ngʼombe zisanu ndi ziwiri zowonda ndi zosaoneka bwino zimene zinatuluka pambuyozo ndiponso ngala zisanu ndi ziwiri zachabechabe, zowauka ndi mphepo ya kummawa zija ndi zaka zisanu ndi ziwiri za njala.
Njalo amankomokazi acakileyo lamabi akhuphuka emva kwawo ayiminyaka eyisikhombisa; lezikhwebu eziyisikhombisa ezicakileyo ezihangulwe ngumoya wempumalanga zizakuba yiminyaka eyisikhombisa yendlala.
28 “Tsono ndi monga ndafotokozeramu kuti Mulungu wakuwuziranitu zimene adzachite.
Le yinto engiyikhulume kuFaro ukuthi: Lokho uNkulunkulu akwenzayo, ukutshengisile kuFaro.
29 Zaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zochuluka zikubwera mu dziko lonse la Igupto,
Khangela, kuyeza iminyaka eyisikhombisa yenala enkulu elizweni lonke leGibhithe.
30 koma zidzatsatana ndi zaka zina zisanu ndi ziwiri za njala. Chakudya chochuluka cha mu Igupto chija chidzayiwalika ndipo njalayo idzawononga dziko.
Kuzavela iminyaka eyisikhombisa yendlala emva kwayo; izakhohlakala-ke inala yonke elizweni leGibhithe; njalo indlala izaliqeda ilizwe.
31 Zakudya zochuluka za mʼdzikomo zija sizidzakumbukirikanso chifukwa njala imene iti idzabwereyo idzakhala yoopsa.
Njalo inala kayiyikwaziwa elizweni ngenxa yaleyondlala emva kwalokho, ngoba izakuba nzima kakhulu.
32 Popeza kuti malotowa aperekedwa kwa inu Mfumu kawiri, ndiye kuti Mulungu watsimikiza kuti adzachitadi zimenezi posachedwapa.
Njalo ukuthi iphupho liphindwe kabili kuFaro, kungoba into le imisiwe nguNkulunkulu, futhi uNkulunkulu uyaphangisa ukukwenza.
33 “Tsopano Farao apezeretu munthu wozindikira ndi wanzeru ndipo amuyike kukhala woyangʼanira dziko lonse la Igupto.
Khathesi-ke uFaro kakhangele indoda eqedisisayo lehlakaniphileyo, ayibeke phezu kwelizwe leGibhithe.
34 Asankhenso akuluakulu a mʼdziko lino. Iwowa azitenga ndi kuyika padera limodzi la magawo asanu aliwonse a zokolola za mʼdziko muno mu zaka zonse zisanu ndi ziwiri za chakudya chochuluka.
UFaro kenze lokhu, abeke ababonisi phezu kwelizwe, athathe ingxenye yesihlanu yelizwe leGibhithe eminyakeni eyisikhombisa yenala.
35 Iwo asonkhanitse zakudya zonse za mʼzaka zabwino zikubwerazi. Pansi pa ulamuliro wa Farao, akuluakuluwo asonkhanitse ndi kusunga bwino tirigu mʼmizinda yonse.
Kababuthe konke ukudla kwaliminyaka elungileyo ezayo, njalo kababuthelele amabele ngaphansi kwesandla sikaFaro, kube yikudla emizini, bawagcine.
36 Chakudya chimenechi chisungidwe kuti chidzagwiritsidwe ntchito mʼzaka zisanu ndi ziwiri za njala imene ikubwerayo mu Igupto, kuti anthu a mʼdzikoli asadzafe ndi njalayo.”
Njalo ukudla kuzakuba yisiphala selizwe okweminyaka eyisikhombisa yendlala ezakuba khona elizweni leGibhithe, ukuze ilizwe lingabhujiswa yindlala.
37 Farao ndi nduna zake anagwirizana nawo malangizo a Yosefe.
Njalo into le yabanhle emehlweni kaFaro lemehlweni ezinceku zakhe zonke.
38 Choncho Farao anafunsa nduna zake nati, “Kodi tingathe kumupeza munthu wina ngati uyu, amene ali ndi mzimu wa Mulungu?”
UFaro wasesithi ezincekwini zakhe: Singamthola yini onjengaye, indoda okuyo uMoya kaNkulunkulu?
39 Farao anati kwa Yosefe, “Pakuti Mulungu wakudziwitsa iwe zonsezi, palibe wina wodziwa zinthu ndi wanzeru ngati iwe.
UFaro wasesithi kuJosefa: Njengalokhu uNkulunkulu ekwazisile konke lokhu, kakho oqedisisayo lohlakaniphileyo njengawe.
40 Iwe ukhala nduna yayikulu mu dziko langa ndipo anthu onse adzamvera zimene walamula. Ine ndekha ndiye amene ndidzakuposa mphamvu chifukwa ndimakhala pa mpando waufumu.”
Wena uzakuba phezu kwendlu yami, njalo emlonyeni wakho bonke abantu bami bazabuswa; kuphela esihlalweni sobukhosi ngizakuba mkhulu kulawe.
41 Choncho Farao anati kwa Yosefe, “Ine ndikukuyika iwe kukhala nduna yoyangʼanira dziko lonse la Igupto.”
UFaro wasesithi kuJosefa: Khangela, ngikubekile phezu kwelizwe lonke leGibhithe.
42 Ndipo Farao anavula mphete ku chala chake nayiveka ku chala cha Yosefe. Anamuvekanso mkanjo wonyezimira ndi nkufu wagolide mʼkhosi mwake.
UFaro wasekhupha indandatho yakhe elophawu lwakhe esandleni sakhe, wayifaka esandleni sikaJosefa, wamgqokisa izigqoko zelembu elicolekileyo kakhulu, wamgaxa iketane legolide entanyeni yakhe.
43 Anamukweza Yosefe pa galeta ngati wachiwiri pa ulamuliro. Ndipo anthu anafuwula pamaso pake nati, “Mʼgwadireni!” Motero anakhala nduna yayikulu ya dziko lonse la Igupto.
Wamhambisa enqoleni yesibili ayelayo; njalo bamemeza phambi kwakhe besithi: Guqani! Ngokunjalo wambeka phezu kwelizwe lonke leGibhithe.
44 Kenaka Farao anati kwa Yosefe, “Ine ndine Farao; tsono iwe ukapanda kulamula, palibe amene akhoza kuchita chilichonse ngakhale kuyenda kumene mʼdziko lonse la Igupto.”
UFaro wasesithi kuJosefa: NginguFaro; kodwa ngaphandle kwakho kakho ozaphakamisa isandla sakhe loba unyawo lwakhe elizweni lonke leGibhithe.
45 Farao anamupatsa Yosefe dzina lakuti Zafenati-Panea ndipo anamupatsanso Asenati mwana wa mkazi wa Potifara, wansembe wa Oni, kuti akhale mkazi wake. Choncho Yosefe anayendera dziko lonse la Igupto.
UFaro wasebiza ibizo likaJosefa ngokuthi uZafenathi-Paneya. Wamnika uAsenathi, indodakazi kaPotifera umpristi weOni, ukuthi abe ngumkakhe. UJosefa wasephuma wadabula elizweni leGibhithe.
46 Yosefe anali ndi zaka 30 pamene amayamba ntchito kwa Farao, mfumu ya ku Igupto. Ndipo Yosefe anachoka pa maso pa Farao nayendera dziko lonse la Igupto.
Njalo uJosefa wayeleminyaka engamatshumi amathathu mhla esima phambi kukaFaro inkosi yeGibhithe. UJosefa wasephuma esuka ebusweni bukaFaro, wadabula ilizwe lonke leGibhithe.
47 Mʼzaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zambiri zija, anthu mʼdzikomo anakolola zochuluka.
Umhlaba wathela ngezandla ezigcweleyo eminyakeni eyisikhombisa yenala.
48 Yosefe anasonkhanitsa zakudya zonse zokololedwa mʼzaka zisanu ndi ziwiri zija ndipo anazisunga mʼmizinda. Mu mzinda uliwonse anayikamo chakudya chimene chinalimidwa mʼminda yozungulira komweko.
Waseqoqa konke ukudla kweminyaka eyisikhombisa eyayiselizweni leGibhithe, wabeka ukudla emizini; ukudla kwensimu ezingelezele lowo lalowomuzi wakubeka kuwo.
49 Yosefe anasunga tirigu wochuluka kwambiri ngati mchenga wa ku nyanja. Kunali tirigu wochuluka kwambiri motero kuti analeka nʼkulembera komwe.
UJosefa wasebuthelela amabele njengetshebetshebe lolwandle, aba manengi kakhulu, waze wayekela ukubala, ngoba ayengelanani.
50 Zisanafike zaka zanjala, Yosefe anabereka ana aamuna awiri mwa Asenati mwana wa mkazi wa Potifara, wansembe wa Oni.
Wasezalelwa uJosefa amadodana amabili, ungakafiki umnyaka wendlala, amzalela wona uAsenathi indodakazi kaPotifera umpristi weOni.
51 Yosefe anamutcha mwana wake woyamba, Manase popeza anati, “Mulungu wandiyiwalitsa zovuta zanga zija ndiponso banja la abambo anga.”
UJosefa wasebiza ibizo lezibulo wathi nguManase, wathi: Ngoba uNkulunkulu ungenze ukuthi ngikhohlwe konke ukuhlupheka kwami lendlu yonke kababa.
52 Mwana wachiwiri wa mwamuna anamutcha Efereimu popeza anati, “Mulungu wandipatsa ana mʼdziko la masautso anga.”
Lebizo leyesibili walibiza wathi nguEfrayimi, wathi: Ngoba uNkulunkulu ungenze ukuthi ngibe lezithelo elizweni lokuhlupheka kwami.
53 Zaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zochuluka zija zinatha,
Kwasekuphela iminyaka eyisikhombisa yenala eyayiselizweni leGibhithe.
54 ndipo zaka zisanu ndi ziwiri za njala zija zinayamba monga ananenera Yosefe. Njalayi inafika ku mayiko ena onse koma ku dziko lonse la Igupto kunali chakudya.
Kwasekuqala ukufika iminyaka eyisikhombisa yendlala, njengoba uJosefa wayetshilo. Kwasekusiba khona indlala emazweni wonke, kodwa elizweni lonke leGibhithe kwakukhona isinkwa.
55 Pamene njala ija inakwanira dziko lonse la Igupto anthu analilira Farao kuti awapatse chakudya. Koma Farao anawawuza kuti, “Pitani kwa Yosefe ndipo mukachite zimene akakuwuzeni.”
Kwathi ilizwe leGibhithe lonke selilamba, abantu bakhala ngesinkwa kuFaro. UFaro wasesithi kuwo wonke amaGibhithe: Yanini kuJosefa, lenze lokho alitshela khona.
56 Pamene njala inafalikira dziko lonse, Yosefe anatsekula nkhokwe za zakudya namagulitsa tirigu kwa anthu a ku Igupto aja, pakuti njala inafika poyipa kwambiri mu Igupto monse.
Kwathi sekulendlala ebusweni belizwe lonke, uJosefa wavula zonke iziphala, wathengisela amaGibhithe; indlala-ke yaba lamandla elizweni leGibhithe.
57 Anthu ankabwera ku Igupto kuchokera ku mayiko ena onse kudzagula tirigu kwa Yosefe, chifukwa njala inafika poyipa kwambiri pa dziko lonse lapansi.
Lonke ilizwe lafika eGibhithe kuJosefa ukuthenga, ngoba indlala yayilamandla emhlabeni wonke.

< Genesis 41 >