< Genesis 41 >

1 Patapita zaka ziwiri zathunthu, Farao analota atayimirira mʼmbali mwa mtsinje wa Nailo,
Kum hni touh a loum hnukkhu, Faro ni mang a sak teh, thaihaw, palang rai vah a kangdue.
2 ndipo anangoona ngʼombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zooneka bwino ndi zonenepa zikutuluka mu mtsinje muja ndi kuyamba kudya msipu wa mu mawango.
A meikahawi ni teh kathâw e maitomanu hah tui thung hoi a tâco teh pho um vah apa.
3 Kenaka ngʼombe zina zazikazi zisanu ndi ziwiri zosaoneka bwino ndi zowonda zinatulukanso mu mtsinje wa Nailo ndipo zinayimirira pambali pa zina zija zimene zinali mʼmphepete mwa mtsinje uja.
Hahoi khenhaw! maitomanu sari touh, a meikahawi hoeh ni teh kamsoe e hah tui thung hoi a tâco van teh palang rai vah kangdout e maitomanu teng vah a kangdue.
4 Ndipo ngʼombe zosaoneka bwino ndi zowonda zija zinadya ngʼombe zonenepa zija. Kenaka Farao anadzidzimuka.
Maitomanunaw a meikahawihoeh ni teh kamsoe e naw ni a meikahawi ni teh kathâw e naw hah koung a ca awh. Hahoi teh Faro teh vak a kâhlaw.
5 Posakhalitsa anagonanso ndipo analota kachiwiri: Analota ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zathanzi labwino zitabala pa phata limodzi.
Hahoi bout a i teh mang bout a sak. Khenhaw! cakung buet touh dawk kahawi ni teh kalen e cavui sari touh a tâco.
6 Kenaka ngala zina zisanu ndi ziwiri zinaphuka. Izi zinali zowonda ndi zowauka ndi mphepo ya kummawa.
Hahoi khenhaw! kathoengca ni teh Kanîtholae kahlî ni remke lah a hmang e cavui sari touh bout a tâco.
7 Ngala zowonda zija zinameza ngala zathanzi ndi zonenepa zija. Farao anadzidzimuka ndipo anaona kuti anali maloto chabe.
Cavui kathoengcae sari touh ni, cavui kalen ni teh kahawi e sari touh hah koung a payawp awh. Faro vak a kâhlaw teh khenhaw! mang lah ao.
8 Mmawa, Farao anavutika mu mtima kotero anayitanitsa amatsenga ndi anzeru onse a mu Igupto. Iwo atabwera, iye anawawuza maloto ake, koma panalibe ndi mmodzi yemwe amene anatha kutanthauzira malotowo kwa Farao.
A tangtho torei, a muitha a lungpuen teh tami a patoun. Izip ram e mitpaleikathoumnaw hoi tami lungang pueng a kaw teh Faro ni a mang hah a dei pouh. Hahoi Faro hanelah ka deicai thai e buet touh boehai awm hoeh.
9 Ndipo mkulu wa operekera zakumwa anati kwa Farao, “Lero ndakumbukira kulephera kwanga.
Hatnavah misurtui kapoenaw kaukkung ni Faro koevah, sahnin ka yonnae ka kâpanue.
10 Paja nthawi ina Farao anapsera mtima antchito akefe, ndipo anatitsekera (ine ndi mkulu wa ophika buledi) mʼndende, mʼnyumba ya mkulu wa alonda.
A sannaw koevah, Faro a lungkhuek teh karingkungnaw kaukkung im vah kai hoi vaiyei kasakkungnaw kaukkung thongim ka bo roi navah,
11 Tsiku lina tonse awiri tinalota maloto, ndipo loto lililonse linali ndi tanthauzo lake.
mang reirei ka sak roi. Kaimouh roi e mang hah deingainae kâvan hoeh e doeh.
12 Tsono momwemo munali mnyamata wina Wachihebri, wantchito wa mkulu wa alonda. Ife tinamufotokozera maloto athu, ndipo anatitanthauzira malotowo. Munthu aliyense anamupatsa tanthauzo la loto lake.
Hawvah kaimouh karingkung e san Hebru tami buet touh ao teh mang hah ka dei pouh roi. Ahni ni mang heh a deicai teh ka mang roi e patetlah a deicai van.
13 Ndipo zinthu zinachitikadi monga mmene anatitanthauzira. Ine anandibwezera pa ntchito yanga ndipo winayo anapachikidwa.”
A deicai e patetlah mang teh reirei a tâco van. Kai teh thaw bout tawk sak lah ka o teh, ahni teh kai thi sak e lah ao telah ati.
14 Choncho Farao anamuyitanitsa Yosefe, ndipo mofulumira anabwera naye kuchokera mʼdzenje muja. Ndipo atameta, ndi kusintha zovala, anapita kwa Farao.
Hat toteh, Faro ni Joseph hah tang a kaw sak. Ka rang poung lah thongim thung a thung patuen dawk e a rasa awh teh, a pâkhamuen a ngaw hnukkhu a khohna a kâthung teh Faro koe a kâen.
15 Farao anati kwa Yosefe, “Ndinalota maloto ndipo palibe amene watha kunditanthauzira. Tsono ndawuzidwa kuti iwe ukamva loto umadziwanso kulimasulira.”
Faro ni Joseph koe mang ka sak teh ka deicaikung apihai awm hoeh. Hatei nang ni mang heh na thaipanuek teh, na deicai thai telah ayânaw ni dei e hah ka thai telah ati.
16 Yosefe anamuyankha Farao kuti, “Sindingathe koma Mulungu apereka yankho limene Farao akufuna.”
Joseph ni Faro koe hot teh kai koe awm hoeh. Cathut ni Faro koe roumnae lahoi a deicai han doeh telah ati.
17 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, “Ndinalota nditayimirira mʼmphepete mwa mtsinje wa Nailo,
Faro ni Joseph koe ka mang lavah khenhaw! palang rai ka kangdue.
18 ndipo ngʼombe zisanu ndi ziwiri zonenepa ndi zooneka bwino zinatuluka mu mtsinje muja ndi kumadya msipu wa mu mawango.
Hahoi khenhaw! maitomanu a meikahawi ni teh kathâw e sari touh tuithung hoi a tâco teh pho um vah a pâ.
19 Kenaka, ngʼombe zina zisanu ndi ziwiri zinatuluka. Izi zinali zosaoneka bwino ndiponso zowonda ndipo sindinaonepo ngʼombe zosaoneka bwino chonchi mʼdziko lonse la Igupto.
Hahoi alouke maitomanu a meikamathout niteh, ka kamsoe e hot patet e meimathout teh Izip ram pueng dawk patenghai ka hmu boihoeh e hah a tâco.
20 Ngʼombe zosaoneka bwino ndi zowonda zija zinadya zisanu ndi ziwiri zonenepa zimene zinatuluka poyamba zija.
Hahoi a mei kathout ni teh ka kamsoe e maitomanunaw ni kathâw e maitomanunaw hah koung a ca awh.
21 Koma ngakhale ngʼombezi zinadya zinazo, palibe amene akanatha kuzindikira kuti zinatero popeza zinali zosaonekabe bwino monga poyamba. Ndipo ndinadzidzimuka.
Koung a ca awh hnukkhu patenghai yah apinihai a ca awh tie panuek kalawn hoeh. A ca awh hoehnahlan e patetlah a mei a mathoe awh mingming, hahoi vak ka kâhlaw.
22 “Nditagonanso kachiwiri, ndinalota ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zathanzi ndi zonenepa zitabala pa phata limodzi.
Hahoi ka mang lavah khenhaw! Cakung buet touh dawkvah, cavui kahawipoung e sari touh a tâco.
23 Kenaka panaphukanso ngala zina zisanu ndi ziwiri zofota, zowonda ndi zowauka ndi mphepo ya kummawa.
Hahoi khenhaw! cavui sari touh kamyai ni teh kathoengcae, Kanîtholae kahlî ni remke lah a hmang e a tâco e hah bout ka hmu.
24 Ngala zowondazo zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zabwino zija. Ndinawawuza amatsenga koma palibe ndi mmodzi yemwe anatha kundimasulira.”
Cavui kathoutnaw ni cavui kahawinaw sari touh hah koung a ca awh. Hote mang hah mitpaleikathoumnaw ka dei pouh ei, apinihai deicai thai awh hoeh, telah a dei.
25 Ndipo Yosefe anati kwa Farao, “Maloto awiriwa ndi ofanana ndipo ali ndi tanthauzo limodzi. Mulungu waululira Farao chimene atachite.
Joseph ni Faro koe Faro nange mang heh buet touh doeh. Cathut ni a sak hane hah Faro koe na panue sak e doeh.
26 Ngʼombe zisanu ndi ziwiri zabwinozo ndi zaka zisanu ndi ziwiri. Ndipo ngala zisanu ndi ziwiri zabwinozo ndi zaka zisanu ndi ziwiri. Kutanthauza kwa maloto nʼkumodzi.
Meikahawi e maitomanu sari touh teh kum sari touh doeh. Kahawi e cavui sari touh hai kum sari touh doeh. Mang teh buet touh doeh.
27 Ngʼombe zisanu ndi ziwiri zowonda ndi zosaoneka bwino zimene zinatuluka pambuyozo ndiponso ngala zisanu ndi ziwiri zachabechabe, zowauka ndi mphepo ya kummawa zija ndi zaka zisanu ndi ziwiri za njala.
Hahoi a hnukkhu vah ka tâcawt e a mei kathout ni teh ka kamsoe e maitomanu sari touh hai kum sari touh doeh. Cavui sari touh Kanîtholae kahlî ni remke lah a hmang e hai kum sari touh doeh.
28 “Tsono ndi monga ndafotokozeramu kuti Mulungu wakuwuziranitu zimene adzachite.
Hetheh, Faro koe ka dei e Cathut ni a sak hane Faro a panue sak e doeh.
29 Zaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zochuluka zikubwera mu dziko lonse la Igupto,
Izip ram vah khobunae kum sari touh ao han.
30 koma zidzatsatana ndi zaka zina zisanu ndi ziwiri za njala. Chakudya chochuluka cha mu Igupto chija chidzayiwalika ndipo njalayo idzawononga dziko.
Hatei, hat hnukkhu takangnae kum sari touh bout ao han. Hottelah takang ni ram teh voutthoup lah ao sak han dawkvah, khobunae kum pueng hah Izip ram teh pahnim e lah ao han.
31 Zakudya zochuluka za mʼdzikomo zija sizidzakumbukirikanso chifukwa njala imene iti idzabwereyo idzakhala yoopsa.
Rek ka tho e takang teh puenghoi a pataw han dawkvah, khobunae kum hah pahnim lah ao han.
32 Popeza kuti malotowa aperekedwa kwa inu Mfumu kawiri, ndiye kuti Mulungu watsimikiza kuti adzachitadi zimenezi posachedwapa.
Hahoi mang vai hni totouh Faro a mangsaknae teh hete hno kecu dawk doeh. Sak hane teh Cathut ni a caksak teh Cathut roeroe ni karanglah a pha sak han.
33 “Tsopano Farao apezeretu munthu wozindikira ndi wanzeru ndipo amuyike kukhala woyangʼanira dziko lonse la Igupto.
Hatdawkvah, Faro ni tami buet touh a lungkaang e hoi kho ka pouk thai e tawng nateh Izip ram vah kahrawikung lah awm sak naseh.
34 Asankhenso akuluakulu a mʼdziko lino. Iwowa azitenga ndi kuyika padera limodzi la magawo asanu aliwonse a zokolola za mʼdziko muno mu zaka zonse zisanu ndi ziwiri za chakudya chochuluka.
Faro ni hotheh sak naseh, ram thung vah Izip ram cakang hah pung panga pung touh pâtung naseh.
35 Iwo asonkhanitse zakudya zonse za mʼzaka zabwino zikubwerazi. Pansi pa ulamuliro wa Farao, akuluakuluwo asonkhanitse ndi kusunga bwino tirigu mʼmizinda yonse.
Ahnimouh ni khobu kum cakang pung hah pâkhueng vaiteh Faro kâtawnnae rahim vah o hanelah kho tangkuem hmalah ca hane pâtung naseh, khenyawn awh naseh.
36 Chakudya chimenechi chisungidwe kuti chidzagwiritsidwe ntchito mʼzaka zisanu ndi ziwiri za njala imene ikubwerayo mu Igupto, kuti anthu a mʼdzikoli asadzafe ndi njalayo.”
Hottelah takang kecu dawk ram a rawk hoeh nahanlah, takangnae kum kum sari touh Izip ram ka phat hane dawkvah, kâhruetcuet lah ao han, telah ati.
37 Farao ndi nduna zake anagwirizana nawo malangizo a Yosefe.
Hottelah pouknae a poe e hah, Faro hoi a sannaw pueng ni ahawi rip ati awh.
38 Choncho Farao anafunsa nduna zake nati, “Kodi tingathe kumupeza munthu wina ngati uyu, amene ali ndi mzimu wa Mulungu?”
Hottelah Faro ni a sannaw koe het patet e Cathut Muitha onae tami heh hmu thai awh han na ou telah ati.
39 Farao anati kwa Yosefe, “Pakuti Mulungu wakudziwitsa iwe zonsezi, palibe wina wodziwa zinthu ndi wanzeru ngati iwe.
Faro ni Joseph koe Cathut ni hote hnonaw pueng hah na panue sak dawkvah, nang patetlae tami lungkaang hoi hno kaawm hane oang ka panuek e awm hoeh.
40 Iwe ukhala nduna yayikulu mu dziko langa ndipo anthu onse adzamvera zimene walamula. Ine ndekha ndiye amene ndidzakuposa mphamvu chifukwa ndimakhala pa mpando waufumu.”
Nang teh kaie imthung karingkung lah na o han, ka taminaw pueng hah nange kâ lahoi ao awh han, bawitungkhung dueng hah nang hlak kai bet ka lenhnawn han telah ati.
41 Choncho Farao anati kwa Yosefe, “Ine ndikukuyika iwe kukhala nduna yoyangʼanira dziko lonse la Igupto.”
Faro ni Joseph koe khenhaw! Izip ram pueng dawk kahrawikung lah na ta toe telah ati.
42 Ndipo Farao anavula mphete ku chala chake nayiveka ku chala cha Yosefe. Anamuvekanso mkanjo wonyezimira ndi nkufu wagolide mʼkhosi mwake.
Faro ni kutnoutthutnae kuthrawt hah a rading teh, Joseph kut dawk a buet pouh, hni loukloukkaang e hoi sak e hah a kâkhu sak teh a lahuen dawk sui dingyin hah a awi sak.
43 Anamukweza Yosefe pa galeta ngati wachiwiri pa ulamuliro. Ndipo anthu anafuwula pamaso pake nati, “Mʼgwadireni!” Motero anakhala nduna yayikulu ya dziko lonse la Igupto.
A tawn e leng kahni touh dawk a kâcui sak teh, a hmalah tabut awh, telah a hram awh. Hottelah Izip ram thung kahrawikung lah a coung sak.
44 Kenaka Farao anati kwa Yosefe, “Ine ndine Farao; tsono iwe ukapanda kulamula, palibe amene akhoza kuchita chilichonse ngakhale kuyenda kumene mʼdziko lonse la Igupto.”
Faro ni Joseph koevah, kai teh Faro doeh, nange kâpoe laipalah Izip ram thung pueng a kut hai thoseh, a khok hai thoseh, dâw thai mahoeh telah ati.
45 Farao anamupatsa Yosefe dzina lakuti Zafenati-Panea ndipo anamupatsanso Asenati mwana wa mkazi wa Potifara, wansembe wa Oni, kuti akhale mkazi wake. Choncho Yosefe anayendera dziko lonse la Igupto.
Faro ni Joseph hah Zaphnath-Paaneah telah min a poe. On kho e vaihma Potiphar canu Asenath hah a yu lah a paluen pouh awh. Hahoi Joseph teh Izip ram kaukkung lah ahni koehoi a cei.
46 Yosefe anali ndi zaka 30 pamene amayamba ntchito kwa Farao, mfumu ya ku Igupto. Ndipo Yosefe anachoka pa maso pa Farao nayendera dziko lonse la Igupto.
Joseph teh Izip siangpahrang Faro hmalah a kangdue navah, kum 30 touh doeh Joseph teh Faro koehoi a tâco teh Izip ram pueng dawk a cei.
47 Mʼzaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zambiri zija, anthu mʼdzikomo anakolola zochuluka.
Khobu kum kum sari touh thung talai ni puenghoi a pawhik a tâco sak.
48 Yosefe anasonkhanitsa zakudya zonse zokololedwa mʼzaka zisanu ndi ziwiri zija ndipo anazisunga mʼmizinda. Mu mzinda uliwonse anayikamo chakudya chimene chinalimidwa mʼminda yozungulira komweko.
Izip ram e khobu kum kum sari touh thung e cakang pueng hah a pâkhueng teh kho tangkuem tengpam e cakang hah a hmouk sak.
49 Yosefe anasunga tirigu wochuluka kwambiri ngati mchenga wa ku nyanja. Kunali tirigu wochuluka kwambiri motero kuti analeka nʼkulembera komwe.
Joseph ni cakang hah talî teng e sadi patetlah kapappoung lah a pâtung, touk patenghai touk ngai hoeh toe, bangkongtetpawiteh, touklek hoeh toe.
50 Zisanafike zaka zanjala, Yosefe anabereka ana aamuna awiri mwa Asenati mwana wa mkazi wa Potifara, wansembe wa Oni.
Hahoi takang a tho hoehnahlan vah Joseph ni capa kahni toun a tawn. Hotnaw teh On kho vaihma Potiphar canu Asenath ni a khe pouh e naw doeh.
51 Yosefe anamutcha mwana wake woyamba, Manase popeza anati, “Mulungu wandiyiwalitsa zovuta zanga zija ndiponso banja la abambo anga.”
Joseph ni a camin hah Manasseh telah a phung. Bangkongtetpawiteh, Cathut ni ka tawntamnae hoi apa imthung pueng na pahnim sak telah ati.
52 Mwana wachiwiri wa mwamuna anamutcha Efereimu popeza anati, “Mulungu wandipatsa ana mʼdziko la masautso anga.”
Hahoi a capa apâhni e min teh Ephraim telah a phung. Bangkongtetpawiteh, Cathut ni kaie runae ram dawk ca catounnaw na tawn sak telah ati.
53 Zaka zisanu ndi ziwiri za zokolola zochuluka zija zinatha,
Hottelah Izip ram ka phat e khobu kum teh a loum.
54 ndipo zaka zisanu ndi ziwiri za njala zija zinayamba monga ananenera Yosefe. Njalayi inafika ku mayiko ena onse koma ku dziko lonse la Igupto kunali chakudya.
Hahoi takang kum kum sari touh Joseph ni a dei tangcoung patetlah a kamtawng teh ram pueng dawk a pha. Hatei, Izip ram pueng dawk rawca ao.
55 Pamene njala ija inakwanira dziko lonse la Igupto anthu analilira Farao kuti awapatse chakudya. Koma Farao anawawuza kuti, “Pitani kwa Yosefe ndipo mukachite zimene akakuwuzeni.”
Hottelah Izip ram pueng teh takang ni koung a pha toteh, Faro koe rawca hei hoi a hram awh. Faro ni Izipnaw pueng koe Joseph koe cet awh nateh, a dei e pueng sak awh telah atipouh.
56 Pamene njala inafalikira dziko lonse, Yosefe anatsekula nkhokwe za zakudya namagulitsa tirigu kwa anthu a ku Igupto aja, pakuti njala inafika poyipa kwambiri mu Igupto monse.
Hahoi takang teh talai van pueng a pha teh, Joseph ni cakang pâtungnae tâsong pueng hah a paawng teh Izipnaw koevah a yo pouh. Izip ram vah takang teh puenghoi a pataw.
57 Anthu ankabwera ku Igupto kuchokera ku mayiko ena onse kudzagula tirigu kwa Yosefe, chifukwa njala inafika poyipa kwambiri pa dziko lonse lapansi.
Talai van pueng dawk takang teh a pataw poung dawkvah, kho tangkuem e tami pueng teh cakang ran hanelah Izip ram e Joseph koe a cei awh.

< Genesis 41 >