< Genesis 40 >
1 Patapita nthawi, woperekera zakumwa ndi wopanga buledi a ku nyumba kwa mfumu ya ku Igupto analakwira mbuye wawoyo.
Bir süre sonra Mısır Kralı'nın sakisiyle fırıncısı efendilerini gücendirdiler.
2 Farao anapsa mtima ndi akuluakulu awiriwa,
Firavun bu iki görevlisine, baş sakiyle fırıncıbaşına öfkelendi.
3 ndipo anakawatsekera mʼndende, nakawayika mʼmanja mwa mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa mfumu kuja, mʼndende momwe Yosefe ankasungidwamo.
Onları muhafız birliği komutanının evinde, Yusuf'un tutsak olduğu zindanda göz altına aldı.
4 Mkulu wa alonda aja anawapereka mʼmanja mwa Yosefe, ndipo iye anawasamalira. Iwo anakhala mʼndendemo kwa kanthawi.
Muhafız birliği komutanı Yusuf'u onların hizmetine atadı. Bir süre zindanda kaldılar.
5 Usiku wina, aliyense wa anthu awiriwa, wopereka zakumwa pamodzi ndi wopanga buledi wa ku nyumba ya mfumu ya ku Igupto aja, amene ankasungidwa mʼndende, analota maloto. Malotowo anali ndi tanthauzo lake.
Firavunun sakisiyle fırıncısı tutsak oldukları zindanda aynı gece birer düş gördüler. Düşleri farklı anlamlar taşıyordu.
6 Mmawa wake, Yosefe atabwera, anaona kuti nkhope zawo zinali zakugwa.
Sabah Yusuf yanlarına gittiğinde, onları tedirgin gördü.
7 Choncho anafunsa akuluakulu a kwa Farao amene anali naye mʼndende muja kuti, “Bwanji nkhope zanu zili zachisoni lero?”
Efendisinin evinde, kendisiyle birlikte zindanda kalan firavunun görevlilerine, “Niçin suratınız asık bugün?” diye sordu.
8 Iwo anayankha, “Tonse awiri talota maloto, koma palibe wotitanthauzira malotowo.” Pamenepo Yosefe anawawuza kuti, “Ndi Mulungu yekha amene amapereka matanthauzo a maloto. Uzeni ine maloto anu.”
“Düş gördük ama yorumlayacak kimse yok” dediler. Yusuf, “Yorum Tanrı'ya özgü değil mi?” dedi, “Lütfen düşünüzü bana anlatın.”
9 Choncho mkulu wa operekera zakumwa uja anamuwuza Yosefe maloto ake. Anati, “Mʼmaloto anga ndinaona mtengo wa mpesa,
Baş saki düşünü Yusuf'a anlattı: “Düşümde önümde bir asma gördüm.
10 unali ndi nthambi zitatu. Mpesawo utangophukira, unachita maluwa ndipo maphava ake anabereka mphesa zakupsa.
Üç çubuğu vardı. Tomurcuklar açar açmaz çiçeklendi, salkım salkım üzüm verdi.
11 Chikho cha Farao chinali mʼmanja mwanga, ndipo ndinatenga mphesa, kupsinyira mu chikho cha Farao ndi kuchipereka mʼmanja mwake.”
Firavunun kâsesi elimdeydi. Üzümleri alıp firavunun kâsesine sıktım. Sonra kâseyi ona verdim.”
12 Yosefe anati kwa iye, “Tanthauzo lake ndi ili: Nthambi zitatuzo ndi masiku atatu.
Yusuf, “Bu şu anlama gelir” dedi, “Üç çubuk üç gün demektir.
13 Pakangopita masiku atatu, Farao adzakutulutsa muno. Udzaperekera zakumwa kwa Farao monga momwe umachitira poyamba.
Üç gün içinde firavun seni zindandan çıkaracak, yine eski görevine döneceksin. Geçmişte olduğu gibi yine ona sakilik yapacaksın.
14 Koma zako zikakuyendera bwino, udzandikumbukire ndi kundikomera mtima. Chonde ukandipepesere kwa Farao kuti anditulutse muno.
Ama her şey yolunda giderse, lütfen beni anımsa. Bir iyilik yap, firavuna benden söz et. Çıkar beni bu zindandan.
15 Popezatu ine anangochita mondiba kubwera nane kuno kuchokera ku dziko la Ahebri, ndipo ngakhale kunoko, ine sindinalakwe kali konse kuti ndizipezeka mʼdzenje muno.”
Çünkü ben İbrani ülkesinden zorla kaçırıldım. Burada da zindana atılacak bir şey yapmadım.”
16 Mkulu wa opanga buledi ataona kuti Yosefe wapereka tanthauzo labwino, anati kwa Yosefe, “Inenso ndinalota nditasenza nsengwa zitatu za buledi.
Fırıncıbaşı bu iyi yorumu duyunca, Yusuf'a, “Ben de bir düş gördüm” dedi, “Başımın üstünde üç sepet beyaz ekmek vardı.
17 Mu nsengwa yapamwamba munali zakudya zamitundumitundu za Farao, koma mbalame zimadya zakudyazo.”
En üstteki sepette firavun için pişirilmiş çeşitli pastalar vardı. Kuşlar başımın üstündeki sepetten pastaları yiyorlardı.”
18 Yosefe anati, “Tanthauzo lake ndi ili: nsengwa zitatuzo ndi masiku atatu.
Yusuf, “Bu şu anlama gelir” dedi, “Üç sepet üç gün demektir.
19 Pakangotha masiku atatu Farao adzakutulutsa muno koma adzakupachika. Ndipo mbalame zidzadya mnofu wako.”
Üç gün içinde firavun seni zindandan çıkarıp ağaca asacak. Kuşlar etini yiyecekler.”
20 Tsono tsiku lachitatulo linali lokumbukira kubadwa kwa Farao, ndipo anawakonzera phwando akuluakulu ake onse. Anatulutsa mʼndende mkulu wa operekera zakumwa ndi mkulu wa ophika buledi, ndipo anawayimiritsa pamaso pa nduna zake.
Üç gün sonra, firavun doğum gününde bütün görevlilerine bir şölen verdi. Görevlilerinin önünde baş sakisiyle fırıncıbaşını zindandan çıkardı.
21 Tsono Farao anamubwezera mkulu wa operekera zakumwa uja pa udindo wake, kotero kuti anayamba kuperekeranso zakumwa kwa Farao,
Yusuf'un yaptığı yoruma uygun olarak baş sakisini eski görevine atadı. Baş saki firavuna şarap sunmaya başladı. Ama firavun fırıncıbaşını astırdı.
22 koma mkulu wa ophika buledi anamupachika, mofanana ndi mmene Yosefe anatanthauzira maloto.
23 Koma mkulu wa operekera zakumwa uja sanamukumbukire Yosefe ndipo anamuyiwaliratu.
Gelgelelim, baş saki Yusuf'u anımsamadı, unuttu gitti.