< Genesis 40 >

1 Patapita nthawi, woperekera zakumwa ndi wopanga buledi a ku nyumba kwa mfumu ya ku Igupto analakwira mbuye wawoyo.
Och det begaf sig derefter, att Konungens i Egypten höfvitsman öfver skänkerna, och höfvitsmannen öfver bakarena, bröto deras herra Konungenom i Egypten emot.
2 Farao anapsa mtima ndi akuluakulu awiriwa,
Och Pharao vardt vred uppå dem,
3 ndipo anakawatsekera mʼndende, nakawayika mʼmanja mwa mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa mfumu kuja, mʼndende momwe Yosefe ankasungidwamo.
Och lät sätta dem i hofmästarens hus i fängelse, der Joseph låg fången.
4 Mkulu wa alonda aja anawapereka mʼmanja mwa Yosefe, ndipo iye anawasamalira. Iwo anakhala mʼndendemo kwa kanthawi.
Och hofmästaren satte Joseph öfver dem, att han skulle tjena dem; och de såto några dagar.
5 Usiku wina, aliyense wa anthu awiriwa, wopereka zakumwa pamodzi ndi wopanga buledi wa ku nyumba ya mfumu ya ku Igupto aja, amene ankasungidwa mʼndende, analota maloto. Malotowo anali ndi tanthauzo lake.
Och både skänken och bakaren drömde om ena natt hvar sin dröm, och hvars deras dröm hade sin uttydelse.
6 Mmawa wake, Yosefe atabwera, anaona kuti nkhope zawo zinali zakugwa.
Då nu Joseph kom om morgonen in till dem, och såg dem ångse,
7 Choncho anafunsa akuluakulu a kwa Farao amene anali naye mʼndende muja kuti, “Bwanji nkhope zanu zili zachisoni lero?”
Frågade han dem, och sade: Hvi ären I så ångse i dag?
8 Iwo anayankha, “Tonse awiri talota maloto, koma palibe wotitanthauzira malotowo.” Pamenepo Yosefe anawawuza kuti, “Ndi Mulungu yekha amene amapereka matanthauzo a maloto. Uzeni ine maloto anu.”
De svarade: Oss hafver drömt, och vi hafvom ingen, som oss det utlägger. Joseph sade: Utläggningen hörer Gudi till; dock förtäljer mig det.
9 Choncho mkulu wa operekera zakumwa uja anamuwuza Yosefe maloto ake. Anati, “Mʼmaloto anga ndinaona mtengo wa mpesa,
Då förtäljde skänken sin dröm för Joseph, och sade till honom: Mig drömde, att ett vinträ var för mig:
10 unali ndi nthambi zitatu. Mpesawo utangophukira, unachita maluwa ndipo maphava ake anabereka mphesa zakupsa.
Det hade tre grenar; det grönskades, växte och blomstrades, och dess drufvor vordo mogna:
11 Chikho cha Farao chinali mʼmanja mwanga, ndipo ndinatenga mphesa, kupsinyira mu chikho cha Farao ndi kuchipereka mʼmanja mwake.”
Och jag hade Pharaos skänkekar i mine hand, och tog och kryste dem i skänkekaret, och fick Pharao skänkekaret i handena.
12 Yosefe anati kwa iye, “Tanthauzo lake ndi ili: Nthambi zitatuzo ndi masiku atatu.
Joseph sade: Detta är uttydningen: Tre grenar äro tre dagar.
13 Pakangopita masiku atatu, Farao adzakutulutsa muno. Udzaperekera zakumwa kwa Farao monga momwe umachitira poyamba.
Efter tre dagar skall Pharao upphäfva ditt hufvud, och sätta dig åter till dit ämbete, att du får honom skänkekaret i hans hand, såsom tillförene, då du var hans skänk.
14 Koma zako zikakuyendera bwino, udzandikumbukire ndi kundikomera mtima. Chonde ukandipepesere kwa Farao kuti anditulutse muno.
Men tänk uppå mig, då dig går väl, och gör barmhertighet med mig, att du Pharao ingifver, att han tager mig utaf detta huset;
15 Popezatu ine anangochita mondiba kubwera nane kuno kuchokera ku dziko la Ahebri, ndipo ngakhale kunoko, ine sindinalakwe kali konse kuti ndizipezeka mʼdzenje muno.”
Ty jag är hemliga bortstulen utaf de Ebreers lande: Så hafver jag ock här intet gjort, att de mig insatt hafva.
16 Mkulu wa opanga buledi ataona kuti Yosefe wapereka tanthauzo labwino, anati kwa Yosefe, “Inenso ndinalota nditasenza nsengwa zitatu za buledi.
Då bakaren såg, att uttydningen var god, sade han till Joseph: Mig hafver ock drömt, att jag bar tre flätade korgar på mitt hufvud;
17 Mu nsengwa yapamwamba munali zakudya zamitundumitundu za Farao, koma mbalame zimadya zakudyazo.”
Och i öfversta korgenom allahanda bakad mat till Pharaos behof; och foglarne åto af korgenom på mitt hufvud.
18 Yosefe anati, “Tanthauzo lake ndi ili: nsengwa zitatuzo ndi masiku atatu.
Joseph svarade, och sade: Detta är uttydningen: Tre korgar äro tre dagar.
19 Pakangotha masiku atatu Farao adzakutulutsa muno koma adzakupachika. Ndipo mbalame zidzadya mnofu wako.”
Och efter tre dagar skall Pharao upphäfva ditt hufvud, och hänga dig i en galga; och foglarne skola äta ditt kött på dig.
20 Tsono tsiku lachitatulo linali lokumbukira kubadwa kwa Farao, ndipo anawakonzera phwando akuluakulu ake onse. Anatulutsa mʼndende mkulu wa operekera zakumwa ndi mkulu wa ophika buledi, ndipo anawayimiritsa pamaso pa nduna zake.
Och det hände tredje dagen, då begick Pharao sin årsdag, och han gjorde alla sina tjenare ena måltid: Och upphof den öfversta skänkens hufvud, och den öfversta bakarens, ibland sina tjenare;
21 Tsono Farao anamubwezera mkulu wa operekera zakumwa uja pa udindo wake, kotero kuti anayamba kuperekeranso zakumwa kwa Farao,
Och satte den öfversta skänken åter till sitt skänkeämbete, att han skulle få Pharao skänkekaret i handena;
22 koma mkulu wa ophika buledi anamupachika, mofanana ndi mmene Yosefe anatanthauzira maloto.
Men den öfversta bakaren lät han hänga; som Joseph hade uttydt honom.
23 Koma mkulu wa operekera zakumwa uja sanamukumbukire Yosefe ndipo anamuyiwaliratu.
Men den öfverste skänken tänkte intet på Joseph, utan förgat honom.

< Genesis 40 >