< Genesis 4 >

1 Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
L'homme connut Eve, sa femme. Elle conçut et donna naissance à Caïn, et dit: « J'ai obtenu un homme avec l'aide de Yahvé. »
2 Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
Elle donna de nouveau naissance à Abel, frère de Caïn. Abel était gardien de moutons, mais Caïn était cultivateur de la terre.
3 Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
Au fil du temps, Caïn apporta une offrande à Yahvé avec les fruits du sol.
4 Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
Abel apporta aussi une partie des premiers-nés de son troupeau et de sa graisse. Yahvé respecta Abel et son offrande,
5 Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
mais il ne respecta pas Caïn et son offrande. Caïn fut très irrité, et l'expression de son visage tomba.
6 Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
Yahvé dit à Caïn: « Pourquoi es-tu en colère? Pourquoi l'expression de ton visage est-elle tombée?
7 Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
Si tu fais bien, ne sera-t-elle pas élevée? Si tu ne fais pas le bien, le péché est accroupi à la porte. C'est toi qu'il désire, mais c'est toi qui dois le dominer. »
8 Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
Caïn dit à Abel, son frère: « Allons dans le champ. » Pendant qu'ils étaient dans le champ, Caïn se souleva contre Abel, son frère, et le tua.
9 Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
Yahvé dit à Caïn: « Où est Abel, ton frère? » Il a dit: « Je ne sais pas. Suis-je le gardien de mon frère? »
10 Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
Yahvé dit: « Qu'as-tu fait? La voix du sang de ton frère crie vers moi depuis la terre.
11 Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
Maintenant, tu es maudit à cause de la terre, qui a ouvert sa bouche pour recevoir de ta main le sang de ton frère.
12 Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
Désormais, quand tu laboureras la terre, elle ne te cédera plus sa force. Tu seras un fugitif et un vagabond sur la terre. »
13 Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
Caïn dit à Yahvé: « Mon châtiment est plus grand que ce que je peux supporter.
14 Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
Voici, tu m'as chassé aujourd'hui de la surface de la terre. Je serai caché de ta face, et je serai un fugitif et un vagabond sur la terre. Celui qui me trouvera me tuera. »
15 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
Yahvé lui dit: « C'est pourquoi, si quelqu'un tue Caïn, il se vengera sept fois plus. » Yahvé avait prévu un signe pour Caïn, afin que celui qui le trouverait ne le frappe pas.
16 Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
Caïn quitta la présence de Yahvé et habita dans le pays de Nod, à l'est d'Eden.
17 Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
Caïn connut sa femme. Elle devint enceinte et donna naissance à Hénoc. Il bâtit une ville, et donna à la ville le nom de son fils, Hénoc.
18 Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
Irad naquit d'Hénoc. Irad devint le père de Mehujael. Mehujael devint le père de Methushael. Methushael engendra Lamek.
19 Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
Lamek prit deux femmes: le nom de la première était Ada, et le nom de la seconde était Zilla.
20 Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
Ada donna naissance à Jabal, qui fut le père de ceux qui habitent dans des tentes et qui ont du bétail.
21 Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
Le nom de son frère était Jubal, qui était le père de tous ceux qui manient la harpe et le chalumeau.
22 Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
Zilla donna aussi naissance à Tubal Caïn, le forgeur de tous les instruments tranchants en bronze et en fer. La sœur de Tubal Caïn était Naama.
23 Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
Lamek dit à ses femmes, « Adah et Zillah, entendez ma voix. Femmes de Lamech, écoutez mon discours, car j'ai tué un homme pour m'avoir blessé, un jeune homme pour m'avoir meurtri.
24 Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
Si Caïn sera vengé sept fois, vraiment Lamech soixante-dix-sept fois. »
25 Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
Adam connut de nouveau sa femme. Elle donna naissance à un fils, qu'elle appela Seth, en disant: « Dieu m'a donné un autre enfant à la place d'Abel, car Caïn l'a tué. »
26 Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.
Un fils naquit aussi à Seth, et il le nomma Enosh. En ce temps-là, les hommes commencèrent à invoquer le nom de Yahvé.

< Genesis 4 >