< Genesis 4 >

1 Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
Adam kendte sin Hustru Eva, og hun blev frugtsommelig og fødte Kain; og hun sagde: "Jeg har fået en Søn med HERRENS Hjælp!"
2 Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
Fremdeles fødte hun hans Broder Abel. Abel blev Fårehyrde, Kain Agerdyrker.
3 Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
Nogen Tid efter bragte Kain HERREN en Offergave af Jordens Frugt,
4 Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
medens Abel bragte en Gave af sin Hjords førstefødte og deres Fedme. Og HERREN så til Abel og hans Offergave,
5 Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
men til Kain og hans Offergave så han ikke. Kain blev da såre vred og gik med sænket Hoved.
6 Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
Da sagde HERREN til Kain: "Hvorfor er du vred, og hvorfor går du med sænket Hoved?
7 Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
Du ved, at når du handler vel, kan du løfte Hovedet frit; men handler du ikke vel, så lurer Synden ved Døren; dens Attrå står til dig, men du skal herske over den!"
8 Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
Men Kain yppede Kiv med sin Broder Abel; og engang de var ude på Marken, sprang Kain ind på ham og slog ham ihjel.
9 Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
Da sagde HERREN til Kain: "Hvor er din Broder Abel?" Han svarede: "Det ved jeg ikke; skal jeg vogte min Broder?"
10 Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
Men han sagde: "Hvad har du gjort! Din Broders Blod råber til mig fra Jorden!
11 Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
Derfor skal du nu være bandlyst fra Agerjorden, som åbnede sig og tog din Broders Blod af din Hånd!
12 Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
Når du dyrker Agerjorden, skal den ikke mere skænke dig sin Kraft du skal flakke hjemløs om på Jorden!"
13 Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
Men Kain sagde til HERREN: "Min Straf er ikke til at bære;
14 Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
når du nu jager mig bort fra Agerjorden, og jeg må skjule mig for dit Åsyn og flakke hjemløs om på Jorden, så kan jo enhver, der møder mig, slå mig ihjel!"
15 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
Da svarede HERREN: "Hvis Kain bliver slået ihjel, skal han hævnes; syvfold!" Og HERREN satte et Tegn på Kain, for at ingen, der mødte ham, skulde slå ham ihjel.
16 Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
Så drog Kain bort fra HERRENs Åsyn og slog sig ned i Landet Nod østen for Eden.
17 Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
Kain kendte sin Hustru, og hun blev frugtsommelig og fødte Hanok. Han grundede en By og gav den sin; Søn Hanoks Navn.
18 Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
Hanok fik en Søn Irad; Irad avlede Mehujael; Mehujael avlede Mehujael; og Metusjael avlede Lemek
19 Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
Lemek tog sig to Hustruer; den ene hed Ada, den anden Zilla.
20 Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
Ada fødte Jabal; han blev Stamfader til dem, der bor i Telte og holder Kvæg;
21 Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
hans Broder hed Jubal; han blev Stamfader til alle dem, der spiller på Harpe og Fløjte.
22 Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
Også Zilla fik en Søn, Tubal-Kajin; han blev Stamfader til alle dem, der smeder Kobber og Jern. Tubal-Kajins Søster var Na'ama.
23 Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
Og Lemelk sagde til sine Hustruer: "Ada og Zilla, hør min Røst, Lemeks Hustruer, lyt til mit Ord: En Mand har jeg dræbt for et Sår, en Dreng for en Skramme!
24 Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
Blev Kain hævnet syvfold, så hævnes Lemek syv og halvfjerdsindstyve Gange!"
25 Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
Adam kendte på ny sin Hustru, og hun fødte en Søn, som hun gav Navnet Set; "thi," sagde hun, "Gud har sat mig andet Afkom i Abels Sted, fordi Kain slog ham ihjel!"
26 Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.
Set fik også en Søn, som han kaldte Enosj; på den Tid begyndte man at påkalde HERRENs Navn.

< Genesis 4 >