< Genesis 4 >

1 Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
Og Adam kendte sin Hustru Eva; og hun undfik og fødte Kain og sagde: Jeg har faaet en Mand, som er Herren.
2 Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
Og hun blev ved at føde, nemlig hans Broder Abel; og Abel blev en Faarehyrde, og Kain dyrkede Jorden.
3 Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
Og det hændte sig, der en Tid var forløben, og Kain frembar et Offer til Herren af Jordens Frugt.
4 Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
Og Abel, ogsaa han bar frem af sin Hjords første Affødning og af deres Fedme; og Herren saa til Abel og til hans Offer.
5 Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
Men til Kain og til hans Offer saa han ikke; da blev Kain meget vred, og hans Ansigt falmede.
6 Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
Og Herren sagde til Kain: Hvi er du vred, og hvi er dit Ansigt falmet?
7 Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
Er det ikke saa, at dersom du gør godt, da er du behagelig, og dersom du ikke gør godt, da ligger Synden for Døren, og til dig er dens Attraa? men du skal herske over den.
8 Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
Og Kain talede med Abel sin Broder; og det hændte sig, der de vare paa Marken, da stod Kain op imod Abel sin Broder og ihjelslog ham.
9 Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
Og Herren sagde til Kain: Hvor er Abel, din Broder? Og han sagde: Jeg ved ikke, mon jeg være min Broders Vogter?
10 Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
Og han sagde: Hvad har du gjort? din Broders Blods Røst raaber til mig af Jorden.
11 Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
Og nu være du forbandet fra Jorden, som oplod sin Mund til at tage din Broders Blod af din Haand.
12 Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
Naar du dyrker Jorden, skal den ikke ydermere give dig sin Kraft; ustadig og flygtig skal du være paa Jorden.
13 Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
Da sagde Kain til Herren: Min Misgerning er større, end jeg kan bære.
14 Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
Se, du har i Dag drevet mig fra Jordens Kreds, og jeg maa skjule mig for dit Ansigt; og jeg bliver ustadig og flygtig paa Jorden, og det vil ske, hvo som finder mig, slaar mig ihjel.
15 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
Men Herren sagde til ham: Derfor, hvo som ihjelslaar Kain, paa ham skal det hævnes syvfold; saa satte Herren for Kain et Tegn, at ingen, som fandt ham, skulde slaa ham ihjel.
16 Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
Saa gik Kain ud fra Herrens Ansigt og blev i det Land Nod Østen for Eden.
17 Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
Og Kain kendte sin Hustru, og hun undfik og fødte Hanok; og han byggede en Stad og kaldte Stadens Navn efter sin Søns Navn, Hanok.
18 Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
Og for Hanok blev født Irad, og Irad avlede Mehujael, og Mehujael avlede Mathusael, og Mathusael avlede Lamek.
19 Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
Og Lamek tog sig to Hustruer, den enes Navn var Ada, og den andens Navn Zilla.
20 Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
Og Ada fødte Jabal; han var Fader til dem, som boede i Telte og vogtede Kvæg.
21 Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
Og hans Broders Navn var Jubal; han var Fader til alle dem, der legede paa Harpe og Fløjte.
22 Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
Og Zilla, ogsaa hun fødte, nemlig Thubalkain, som kunstigen gjorde alle Haande skarpt Kobber- og Jerntøj; og Thubalkains Søster var Naama.
23 Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
Og Lamek sagde til sine Hustruer: Ada og Zilla, hører min Røst, Lameks Hustruer, mærker min Tale! Om jeg har slagen en Mand ihjel, mig til et Saar, og en Dreng, mig til en Byld:
24 Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
da skal Kain hævnes syvfold, og Lamek halvfjerdsindstyve Gange og syv Gange.
25 Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
Og Adam kendte ydermere sin Hustru, og hun fødte en Søn og kaldte hans Navn Seth; thi Gud har sat mig, sagde hun, en anden Sæd i Abels Sted; thi Kain slog ham ihjel.
26 Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.
Og for Seth blev og født en Søn, og han kaldte hans Navn Enos; da begyndte man at paakalde Herrens Navn.

< Genesis 4 >