< Genesis 39 >
1 Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
Jožef je bil priveden dol v Egipt, in faraonov častnik Potifár, poveljnik straže, Egipčan, ga je kupil iz roke Izmaelcev, ki so ga privedli tja dol.
2 Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
Gospod pa je bil z Jožefom in bil je uspešen človek in bil je v hiši svojega gospodarja Egipčana.
3 Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
Njegov gospodar je videl, da je bil z njim Gospod in da je Gospod naredil, da je v njegovi roki vse uspevalo.
4 Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
Jožef je našel naklonjenost v njegovih očeh in mu služil. Postavil ga je za nadzornika nad svojo hišo in vse, kar je imel, je položil v njegovo roko.
5 Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
Pripetilo se je čez čas, ko ga je postavil za nadzornika v svoji hiši in nad vsem, kar je imel, da je Gospod zaradi Jožefa blagoslovil Egipčanovo hišo in Gospodov blagoslov je bil nad vsem, kar je imel v hiši in na polju.
6 Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
Vse, kar je imel, je pustil v Jožefovi roki in ni vedel, kar bi moral, razen kruha, ki ga je jedel. Jožef pa je bil čedne zunanjosti in lepega videza.
7 Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
Pripetilo se je po teh stvareh, da je gospodarjeva žena vrgla svoje oči na Jožefa in rekla: »Lezi z menoj.«
8 Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
Toda odklonil je in ženi svojega gospodarja rekel: »Glej, moj gospodar ne ve kaj je z menoj v hiši in vse, kar ima, je zaupal v mojo roko.
9 Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
Nikogar večjega v tej hiši ni kakor jaz niti ni nobene stvari zadržal pred menoj, razen tebe, ker si njegova žena; kako lahko jaz potem storim to veliko zlobnost in grešim zoper Boga?«
10 Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
Pripetilo se je, ko je dan za dnem govorila Jožefu, da ji ni prisluhnil, da leži z njo ali da bi bil z njo.
11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
Pripetilo se je okoli tega časa, da je Jožef odšel v hišo, da opravi svoje opravilo in tam v hiši ni bilo nikogar od ljudi.
12 Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
Ona pa ga je ujela za njegovo obleko, rekoč: »Lezi z menoj« in pustil je svojo obleko v njeni roki, pobegnil in izginil ven.
13 Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
Pripetilo se je, ko je videla, da je v njeni roki pustil svojo obleko in je pobegnil naprej,
14 iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
da je zaklicala k možem svoje hiše in jim govorila, rekoč: »Vidite, k nam je privedel Hebrejca, da nas zasmehuje. Prišel je k meni, da leži z menoj, jaz pa sem zaklicala z močnim glasom.
15 Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
Pripetilo se je, ko je zaslišal, da sem povzdignila svoj glas in zakričala, da je svojo obleko pustil pri meni, pobegnil in izginil ven.«
16 Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
Njegovo obleko je položila poleg sebe, dokler njen gospodar ni prišel domov.
17 Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
Govorila mu je glede na te besede, rekoč: »Hebrejski služabnik, ki si ga privedel k nam, je prišel noter k meni in me zasmehoval
18 Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
in pripetilo se je, ko sem povzdignila svoj glas in zakričala, da je svojo obleko pustil pri meni in pobegnil.«
19 Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
Pripetilo se je, ko je njegov gospodar slišal besede svoje žene, ki mu jih je govorila, rekoč: »Na ta način mi je storil tvoj služabnik, « da je bil vžgan njegov bes.
20 Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
Jožefov gospodar ga je vzel in ga vtaknil v ječo, kraj, kjer so bili zvezani kraljevi jetniki in bil je tam v ječi.
21 koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
Toda Gospod je bil z Jožefom in mu izkazal usmiljenje in mu dal naklonjenost v očeh čuvaja ječe.
22 Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
Čuvaj ječe je v Jožefovo roko zaupal vse jetnike, ki so bili v ječi in karkoli so tam storili, je bil on izvršitelj tega.
23 Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.
Čuvaj ječe ni gledal na nobeno stvar, ki je bila pod njegovo roko, ker je bil z njim Gospod in tisto, kar je naredil, je Gospod storil, da je to uspevalo.