< Genesis 39 >

1 Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
Иосиф а фост дус ын Еӂипт, ши Потифар, дрегэторул луй Фараон, кэпетения стрэжерилор, ун еӂиптян, л-а кумпэрат де ла исмаелиций каре-л адусесерэ аколо.
2 Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
Домнул а фост ку Иосиф, аша кэ тоате ый мерӂяу бине; ел локуя ын каса стэпынулуй сэу, еӂиптянул.
3 Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
Стэпынул луй а вэзут кэ Домнул ера ку ел ши кэ Домнул фэчя сэ-й мяргэ бине орь де че се апука.
4 Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
Иосиф а кэпэтат маре тречере ынаинтя стэпынулуй сэу, каре л-а луат ын служба луй, л-а пус май-маре песте каса луй ши й-а ынкрединцат тот че авя.
5 Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
Де ындатэ че Потифар л-а пус май-маре песте каса луй ши песте тот че авя, Домнул а бинекувынтат каса еӂиптянулуй дин причина луй Иосиф, ши бинекувынтаря Домнулуй а фост песте тот че авя ел: фие акасэ, фие ла кымп.
6 Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
Еӂиптянул а лэсат пе мыниле луй Иосиф тот че авя ши н-авя алтэ грижэ декыт сэ мэнынче ши сэ бя. Дар Иосиф ера фрумос ла статурэ ши плэкут ла кип.
7 Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
Дупэ кытэва време, с-а ынтымплат кэ неваста стэпынулуй сэу а пус окий пе Иосиф ши а зис: „Кулкэ-те ку мине!”
8 Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
Ел н-а воит ши а зис невестей стэпынулуй сэу: „Везь кэ стэпынул меу ну-мь чере сокотялэ де нимик дин касэ ши мь-а дат пе мынэ тот че аре.
9 Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
Ел ну есте май маре декыт мине ын каса ачаста ши ну мь-а оприт нимик, афарэ де тине, пентру кэ ешть неваста луй. Кум аш путя сэ фак еу ун рэу атыт де маре ши сэ пэкэтуеск ымпотрива луй Думнезеу?”
10 Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
Мэкар кэ еа ворбя ын тоате зилеле луй Иосиф, ел н-а воит сэ се кулче ши сэ се ымпреуне ку еа.
11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
Ынтр-о зи, кынд интрасе ын касэ ка сэ-шь факэ лукрул ши кынд ну ера аколо ничунул дин оамений касей,
12 Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
еа л-а апукат де хайнэ, зикынд: „Кулкэ-те ку мине!” Ел й-а лэсат хайна ын мынэ ши а фуӂит афарэ дин касэ.
13 Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
Кынд а вэзут еа кэ-й лэсасе хайна ын мынэ ши фуӂисе афарэ,
14 iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
а кемат оамений дин касэ ши ле-а зис: „Ведець, не-а адус ун евреу ка сэ-шь батэ жок де ной! Омул ачеста а венит ла мине ка сэ се кулче ку мине, дар еу ам ципат ын гура маре.
15 Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
Ши, кынд а вэзут кэ ридик гласул ши стриг, шь-а лэсат хайна лынгэ мине ши а фуӂит афарэ.”
16 Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
Ши а пус хайна луй Иосиф лынгэ еа пынэ с-а ынторс акасэ стэпынул луй.
17 Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
Атунч й-а ворбит астфел: „Робул ачела евреу пе каре ни л-ай адус а венит ла мине ка сэ-шь батэ жок де мине.
18 Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
Ши кум ам ридикат гласул ши ам ципат, шь-а лэсат хайна лынгэ мине ши а фуӂит афарэ.”
19 Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
Дупэ че а аузит кувинтеле невестей сале, каре-й зичя: „Ятэ че мь-а фэкут робул тэу”, стэпынул луй Иосиф с-а мыният фоарте таре.
20 Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
А луат пе Иосиф ши л-а арункат ын темницэ, ын локул унде ерау ынкишь ынтемницаций ымпэратулуй, ши астфел Иосиф а стат аколо, ын темницэ.
21 koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
Домнул а фост ку Иосиф ши Шь-а ынтинс бунэтатя песте ел. Л-а фэкут сэ капете тречере ынаинтя май-марелуй темницей.
22 Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
Ши май-мареле темницей а пус суб привегеря луй пе тоць ынтемницаций каре ерау ын темницэ. Ши нимик ну се фэчя аколо декыт прин ел.
23 Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.
Май-мареле темницей ну се май ынгрижя де нимик дин че авя Иосиф ын мынэ, пентру кэ Домнул ера ку ел. Ши Домнул ый дэдя избындэ ын тот че фэчя.

< Genesis 39 >