< Genesis 39 >

1 Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
Josef blev ført ned til Egypten; og Potifar, en egypter, som var hoffmann hos Farao og høvding over livvakten, kjøpte ham av ismaelittene som hadde hatt ham med sig dit.
2 Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
Men Herren var med Josef, så alt lyktes for ham; og han vedblev å være i huset hos sin herre egypteren.
3 Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
Da hans herre så at Herren var med ham, og at Herren lot alt det han gjorde, lykkes for ham,
4 Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
fant Josef nåde for hans øine og fikk gå ham til hånde; og han satte ham over sitt hus, og alt det han hadde, la han i hans hender.
5 Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
Og helt fra den tid han hadde satt ham over sitt hus og over alt det han hadde, velsignet Herren egypterens hus for Josefs skyld, og Herrens velsignelse var over alt det han hadde, både i huset og på marken.
6 Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
Og han overlot alt det han hadde, i Josefs hender, og han så ikke til med ham i noget, uten med den mat han selv åt. Og Josef var vakker av skapning og vakker å se til.
7 Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
Og nogen tid efter hendte det at hans herres hustru kastet sine øine på Josef og sa: Kom og ligg hos mig!
8 Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
Men han vilde ikke og sa til sin herres hustru: Min herre ser ikke til med mig i nogen ting i hele sitt hus, og alt det han eier, har han lagt i mine hender;
9 Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
han har ikke mere å si her i huset enn jeg, og han har ikke nektet mig noget uten dig, fordi du er hans hustru. Hvorledes skulde jeg da gjøre denne store ondskap og synde mot Gud?
10 Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
Som hun nu dag efter dag talte til Josef, og han ikke føide henne i å ligge hos henne og være sammen med henne,
11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
så hendte det en dag at han kom inn i huset for å gjøre sitt arbeid, mens ingen av husets folk var inne.
12 Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
Da grep hun fatt i hans kappe og sa: Ligg hos mig! Men han lot sin kappe efter sig i hennes hånd og flyktet ut av huset.
13 Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
Og da hun så at han hadde latt sin kappe efter sig i hennes hånd og var flyktet ut av huset,
14 iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
ropte hun på sine husfolk og sa til dem: Se, her har han ført en hebraisk mann hit til oss for å føre skam over oss; han kom inn til mig for å ligge hos mig, men jeg ropte så høit jeg kunde,
15 Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
og da han hørte at jeg satte i å rope, lot han sin kappe efter sig hos mig og flyktet ut av huset.
16 Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
Så lot hun hans kappe bli liggende hos sig til hans herre kom hjem.
17 Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
Da talte hun likedan til ham og sa: Den hebraiske træl som du har ført hit til oss, kom inn til mig for å føre skam over mig;
18 Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
men da jeg satte i å rope, lot han sin kappe efter sig hos mig og flyktet ut av huset.
19 Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
Da nu hans herre hørte hvad hans hustru fortalte, hvorledes hun sa: Således har din træl gjort mot mig, da optendtes hans vrede.
20 Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
Og Josefs herre tok og satte ham i fengslet, der hvor kongens fanger holdtes fengslet; og han blev sittende der i fengslet.
21 koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
Men Herren var med Josef og lot ham vinne alles hjerter og gav ham yndest hos fengslets overopsynsmann.
22 Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
Og fengslets overopsynsmann satte Josef til å se efter alle fangene som var i fengslet; og alt det som skulde gjøres der, det gjorde han.
23 Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.
Fengslets overopsynsmann så ikke efter nogen ting som han hadde under hender, fordi Herren var med ham; og hvad han gjorde, gav Herren lykke til.

< Genesis 39 >