< Genesis 39 >
1 Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
UJosefa wathathwa wasiwa eGibhithe. UPhothifa, owayengomunye wezikhulu zikaFaro, eyindunankulu yabalindi, wamthenga kuma-Ishumayeli abayibo abamletha khona.
2 Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
UThixo wayelaye uJosefa, waphumelela, wahlala endlini yenkosi yakhe umGibhithe.
3 Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
Kwathi inkosi yakhe ikubona ukuthi uThixo wayelaye lokuthi uThixo wamphumelelisa kukho konke ayekwenza,
4 Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
uJosefa wasethandeka kuye wasesiba yinceku yakhe. UPhothifa wasembeka ukuba ngumphathi womuzi wakhe, kwathi konke ayelakho wakubeka ezandleni zakhe.
5 Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
Kusukela ngesikhathi embeka ukuba ngumphathi womuzi wakhe lakho konke okwakungokwakhe, uThixo wawubusisa umuzi womGibhithe ngenxa kaJosefa. Isibusiso sikaThixo saba phezu kwakho konke uPhothifa ayelakho, loba kusendlini loba kusensimini.
6 Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
Ngakho watshiya konke okwakhe ezandleni zikaJosefa; kwathi ngoba uJosefa enguye ophetheyo wakhohlwa ngakho konke ngaphandle kokudla ayekudla. UJosefa lo wayemi kuhle, ebukeka,
7 Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
kwasekusithi ngemva kwesikhathi inkosikazi yenkosi yakhe yambuka, yamfisa uJosefa yathi, “Woza engutsheni lami!”
8 Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
Kodwa wala. Wamtshela wathi, “Njengoba kuyimi engiphetheyo, inkosi yami kayizihluphi ngalutho emzini wayo; yonke into elayo iyibeke ezandleni zami.
9 Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
Kakho omkhulu kulami kulumuzi. Inkosi yami kayingalisi lutho ngaphandle kwakho, ngoba wena ungumkayo. Pho ngingayenza kanjani into embi kanje, ngenze isono kuNkulunkulu na?”
10 Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
Kwathi loba emphikelela uJosefa insuku ngensuku, wala ukulala laye wala lokuthi ahlale laye.
11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
Ngolunye usuku wangena endlini ukuqhuba umsebenzi wakhe, izisebenzi zasendlini zingekho phakathi endlini.
12 Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
UmkaPhothifa wambamba ngesigqoko wathi, “Woza engutsheni ulale lami!” Kodwa waphunyuka wabaleka waphuma endlini, isigqoko sakhe sasala esandleni sowesifazane.
13 Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
Kwathi ebona ukuthi utshiye isigqoko sakhe esandleni sakhe njalo wabaleka endlini,
14 iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
owesifazane wamemeza izisebenzi zendlini wathi kuzo, “Khangelani, umHebheru lo walethwa lapha ukuzadlala ngathi! Ungene lapha efuna ukulala lami, kodwa ngahlaba umkhosi.
15 Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
Uthe esizwa ngihlaba umkhosi ngidinga uncedo, wasetshiya isigqoko sakhe eceleni kwami wabaleka waphuma endlini.”
16 Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
Wasigcina isigqoko eceleni kwakhe inkosi kaJosefa yaze yabuya ngekhaya.
17 Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
Waseyitshela indaba le wathi: “Isigqili somHebheru lesiyana owasilethela sona sifikile kimi ukuzadlala ngami.
18 Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
Kodwa ngonele ukuthi ngihlabe umkhosi ngidinga uncedo, satshiya isigqoko saso eceleni kwami sabaleka saphuma endlini.”
19 Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
Kwathi inkosi yakhe isizwile indaba eyayitshelwa ngumfazi esithi, “Singenze njalo isigqili sakho,” yathukuthela kakhulu.
20 Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
Inkosi yakhe uJosefa yamthatha yamphosela entolongweni, indawo lapho okwakuvalelwa khona izibotshwa zenkosi. Kodwa kwathi uJosefa ekhonapho entolongweni,
21 koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
uThixo waba laye; wamenzela umusa wamenza wathandeka emehlweni omphathijele.
22 Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
Ngakho-ke umphathijele wamkhweza wamenza umphathi wabo bonke ababebotshiwe besentolongweni, njalo kwaba nguye okhangele konke okwakusenziwa khona.
23 Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.
Umphathijele kazange azihluphe loba ngani eyayiphethwe nguJosefa ngoba uThixo wayelaye uJosefa, wamupha impumelelo kukho konke ayekwenza.