< Genesis 39 >
1 Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
Joseph fut descendu en Égypte. Potiphar, officier de Pharaon, chef des gardes, un Égyptien, l'acheta de la main des Ismaélites qui l'avaient fait descendre.
2 Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
Yahvé était avec Joseph, et il était un homme prospère. Il était dans la maison de son maître, l'Égyptien.
3 Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
Son maître vit que Yahvé était avec lui, et que Yahvé faisait prospérer entre ses mains tout ce qu'il faisait.
4 Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
Joseph trouva grâce à ses yeux. Il le servit, et Potiphar l'établit surveillant de sa maison, et il mit entre ses mains tout ce qui lui appartenait.
5 Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
Dès qu'il l'eut établi surveillant de sa maison et de tout ce qu'il possédait, Yahvé bénit la maison de l'Égyptien à cause de Joseph. La bénédiction de Yahvé fut sur tout ce qu'il avait, dans la maison et dans les champs.
6 Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
Il laissa tout ce qu'il avait entre les mains de Joseph. Il ne s'occupa de rien, sauf de la nourriture qu'il mangea. Joseph était bien bâti et beau.
7 Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
Après cela, la femme de son maître jeta les yeux sur Joseph, et elle dit: « Couche avec moi. »
8 Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
Mais il refusa, et dit à la femme de son maître: « Voici, mon maître ne sait pas ce que j'ai dans la maison, et il a remis entre mes mains tout ce qu'il possède.
9 Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
Personne n'est plus grand que moi dans cette maison, et il ne m'a rien caché que toi, parce que tu es sa femme. Comment donc pourrais-je commettre cette grande méchanceté et pécher contre Dieu? »
10 Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
Comme elle parlait à Joseph jour après jour, il ne l'écoutait pas, ne se couchait pas près d'elle et ne restait pas avec elle.
11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
Vers ce temps-là, il entra dans la maison pour faire son travail, et il n'y avait aucun des hommes de la maison à l'intérieur.
12 Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
Elle le saisit par son vêtement et lui dit: « Couche avec moi! » Il laissa son vêtement dans sa main, et sortit en courant.
13 Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
Lorsqu'elle vit qu'il avait laissé son vêtement dans sa main et qu'il était sorti en courant,
14 iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
elle appela les gens de sa maison et leur parla ainsi: « Voici qu'il a fait entrer chez nous un Hébreu pour se moquer de nous. Il est entré chez moi pour coucher avec moi, et j'ai crié d'une voix forte.
15 Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
Quand il a entendu que j'élevais la voix et que je criais, il a laissé son vêtement près de moi, et il est sorti en courant. »
16 Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
Elle déposa son vêtement près d'elle, jusqu'à ce que son maître revienne à la maison.
17 Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
Elle lui parla ainsi, et dit: Le serviteur hébreu que tu nous as amené est entré chez moi pour se moquer de moi;
18 Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
et comme j'élevais la voix et que je criais, il a laissé son vêtement près de moi et s'est enfui. »
19 Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
Lorsque son maître entendit les paroles de sa femme, qui lui disait: « Voici ce que ton serviteur m'a fait », sa colère s'enflamma.
20 Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
Le maître de Joseph le prit et le mit dans la prison, le lieu où l'on attachait les prisonniers du roi, et il y resta enfermé.
21 koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
Mais Yahvé était avec Joseph, il lui témoigna de la bonté et lui accorda sa faveur aux yeux du gardien de la prison.
22 Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
Le gardien de la prison remit entre les mains de Joseph tous les prisonniers qui se trouvaient dans la prison. Tout ce qu'ils y faisaient, il en était responsable.
23 Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.
Le gardien de la prison ne s'occupait de rien de ce qui était sous sa responsabilité, car l'Éternel était avec lui, et ce qu'il faisait, l'Éternel le faisait prospérer.