< Genesis 39 >

1 Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
Meanwhile, Joseph was led into Egypt. And Putiphar, a eunuch of Pharaoh, a leader of the army, an Egyptian man, purchased him from the hand of the Ishmaelites, by whom he was brought.
2 Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
And the Lord was with him, and he was a man who prospered in everything that he did. And he lived in the house of his lord,
3 Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
who knew very well that the Lord was with him, and that all the things that were done by him were directed by his hand.
4 Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
And Joseph found favor in the sight of his lord, and he ministered to him. And, having been placed in charge of everything by him, he governed the house that was entrusted to him and all the things that had been delivered to him.
5 Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
And the Lord blessed the house of the Egyptian, because of Joseph, and he multiplied all his substance, as much in the buildings, as in the fields.
6 Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
Neither did he know anything other than the bread that he ate. Now Joseph was beautiful in form, and stately in appearance.
7 Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
And so, after many days, his mistress cast her eyes on Joseph, and she said, “Sleep with me.”
8 Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
And without consenting at all to the wicked act, he said to her: “Behold, my lord has delivered all things to me, and he does not know what he has in his own house.
9 Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
Neither is there anything which is not in my power, or that he has not delivered to me, except you, for you are his wife. How then can I do this evil act and sin against my God?”
10 Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
With such words as these, throughout each day, the woman was pestering the young man, and he was refusing the adultery.
11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
Then it happened, on a certain day, that Joseph entered the house, and he was doing something, without any witnesses.
12 Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
And she, grasping the hem of his garment, said, “Sleep with me.” But he, leaving behind the cloak in her hand, fled and went outside.
13 Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
And when the woman saw the garment in her hands and herself being treated with disrespect,
14 iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
she called to herself the men of her house, and she said to them: “Lo, he has brought in a Hebrew man to abuse us. He entered toward me, in order to join with me; and when I had shouted out,
15 Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
and he had heard my voice, he left behind the cloak that I held, and he fled outside.”
16 Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
As a proof, therefore, of her fidelity, she retained the cloak, and she showed it to her husband, when he returned home.
17 Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
And she said: “The Hebrew servant, whom you have brought in to me, approached me to abuse me.
18 Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
And when he had heard me cry out, he left behind the cloak that I held, and he fled outside.”
19 Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
His lord, upon hearing these things, and having excessive trust in the words of his mate, was very angry.
20 Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
And he delivered Joseph into prison, where the prisoners of the king were kept, and he was enclosed in that place.
21 koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
But the Lord was with Joseph, and, having mercy on him, he gave him favor in the sight of the leader of the prison,
22 Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
who delivered into his hand all the prisoners who were held in custody. And whatever was done, was under him.
23 Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.
Neither did he himself know anything, having entrusted all things to him. For the Lord was with him, and he directed everything that he did.

< Genesis 39 >