< Genesis 38 >

1 Pa nthawi imeneyi, Yuda anasiyana ndi abale ake napita kukakhala ndi munthu wina wa ku Adulamu wotchedwa Hira.
Kwasekusithi ngalesosikhathi uJuda wehla esuka kubafowabo, waphambukela endodeni yeAdulamu, obizo layo linguHira.
2 Kumeneko, Yuda anaona mwana wamkazi wa munthu wina wa Chikanaani wotchedwa Suwa. Anamukwatira nagona naye malo amodzi.
UJuda wasebona lapho indodakazi yendoda umKhanani, obizo lakhe linguShuwa; wayithatha wangena kuyo.
3 Iye anatenga pathupi, nabala mwana wamwamuna amene anamutcha Eri.
Yasithatha isisu, yazala indodana; waseyitha ibizo layo uEri.
4 Anatenganso pathupi nabala mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Onani.
Yasiphinda ithatha isisu, yazala indodana; yayitha ibizo layo uOnani.
5 Anaberekanso mwana wina wamwamuna ndipo anamutcha Sela. Ameneyu anabadwa Yuda ali ku Kezibi.
Yasisengezelela futhi yazala indodana, yayitha ibizo layo uShela; kodwa wayeseKezibi ekuyizaleni kwayo.
6 Yuda anamupezera mkazi mwana wake woyamba uja Eri, ndipo dzina la mkaziyo linali Tamara.
UJuda wasemthathela uEri izibulo lakhe umfazi, njalo ibizo lakhe linguTamari.
7 Koma ntchito zoyipa za Eri, mwana wachisamba wa Yuda zinayipira Yehova. Choncho Mulungu anamulanga ndi imfa.
Kodwa uEri, izibulo likaJuda, wayemubi emehlweni eNkosi; iNkosi yasimbulala.
8 Pamenepo Yuda anati kwa Onani, “Kwatira mkazi wamasiye wa mʼbale wako. Ulowe chokolo kuti mʼbale wako akhale ndi mwana.”
UJuda wasesithi kuOnani: Ngena kumkamfowenu, wenze kuye imfanelo yomfowabo wendoda, umvusele umfowenu inzalo.
9 Koma Onani anadziwa kuti mwanayo sadzakhala wake. Choncho nthawi zonse pamene amagona naye mkaziyo, ankatayira umuna pansi kuti asamuberekere mwana mʼbale wake.
UOnani wayesazi-ke ukuthi inzalo kayiyikuba ngeyakhe. Kwasekusithi lapho engena kumkamfowabo, wayichithela emhlabathini, ukuze angamniki umfowabo inzalo.
10 Zimene ankachitazi zinayipira Yehova. Choncho anamulanganso ndi imfa.
Kwasekusiba kubi emehlweni eNkosi lokho akwenzayo; ngakho yambulala laye.
11 Kenaka Yuda anati kwa mpongozi wake Tamara, “Bwererani ku nyumba ya abambo anu ndi kukhala kumeneko ngati wamasiye mpaka mwana wanga Sela atakula.” Ananena izi chifukwa ankaopa kuti Sela angafenso ngati abale ake aja. Choncho Tamara anapita kukakhala ku nyumba ya abambo ake.
UJuda wasesithi kuTamari umalokazana wakhe: Hlala ungumfelokazi endlini kayihlo, aze akhule uShela indodana yami; ngoba wathi: Hlezi laye afe njengabafowabo. UTamari wasehamba wahlala endlini kayise.
12 Patapita nthawi yayitali, Batishua, mkazi wa Yuda anamwalira. Yuda atatha kulira maliro a mkazi wake, anapita, iyeyu pamodzi ndi bwenzi lake Hira, Mwadulamu uja, ku Timna kumene ankameta nkhosa zawo.
Emva kwensuku ezinengi yafa indodakazi kaShuwa, umkaJuda. UJuda eseziduduzile, wenyukela kubagundi bezimvu zakhe eThiminathi, yena lomngane wakhe uHira umAdulamu.
13 Tamara atamva kuti apongozi ake akupita ku Timna kukameta nkhosa,
Kwasekusaziswa kuTamari ukuthi: Khangela, uyihlozala wenyukela eThiminathi ukugunda izimvu zakhe.
14 iye anavula zovala zake za umasiye, nadziphimba nkhope ndi nsalu kuti asadziwike, ndipo anakhala pansi pa chipata cha ku Enaimu popita ku Timna. Tamara anachita izi chifukwa anaona kuti ngakhale Selayo anali atakula tsopano, iye sanaperekedwe kuti amulowe chokolo.
Wasekhulula izembatho zobufelokazi bakhe, wazimbomboza ngesimbombozo, wazigoqela, wahlala esangweni iEnayima, elisendleleni eya eThiminathi; ngoba wabona ukuthi uShela wayesekhulile, njalo wayengamnikwanga ukuba ngumkakhe.
15 Yuda atamuona anangomuyesa mkazi wadama chabe, chifukwa anadziphimba nkhope.
Lapho uJuda esembonile, wacabanga ukuthi uliwule, ngoba embomboze ubuso bakhe.
16 Tsono anapita kwa mkaziyo pamphepete pa msewu paja nati, “Tabwera ndigone nawe.” Apa Yuda sankadziwa kuti mkazi uja anali mpongozi wake. Ndiye mkazi uja anamufunsa Yuda nati, “Mudzandipatsa chiyani kuti ndigone nanu?”
Wasephambukela kuye endleleni wathi: Woza-ke, ngingene kuwe; ngoba wayengazi ukuthi ngumalokazana wakhe. Wasesithi: Uzanginikani ukuze ungene kimi?
17 Iye anati, “Ndidzakutumizira kamwana kambuzi ka mʼkhola mwanga.” Mkaziyo anayankha kuti, “Chabwino, ndavomera, koma mungandipatse chikole mpaka mutanditumizira mbuziyo?”
Wasesithi: Mina ngizathumela izinyane lembuzi elivela emhlanjini. Wasesithi: Uzanginika isibambiso uze ulithumele yini?
18 Iye anati, “Ndikupatse chikole chanji?” Mkaziyo anayankha, “Mundipatse mphete yanuyo, chingwe chanucho pamodzi ndi ndodo imene ili mʼdzanja lanulo.” Choncho anazipereka kwa iye nagona naye ndipo anatenga pathupi.
Wasesithi: Sibambiso bani engizakunika sona? Wasesithi: Indandatho elophawu lwakho, lentambo yakho, lodondolo lwakho olusesandleni sakho. Wasemupha, wangena kuye; wasethatha isisu sakhe.
19 Kenaka Tamara anachoka, navula nsalu anadziphimba nayo ija, navalanso zovala zake za umasiye zija.
Wasesukuma wahamba, wakhulula isimbombozo sakhe, wafaka izembatho zobufelokazi bakhe.
20 Tsono Yuda anatuma bwenzi lake Mwadulamu uja ndi kamwana kambuzi kaja kuti akapereke kwa mkazi wadama uja, ndi kuti akatero amubwezere chikole chake chija. Koma atafika sanamupezepo.
UJuda wasethumela izinyane lembuzi ngesandla somngane wakhe umAdulamu ukuze athathe isibambiso esandleni sowesifazana; kodwa kamtholanga.
21 Anawafunsa anthu a komweko, “Kodi mkazi wadama uja amene ankakhala pambali pa msewu wa ku Enaimu, ali kuti?” Iwo anayankha, “Sipanakhalepo mkazi wa dama aliyense pano.”
Wasebuza amadoda endawo yakowesifazana esithi: Lingaphi iwule elaliseEnayima endleleni? Asesithi: Kakuzanga kube khona iwule lapha.
22 Choncho anabwerera kwa Yuda nati, “Sindinamupeze mkazi uja. Kuwonjeza apo, anthu a kumeneko amati, ‘Sipanakhalepo mkazi wadama pano.’”
Wasebuyela kuJuda wathi: Kangilitholanga, futhi lamadoda endawo athi: Kakuzanga kube khona iwule lapha.
23 Pamenepo Yuda anati, “Mulekeni atenge zinthuzo zikhale zake, kuopa kuti anthu angatiseke. Ine sindinalakwe, ndinamutumizira kamwana kambuzika, koma simunamupeze.”
UJuda wasesithi: Kalizithathele, hlezi sideleleke; khangela, ngithumele lelizinyane, kodwa wena kawumtholanga.
24 Patapita miyezi itatu, Yuda anawuzidwa kuti, “Mpongozi wanu Tamara anachita zadama, ndipo zotsatira zake nʼzakuti ali ndi pathupi.” Yuda anati, “Kamutulutseni ndipo mukamutenthe kuti afe!”
Kwasekusithi phose emva kwenyanga ezintathu kwaziswa kuJuda ukuthi: UTamari umalokazana wakhe ufebile, futhi khangela-ke, ulesisu sokufetshwa. UJuda wasesithi: Mkhupheni atshiswe.
25 Akumutulutsa, iye anatuma mawu kwa apongozi ake. Anati, “Ndili ndi pathupi pa munthu amene ndi mwini wake wa zinthu izi. Taziyangʼanitsitsani, kodi mwini wa khoza, chingwe ndi ndodo yoyenderayi ndi yani?”
Esekhutshiwe, yena wathumela kuyisezala, esithi: Ngoniwe yindoda engumnini walezizinto. Wathi futhi: Ake uhlolisise ukuthi ngezikabani lezizinto, indandatho elophawu lezintambo lodondolo.
26 Yuda anazizindikira zinthuzo ndipo anati, “Uyu ndi wolungama kuposa ine, chifukwa sindinamupereke kwa mwana wanga Sela.” Ndipo Yuda sanagone nayenso.
UJuda wasezivuma wathi: Ulungile kulami, ngakho njengoba ngingamnikanga uShela indodana yami. Njalo kabanga esamazi futhi.
27 Pamene Tamara nthawi inamukwanira yoti abeleke, mʼmimbamo munali mapasa.
Kwasekusithi esikhathini sokubeletha kwakhe, khangela-ke, amaphahla ayesesiswini sakhe.
28 Pamene ankabereka, mmodzi wa iwo anatulutsa dzanja lake. Choncho mzamba anatenga kawulusi kofiira nakamangirira pa mkono pa mwanayo nati, “Uyu ndiye anayamba kubadwa.”
Kwasekusithi ekubeletheni kwakhe, elinye lakhupha isandla; umbelethisi wasithatha, wabopha intambo ebomvu esandleni salo, esithi: Lo uzaphuma kuqala.
29 Koma pamene anabweza mkonowo, mʼbale wake anabadwa ndipo mzamba anati, “Wachita kudziphotcholera wekha njira chonchi!” Ndipo anamutcha Perezi.
Kodwa kwathi lifinyeza isandla salo, khangela-ke umfowabo waphuma; wasesithi: Ufohle njani? Ukufohla kakube phezu kwakho. Wasemutha ibizo lakhe uPerezi.
30 Pambuyo pake mʼbale wake amene anali ndi ulusi wofiira pa mkono wake uja anabadwa ndipo anapatsidwa dzina lakuti Zera.
Emva kwalokhu kwasekuphuma umfowabo owayelentambo ebomvu esandleni sakhe; wasemutha ibizo lakhe uZera.

< Genesis 38 >