< Genesis 35 >

1 Tsono Mulungu anati kwa Yakobo, “Nyamuka uchoke kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ukamange guwa lansembe la Mulungu amene anadza kwa iwe pamene umathawa Esau, mʼbale wako.”
Tedae Pathen loh Jakob la, “Thoo, Bethel la cet lamtah pahoi khosa. Te phoeiah na maya Esau mikhmuh lamkah na yong vaengah nang taengah aka phoe Pathen ham hmueihtuk khaw pahoi saii,” a ti nah.
2 Choncho Yakobo anawuza a pa banja pake ndi onse amene anali naye kuti, “Chotsani milungu yachilendo imene muli nayo, ndipo mudziyeretse nokha ndi kusintha zovala zanu.
Te dongah Jakob loh amah imkhuikho neh a taengkah aka om boeih taengah, “Nangmih lakli kah kholong pathen rhoek te voei uh. Te phoeiah caihcil uh lamtah na himbai te tho uh laeh.
3 Tiyeni tinyamuke kuchoka kuno kupita ku Beteli. Kumeneko ndikamumangira guwa lansembe Mulungu amene anandithandiza pa nthawi za masautso anga, komanso amene wakhala nane mʼmayendedwe anga onse.”
Thoo uh sih lamtah Bethel la cet uh sih. Ka citcai tue vaengah kai aka doo tih ka caeh long ah kai taengah aka om Pathen ham hmueihtuk pahoi ka saii ni,” a ti nah.
4 Choncho anamupatsa Yakobo milungu yachilendo yonse imene anali nayo pamodzi ndi ndolo. Iye anazikwirira pansi pa mtengo wa thundu ku Sekemu.
Te dongah amih kut kah kholong pathen rhoek boeih neh a hna dongkah hnaii te Jakob taengah a paek uh tih Jakob loh Shekhem taengkah rhokael hmuiah a up.
5 Pamenepo ananyamuka, ndipo mtima woopa Mulungu unagwera anthu onse a mʼmizinda yozungulira, kotero kuti palibe aliyense amene anatsatira banja la Yakobo.
Tedae a caeh uh neh Pathen kah mueirhih loh khopuei kaepvai ah yaal tih Jakob ca te hloem uh pawh.
6 Yakobo ndi anthu onse anali naye aja anafika ku Luzi (ku Beteli) mu dziko la Kanaani.
Te phoeiah Jakob neh amah taengkah a pilnam boeih loh Kanaan kho kah Luz Bethel te a pha uh.
7 Kumeneko anamanga guwa lansembe nalitcha Eli Beteli, chifukwa kunali kumeneko kumene Mulungu anadziwulula yekha kwa Yakobo pamene ankathawa mʼbale wake.
Te vaengah hmueihtuk pahoi a suem tih a hmuen te El Bethel a sui. A maya mikhmuh lamloh a yong vaengah khaw te rhoek ah ni anih ham Pathen a phoe pah dongah ni.
8 Debora mlezi wa Rakele anamwalira komweko nayikidwa mʼmanda pansi pa mtengo wa thundu cha kumunsi kwa Beteli. Choncho panatchedwa Aloni-Bakuti (mtengo wamaliro).
Rebekah kah cakhoem Deborah a duek vaengah khaw Bethel kungdak kah thingnu hmuiah a up tih a ming te Allon Bakuth la a khue.
9 Yakobo atabwera kuchokera ku Padanaramu, Mulungu anabweranso kwa iye namudalitsa.
Paddanaram lamkah koep a mael vaengah khaw Jakob taengah Pathen a phoe pah tih yoethen a paek.
10 Mulungu anati kwa iye, “Dzina lako ndiwe Yakobo, koma sudzatchedwanso Yakobo; koma udzatchedwa Israeli.” Choncho anamutcha iye Israeli.
Te vaengah Pathen loh anih te, “Na ming he Jakob dae na ming te Jakob la n'khue voel pawt vetih Israel ni nang ming la aka om eh?,” a ti nah. Te dongah a ming te Israel la a khue bal.
11 Ndipo Mulungu anati kwa iye, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse; berekanani ndi kuchulukana. Mtundu wa anthu, inde, mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe, ndipo ena mwa zidzukulu zako adzakhala mafumu.
Te phoeiah anih te Pathen loh, “Kai he Pathen Tlungthang ni. Pungtai lamtah namtom ah ping uh. Namtom hlangping khaw nang lamkah ha thoeng vetih na pumpu lamloh manghai thoeng uh ni.
12 Dziko limene ndinapereka kwa Abrahamu ndi Isake ndiliperekanso kwa iwe. Lidzakhala lako ndi la zidzukulu zako.”
Abraham neh Isaak taengah ka paek hmuen te nang taengah kan paek vetih nang phoeikah na tiingan taengah khaw khohmuen te ka paek ni,” a ti nah.
13 Kenaka Mulungu anamusiya Yakobo.
Tekah hmuen ah Jakob neh a cal rhoi pangthuem Pathen te anih taeng lamloh vik cet.
14 Yakobo anayika mwala wachikumbutso pa malo pamene Mulungu anayankhula naye paja. Iye anathirapo nsembe yachakumwa ndi yamafuta.
Te dongah amah neh a voek nah hmuen ah Jakob loh kaam a ling tih kaam lung te tuisi a suep tih situi a bueih.
15 Yakobo anawatcha malo amene Mulungu anayankhula naye aja kuti Beteli.
Te phoeiah Pathen loh amah a voek nah hmuen ming te Jakob loh Bethel la pahoi a khue.
16 Kenaka anachoka ku Beteli. Koma ali pafupi kufika ku Efurata nthawi yakuti Rakele aone mwana inakwana. Iye anavutika pobereka.
Te phoeiah Bethel lamkah puen uh tih Epharath la caeh ham kho te a lak om pueng dae Rakhel te camoe om tih a ca om bahoeng kuel.
17 Akanali chivutikire choncho, mzamba anamulimbikitsa nati, “Usaope pakuti ubala mwana wina wamwamuna.”
Tedae a ca om a a tloh vaengah anih te ca aka om sak loh, “Tahae kah khaw nang ham tongpa la koep a om dongah rhih boeh,” a ti nah.
18 Tsono pamene Rakele ankapuma wefuwefu (popeza ankamwalira) iye anatcha mwana uja kuti Beni-Oni. Koma abambo ake anamutcha kuti Benjamini.
A duek tom kah a hinglu a pat thuk vaengah camoe ming te Benoni la a khue. Tedae a napa long tah anih te Benjamin la a khue.
19 Choncho Rakele anamwalira ndipo anayikidwa pa njira yopita ku Efurata (Kumeneko ndiye ku Betelehemu).
Te vaengah Rakhel duek tih Epharath Bethlehem long ah te a up.
20 Pa manda ake, Yakobo anayimika mwala wachikumbutso wa pa manda ndipo ulipobe mpaka lero.
Rakhel kah hlan soah Jakob loh kaam a ling te tihnin due Rakhel phuel kah kaam la om.
21 Israeli (Yakobo) anasunthanso nakamanga tenti yake kupitirira nsanja ya Ederi.
Te phoeiah Israel te cet tih Mikdaleder kah a voel ah dap a tuk.
22 Israeli akanali mʼderali, Rubeni anapita nakagonana ndi Biliha, mdzakazi wa abambo ake. Yakobo uja anazimva zimenezi. Yakobo anali ndi ana aamuna khumi ndi awiri:
Tedae tekah kho ah khosa la Israel a om vaengah Reuben te cet tih a napa kah yula Bilhah taengah a yalh te Israel loh a yaak. Te vaengah Jakob ca rhoek hlang hlai nit om uh.
23 Ana a Leya ndi awa: Rubeni anali mwana woyamba wa Yakobo, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, ndi Zebuloni.
Leah ca rhoek ah Reuben te Jakob caming la om tih Simeon, Levi, Judah, Issakhar neh Zebulun omuh.
24 Ana a Rakele ndi awa: Yosefe ndi Benjamini.
Rakhel ca rhoi la Joseph neh Benjamin om.
25 Ana a Biliha, wantchito wa Rakele ndi awa: Dani ndi Nafutali.
Rakhel imom Bilhah ca rhoi la Dan neh Naphtali om.
26 Ana a Zilipa wantchito wa Leya ndi awa: Gadi ndi Aseri. Awa ndiwo ana a Yakobo amene anabadwira ku Padanaramu.
Leah salnu Zilpah ca la Gad neh Asher he om tih Paddanaram ah Jakob ca tongpa la a cun pah.
27 Yakobo anafika ku mudzi kwa abambo ake Isake ku Mamre, (kumene kunkatchedwa ku Kiriyati-Ariba kapenanso Hebroni) kumene Abrahamu ndi Isake anakhalako kale.
Te phoeiah Jakob loh Mamre Kiriatharba Hebron kah a napa Isaak taengla a pha. Teah te Abraham khaw Isaak khaw bakuep.
28 Isake anakhala ndi moyo zaka 180.
Te vaengah Isaak kah khohnin loh kum ya neh kum sawmrhet lo coeng.
29 Anamwalira ali wokalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. Ndipo ana ake Esau ndi Yakobo anamuyika mʼmanda.
Isaak khaw pal tih a duek vaengah patong kum soep la a pilnam taengah khoem uh coeng. Anih te a ca rhoi Esau neh Jakob loh a up.

< Genesis 35 >