< Genesis 33 >
1 Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja.
Jakob je povzdignil svoje oči, pogledal in glej, prišel je Ezav in z njim štiristo mož. Otroke je razdelil Lei in Raheli ter dvema pomočnicama.
2 Anayika antchito ndi ana awo patsogolo, kenaka nʼkubwera Leya ndi ana ake, ndipo pambuyo pawo Rakele ndi Yosefe.
Najbolj spredaj je postavil pomočnici ter njune otroke, za njimi Leo ter njene otroke, nazadnje pa Rahelo in Jožefa.
3 Iye mwini anakhala patsogolo nawerama mpaka kukhudza pansi kasanu ndi kawiri pamene amayandikira mʼbale wake.
Šel je pred njimi in se sedemkrat priklonil do tal, dokler se ni približal svojemu bratu.
4 Koma Esau anathamanga kukakumana ndi Yakobo ndipo anamukupatira namupsompsona. Onse awiri ankangolira.
Ezav je stekel, da ga sreča, ga objel, se spustil na njegov vrat in ga poljubil, in oba sta jokala.
5 Kenaka Esau ataona amayi ndi ana awo anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi anthu amene uli nawowa ndi a ndani?” Yakobo anayankha kuti, “Awa ndi ana amene Mulungu, mwa kukoma mtima kwake, wapereka kwa mtumiki wanune.”
Povzdignil je svoje oči in zagledal ženske in otroke ter rekel: »Kdo so ti s teboj?« Rekel je: »Otroci, ki jih je Bog milostljivo dal tvojemu služabniku.«
6 Tsono antchito aja anayandikira naweramitsa mitu pansi.
Nato sta se približali pomočnici, oni in njuni otroci ter se priklonili.
7 Kenaka, Leya ndi ana ake anabwera. Nawonso anaweramitsa mitu pansi. Potsiriza pa onse anabwera Yosefe ndi Rakele naweramitsanso mitu yawo pansi.
Tudi Lea s svojimi otroki se je približala in se priklonila in potem sta prišla bliže Jožef in Rahela ter se oba priklonila.
8 Esau anafunsa kuti, “Kodi gulu la ziweto ndakumana nalo lija ndi layani?” Yakobo anayankha nati, “Mbuye wanga, gulu lija ndi lanu kuti mundikomere mtima.”
Rekel je: »Kaj nameravaš z vso to čredo, ki sem jo srečal?« On pa je rekel: » Ti so, da najdem milost v očeh mojega gospoda.«
9 Koma Esau anati, “Mʼbale wanga, ine ndili nazo kale zambiri. Zinthu zakozi sunga.”
Ezav je rekel: »Dovolj imam, moj brat. To, kar imaš, obdrži zase.«
10 Yakobo anati, “Chonde musatero. Ngati mwandikomera mtima, landirani mphatso yangayi kuchokera kwa ine. Pakuti ndi mmene mwandirandira bwinomu, ine ndikamaona nkhope yanu ndikuchita ngati ndikuona nkhope ya Mulungu.
Jakob je rekel: »Ne, prosim te, če sem torej našel milost v tvojih očeh, potem sprejmi moje darilo v moji roki, kajti zato sem videl tvoj obraz, kot da sem videl Božje obličje in ti si bil zadovoljen z menoj.
11 Chonde, landirani mphatso imene ndakutengeraniyi, popeza Mulungu wandikomera mtima kwambiri moti ndili ndi zonse zimene ndizifuna.” Ndipo popeza kuti Yakobo anamuwumiriza, Esau analandira.
Vzemi, prosim te, moj blagoslov, ki je priveden k tebi, ker je Bog milostljivo postopal z menoj in ker imam dovolj.« Prigovarjal mu je in on je to vzel.
12 Ndipo Esau anati, “Tiyeni tizipita; nditsagana nanu.”
Rekel je: »Naj greva najino potovanje in naj greva, jaz pa bom šel pred teboj.«
13 Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa.
Rekel mu je: »Moj gospod ve, da so otroci nežni in [da] so z menoj tropi in črede z mladiči in če jih bodo ljudje en dan preveč gonili, bo ves trop poginil.
14 Choncho, mbuye wanga lolani kuti mutsogole. Ine ndiziyenda pangʼonopangʼono pambuyo pa ziwetozi ndi anawa mpaka ndikafika ku Seiri.”
Naj moj gospod, prosim te, gre preko pred svojim služabnikom, jaz pa bom mirno vodil dalje, kolikor bodo živina, ki gre pred menoj in otroci zmožni prenesti, dokler ne pridem k mojemu gospodu v Seír.«
15 Esau anati, “Ndiye bwanji ndikusiyireko ena mwa anthu anga.” Koma Yakobo anati, “Koma muchitiranji zimenezi? Chachikulu nʼkuti mwandilandira bwino, mbuye wanga.”
Ezav je rekel: »Naj torej pustim s teboj nekaj ljudstva, ki je z menoj.« Rekel je: »Kaj potrebujem to? Naj najdem milost v očeh svojega gospoda.«
16 Choncho tsiku limenelo Esau anayamba ulendo wobwerera ku Seiri.
Tako se je ta dan Ezav vrnil na svojo pot v Seír.
17 Komabe Yakobo anapita ku Sukoti. Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Sukoti.
Jakob pa je odpotoval v Sukót, si zgradil hišo in naredil šotore za svojo živino. Zato se ime kraja imenuje Sukót.
18 Mmene ankabwerera kuchokera ku Padanaramu, Yakobo anafika ku Salemu, mzinda wa Sekemu ku Kanaani. Anamanga msasa pamalopo moyangʼanana ndi mzindawo.
Ko je Jakob prišel iz Padan–arama, je prišel v Salem, mesto v Sihemu, ki je v kánaanski deželi in svoj šotor postavil pred mestom.
19 Malo amenewo anagula kwa zidzukulu za Hamori, abambo a Sekemu ndi ndalama 100 zasiliva.
Kupil je kos poljskega zemljišča, kjer je razširil svoj šotor, iz roke otrok Hamórja, Sihemovega očeta, za sto koščkov denarja.
20 Pamalopo anamanganso guwa lansembe, nalitcha Eli Elohe Israeli.
Tam je postavil oltar in ga imenoval El–elohe–Izrael.