< Genesis 33 >

1 Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja.
Iacob lyfte vp his eyes and sawe hys brother Esau come and with him. iiij. hundred men. And he deuyded the childern vnto Lea and vnto Rahel and vnto ye ij. maydens.
2 Anayika antchito ndi ana awo patsogolo, kenaka nʼkubwera Leya ndi ana ake, ndipo pambuyo pawo Rakele ndi Yosefe.
And he put the maydens ad their childern formest ad Lea and hir childern after and Rahel ad Ioseph hindermost.
3 Iye mwini anakhala patsogolo nawerama mpaka kukhudza pansi kasanu ndi kawiri pamene amayandikira mʼbale wake.
And he went before them and fell on the grownde, vij. tymes vntill he came vnto his brother.
4 Koma Esau anathamanga kukakumana ndi Yakobo ndipo anamukupatira namupsompsona. Onse awiri ankangolira.
Esau ranne agaynst him and enbraced hym and fell on his necke and kyssed him and they wepte.
5 Kenaka Esau ataona amayi ndi ana awo anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi anthu amene uli nawowa ndi a ndani?” Yakobo anayankha kuti, “Awa ndi ana amene Mulungu, mwa kukoma mtima kwake, wapereka kwa mtumiki wanune.”
And he lifte vp his eyes and sawe the wyves and their childern and sayde: what are these which thou there hast? And he sayde: they are the childern which God hath geuen thy seruaunte.
6 Tsono antchito aja anayandikira naweramitsa mitu pansi.
Than came the maydens forth ad dyd their obaysaunce.
7 Kenaka, Leya ndi ana ake anabwera. Nawonso anaweramitsa mitu pansi. Potsiriza pa onse anabwera Yosefe ndi Rakele naweramitsanso mitu yawo pansi.
Lea also and hir childern came and dyd their obaysaunce. And last of all came Ioseph and Rahel and dyd their obaysaunce.
8 Esau anafunsa kuti, “Kodi gulu la ziweto ndakumana nalo lija ndi layani?” Yakobo anayankha nati, “Mbuye wanga, gulu lija ndi lanu kuti mundikomere mtima.”
And he sayde: what meanyst thou with all ye drooues which I mett. And he answered: to fynde grace in the syghte of my lorde.
9 Koma Esau anati, “Mʼbale wanga, ine ndili nazo kale zambiri. Zinthu zakozi sunga.”
And Esau sayde: I haue ynough my brother kepe that thou hast vnto thy silf.
10 Yakobo anati, “Chonde musatero. Ngati mwandikomera mtima, landirani mphatso yangayi kuchokera kwa ine. Pakuti ndi mmene mwandirandira bwinomu, ine ndikamaona nkhope yanu ndikuchita ngati ndikuona nkhope ya Mulungu.
Iacob answered: oh nay but yf I haue founde grace in thy syghte receaue my preaset of my hade: for I haue sene thy face as though I had sene ye face of God: wherfore receaue me to grace
11 Chonde, landirani mphatso imene ndakutengeraniyi, popeza Mulungu wandikomera mtima kwambiri moti ndili ndi zonse zimene ndizifuna.” Ndipo popeza kuti Yakobo anamuwumiriza, Esau analandira.
and take my blessynge that I haue brought the for God hath geuen it me frely. And I haue ynough of all thynges. And so he compelled him to take it.
12 Ndipo Esau anati, “Tiyeni tizipita; nditsagana nanu.”
And he sayde: let us take oure iourney and goo and I will goo in thy copany.
13 Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa.
And he sayde vnto him: my lorde knoweth that I haue tendre childern ewes and kyne with yonge vnder myne hande which yf men shulde ouerdryue but euen one daye the hole flocke wolde dye.
14 Choncho, mbuye wanga lolani kuti mutsogole. Ine ndiziyenda pangʼonopangʼono pambuyo pa ziwetozi ndi anawa mpaka ndikafika ku Seiri.”
Let my lorde therfore goo before his servaunte and I will dryue fayre and softly accordynge as the catell that goth before me and the childern be able to endure: vntill I come to mi lorde vnto Seir.
15 Esau anati, “Ndiye bwanji ndikusiyireko ena mwa anthu anga.” Koma Yakobo anati, “Koma muchitiranji zimenezi? Chachikulu nʼkuti mwandilandira bwino, mbuye wanga.”
And Esau sayde: let me yet leaue some of my folke with the. And he sayde: what neadeth it? let me fynde grace in the syghte of my lorde
16 Choncho tsiku limenelo Esau anayamba ulendo wobwerera ku Seiri.
So Esau went his waye agayne yt same daye vnto Seir.
17 Komabe Yakobo anapita ku Sukoti. Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Sukoti.
And Iacob toke his iourney toward Sucoth and bylt him an house and made boothes for his catell: wherof the name of the place is called Sucoth.
18 Mmene ankabwerera kuchokera ku Padanaramu, Yakobo anafika ku Salemu, mzinda wa Sekemu ku Kanaani. Anamanga msasa pamalopo moyangʼanana ndi mzindawo.
And Iacob went to Salem to ye cytie of Sichem in the lande of Canaa after that he was come from Mesopotamia and pitched before the cyte
19 Malo amenewo anagula kwa zidzukulu za Hamori, abambo a Sekemu ndi ndalama 100 zasiliva.
and bought a parcell of ground where he pitched his tent of the childern of Hemor Sichems father for an hundred lambes.
20 Pamalopo anamanganso guwa lansembe, nalitcha Eli Elohe Israeli.
And he made there an aulter and there called vpon the myghtie God of Israell.

< Genesis 33 >