< Genesis 32 >
1 Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
Men Jacob for sin väg, och Guds Änglar mötte honom.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
Och då han såg dem, sade han: Detta äro Guds härar; och kallade det rummet Mahanaim.
3 Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
Men Jacob sände båd fram för sig till sin broder Esau in uti Seirs land, i Edoms ängd.
4 Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
Och befallte dem, och sade: Så säger minom herra Esau: Din tjenare Jacob låter säga dig, jag hafver varit ute när Laban, och hafver allt härtill varit ibland främmande;
5 Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
Och hafver fä och åsnor, får, tjenare och tjenarinnor; och hafver utsändt, och låtit dig minom herra det bebåda, på det jag måtte finna nåd för din ögon.
6 Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
Boden kommo igen till Jacob, och sade: Vi kommom till din broder Esau, och han reser emot dig med fyrahundrade män.
7 Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
Då fruktade Jacob storliga, och var förfärad: Och skifte folket, som var när honom, och får, och fä, och camelar, i två skarar.
8 Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
Och sade: Om Esau kommer på den ena skaran, och står honom, så må den andre undkomma.
9 Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
Ytterligare sade Jacob: Gud, mins faders Abrahams Gud, mins faders Isaacs, Herre, du som till mig sagt hafver: Far åter in i ditt land till dina fränder, jag vill göra dig godt;
10 Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
Jag är för ringa till all den barmhertighet och all den trohet, som du med dinom tjenare gjort hafver; förty jag hade icke mer än denna stafven, då jag gick öfver denna Jordanen, och nu är jag till två skarar vorden.
11 Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
Hjelp mig utu mins broders hand, utu Esaus hand; ty jag fruktar för honom; att han icke kommer, och står mig både mödrar och barn.
12 Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
Du hafver sagt: Jag vill göra dig godt, och göra din säd som sanden i hafvet, den så mycken är, att han ej kan räknas.
13 Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
Och han blef der den nattena, och tog af thy han för handena hade, skänker till sin broder Esau.
14 Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
Tuhundrade getter, tjugu bockar, tuhundrade får, tjugu vädrar;
15 ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
Och tretio däggande camelar med deras föl, fyratio kor, och tio oxar; tjugu åsninnor, med tio föl;
16 Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
Och fick dem under sina tjenares händer, ju hvar hjorden för sig, och sade till dem: Går fram för mig, och låter vara rum emellan den ena hjorden efter den andra.
17 Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
Och böd den första, och sade: När min broder Esau möter dig, och frågar dig: Hvem hörer du till, och hvart vill du, och hvem hörer det till, som du drifver för dig?
18 Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
Skall du säga: Det hörer dinom tjenare Jacob till; han sände sinom herra Esau skänker, och kommer härefter.
19 Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
Så böd han ock den andra, och den tredje, och allom dem som gingo efter hjorden, och sade: Som jag hafver sagt eder, så säger till Esau, när I finnen honom.
20 Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
Och säger ju det med: Si, Jacob din tjenare är efter oss. Förty han tänkte, jag vill blidka honom med den skänken, som går för mig; sedan vill jag se honom; kan hända att han undfår mig väl.
21 Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
Så gingo skänkningarna fram före honom; men han blef den nattena i lägret.
22 Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
Och stod upp om nattena, och tog sina två hustrur, och de två tjensteqvinnorna, och sin ellofva barn, och for till vadet Jabbok:
23 Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
Tog dem och förde dem öfver älfvena, så att det han hade, kom öfver.
24 Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
Och han blef på den sidone allena. Då brottades en man med honom till dess morgonrodnen uppgick.
25 Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
Och då han såg, att han icke kunde öfvervinna honom, rörde han hans höftes sena, och straxt förtvinade hans höftes sena.
26 Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
Och han sade: Låt mig gå, ty morgonrodnen går upp; men han svarade: Jag släpper dig icke, med mindre du välsignar mig.
27 Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
Han sade: Huru heter du? Han svarade: Jacob.
28 Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
Han sade: Du skall icke mer heta Jacob, utan Israel. Förty du hafver med Gud och menniskor kämpat, och hafver fått öfverhandena.
29 Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
Och Jacob frågade honom, och sade: Huru heter du? Men han sade: Hvi frågar du, huru jag heter? Och han välsignade honom der sammastädes.
30 Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
Och Jacob kallade det rummet Pnuel; ty jag hafver sett Gud under ansigtet, och min själ är frälst vorden.
31 Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
Och som han kom fram om Pnuel, gick honom solen upp, och han haltade i sine höft.
32 Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.
Fördenskull äta Israels barn inga höftsene ännu i dag, derföre, att Jacobs höftsena rörd vardt.