< Genesis 32 >

1 Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
Jakub też poszedł swoją drogą i spotkali go aniołowie Boga.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
Gdy Jakub ich ujrzał, powiedział: To obóz Boga. I nadał temu miejscu nazwę Machanaim.
3 Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
Potem Jakub wysłał przed sobą posłańców do swego brata Ezawa, do ziemi Seir, do krainy Edomu.
4 Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
I rozkazał im: Tak powiecie do mego pana Ezawa: To mówi twój sługa Jakub: Byłem gościem u Labana i przebywałem z nim aż do tego czasu.
5 Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
Mam woły, osły i owce, służących i służące, a posyłam oznajmić to memu panu, żebym znalazł łaskę w twoich oczach.
6 Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
Posłańcy wrócili do Jakuba i mówili: Przyszliśmy do twego brata Ezawa, a on też idzie naprzeciwko ciebie, a z nim czterystu mężów.
7 Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
Jakub bardzo się przestraszył i ogarnęła go trwoga. Podzielił więc lud, który z nim [był], oraz owce, woły i wielbłądy na dwa obozy.
8 Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
I powiedział: Jeśli Ezaw przyjdzie do jednego obozu i uderzy na niego, to drugi obóz ocaleje.
9 Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
Potem Jakub powiedział: Boże mego ojca Abrahama i Boże mego ojca Izaaka, PANIE, który do mnie powiedziałeś: Wróć do twojej ziemi i do twojej rodziny, a będę ci wyświadczał dobro.
10 Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
Nie jestem godzien wszelkiego miłosierdzia i całej wierności, które okazałeś swemu słudze. Bo tylko o lasce przeszedłem ten Jordan, a teraz mam dwa obozy.
11 Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
Wyrwij mnie, proszę, z ręki mego brata, z ręki Ezawa, bo się go boję, że przyjdzie i zabije mnie [i] matki z dziećmi.
12 Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
Ty bowiem powiedziałeś: Na pewno będę ci wyświadczał dobro i rozmnożę twoje potomstwo jak piasek morski, który nie może być zliczony z powodu jego mnóstwa.
13 Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
I przenocował tam tej nocy, i wziął z tego, co miał pod ręką, dar dla swego brata Ezawa;
14 Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
Dwieście kóz i dwadzieścia kozłów, dwieście owiec i dwadzieścia baranów;
15 ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
Trzydzieści karmiących wielbłądzic z młodymi, czterdzieści krów i dziesięć wołów, dwadzieścia oślic i dziesięcioro ośląt.
16 Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
I oddał [je] w ręce swoich sług, każde stado oddzielnie, i powiedział do swoich sług: Idźcie przede mną i zachowajcie odstęp między stadami.
17 Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
I rozkazał pierwszemu: Gdy spotka cię mój brat Ezaw, a spyta cię: Czyj jesteś? I dokąd idziesz? A czyje to [stado] przed tobą?
18 Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
Wtedy odpowiesz: To jest dar od twego sługi Jakuba, posłany memu panu Ezawowi. A oto on sam [idzie] za nami.
19 Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
Tak też rozkazał drugiemu i trzeciemu, i wszystkim idącym za tymi stadami: Tymi słowy mówcie do Ezawa, gdy go spotkacie.
20 Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
Powiecie [mu] też: Oto twój sługa Jakub [idzie] za nami. Myślał bowiem: Przebłagam go darem, który idzie przede mną, a potem zobaczę jego oblicze. Może mnie przyjmie łaskawie.
21 Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
I poszedł przed nim ten dar, a sam przenocował tej nocy ze [swoim] obozem.
22 Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
Wstał tej nocy, wziął obie swe żony i dwie swoje służebnice oraz jedenastu swoich synów i przeszedł przez bród Jabboku.
23 Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
I wziął ich, przeprawił przez tę rzekę i przeprowadził [wszystko], co miał.
24 Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
Jakub zaś został sam. I walczył z nim [pewien] mężczyzna aż do wzejścia zorzy.
25 Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
A widząc, że nie może go pokonać, dotknął go w staw biodrowy i wytrącił biodro Jakubowi ze stawu, gdy się z nim mocował.
26 Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
I powiedział: Puść mnie, bo już wzeszła zorza. Odpowiedział: Nie puszczę cię, aż mi pobłogosławisz.
27 Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
Wtedy mu powiedział: Jakie jest twoje imię? I odpowiedział: Jakub.
28 Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
I powiedział: Twoim imieniem nie będzie już Jakub, ale Izrael, bo mężnie zmagałeś się z Bogiem i z ludźmi i zwyciężyłeś.
29 Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
I Jakub spytał: Powiedz mi, proszę, twoje imię. A on odpowiedział: Czemu pytasz o moje imię? I tam mu błogosławił.
30 Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
Jakub nadał więc temu miejscu nazwę Penuel, [mówiąc]: Widziałem bowiem Boga twarzą w twarz, a moja dusza została zachowana.
31 Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
I kiedy minął [miejsce] Penuel, wzeszło słońce, a on utykał z powodu swojego biodra.
32 Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.
Dlatego do dziś synowie Izraela nie jadają ścięgna, które jest w stawie biodrowym, gdyż dotknął Jakuba w staw biodrowy, w ścięgno, które się skurczyło.

< Genesis 32 >