< Genesis 32 >

1 Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
یعقوب به سفر خود ادامه داد. در بین راه فرشتگان خدا بر او ظاهر شدند.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
یعقوب وقتی آنها را دید، گفت: «این است اردوی خدا.» پس آنجا را مَحَنایِم نامید.
3 Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
آنگاه یعقوب، قاصدانی با این پیام نزد برادر خود عیسو به ادوم، واقع در سرزمین سعیر فرستاد: «بنده‌ات یعقوب تا چندی قبل نزد دایی خود لابان سکونت داشتم.
4 Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
5 Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
اکنون گاوها، الاغها، گوسفندها، غلامان و کنیزان فراوانی به دست آورده‌ام. این قاصدان را فرستاده‌ام تا تو را از آمدنم آگاه سازند. ای سَروَرم، امیدوارم مورد لطف تو قرار بگیرم.»
6 Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
قاصدان پس از رساندن پیام، نزد یعقوب برگشته، به وی گفتند: «برادرت عیسو را دیدیم و او الان با چهارصد نفر به استقبال تو می‌آید!»
7 Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
یعقوب با شنیدن این خبر بی‌نهایت ترسان و مضطرب شد. او افراد خانوادهٔ خود را با گله‌ها و رمه‌ها و شترها به دو دسته تقسیم کرد
8 Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
تا اگر عیسو به یک دسته حمله کند، دستهٔ دیگر بگریزد.
9 Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
سپس یعقوب چنین دعا کرد: «ای خدای جدم ابراهیم و خدای پدرم اسحاق، ای خداوندی که به من گفتی به وطن خود نزد خویشاوندانم برگردم و قول دادی که مرا برکت دهی،
10 Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
من لیاقت این همه لطف و محبتی که به خادمت نموده‌ای ندارم. آن زمان که زادگاه خود را ترک کردم و از رود اردن گذشتم، چیزی جز یک چوبدستی همراه خود نداشتم، ولی اکنون مالک دو گروه هستم!
11 Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
خداوندا، التماس می‌کنم مرا از دست برادرم عیسو رهایی دهی، چون از او می‌ترسم. از این می‌ترسم که مبادا او این زنان و کودکان را هلاک کند.
12 Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
به یاد آور که تو قول داده‌ای که مرا برکت دهی و نسل مرا چون شنهای ساحل دریا بی‌شمار گردانی.»
13 Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
یعقوب شب را در آنجا به سر برد و از آنچه با خود داشت این هدایا را برای تقدیم به برادرش عیسو انتخاب کرد:
14 Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
دویست بز ماده، بیست بز نر، دویست میش، بیست قوچ،
15 ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
سی شتر شیرده با بچه‌هایشان، چهل گاو ماده، ده گاو نر، بیست الاغ ماده و ده الاغ نر.
16 Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
او آنها را دسته‌دسته جدا کرده، به خادمانش سپرد و گفت: «از هم فاصله بگیرید و جلوتر از من حرکت کنید.»
17 Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
به مردانی که دستهٔ اول را رهبری می‌کردند گفت که موقع برخورد با عیسو اگر عیسو از ایشان بپرسد: «کجا می‌روید؟ برای چه کسی کار می‌کنید؟ و این حیوانات مال کیست؟»
18 Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
باید بگویند: «اینها متعلق به بنده‌ات یعقوب می‌باشند و هدایایی است که برای سَروَر خود عیسو فرستاده است. خودش هم پشت سر ما می‌آید.»
19 Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
یعقوب همین دستورها را به افراد دستۀ دوم و سوم و به همۀ کسانی که بدنبال گله‌ها می‌آمدند داده، گفت: «وقتی به عیسو رسیدید، همین سخنان را به او بگویید.
20 Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
و نیز بگویید:”بنده‌ات یعقوب نیز پشت سر ما می‌آید.“» یعقوب با خود فکر کرد: «با این هدایایی که جلوتر از خودم می‌فرستم او را نرم خواهم کرد. پس از آن وقتی او را ببینم شاید مرا بپذیرد.»
21 Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
پس او هدایا را جلوتر فرستاد اما خودش شب را در اردوگاه به سر برد.
22 Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
شبانگاه یعقوب برخاست و دو همسر و کنیزان و یازده پسر و تمام اموال خود را برداشته، به کنار رود اردن آمد و آنها را از گذرگاه یبوق به آن طرف رود فرستاد و خود در همان جا تنها ماند. سپس مردی به سراغ او آمده، تا سپیدهٔ صبح با او کشتی گرفت.
23 Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
24 Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
25 Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
وقتی آن مرد دید که نمی‌تواند بر یعقوب غالب شود، مفصل لگن ران او را محکم گرفت، به طوری که لگن او از جا در رفت.
26 Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
سپس آن مرد گفت: «بگذار بروم، چون سپیده دمیده است.» اما یعقوب گفت: «تا مرا برکت ندهی نمی‌گذارم از اینجا بروی.»
27 Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
آن مرد پرسید: «نام تو چیست؟» جواب داد: «یعقوب.»
28 Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
به او گفت: «پس از این نام تو دیگر یعقوب نخواهد بود، بلکه اسرائیل، زیرا نزد خدا و مردم مقاوم بوده و پیروز شده‌ای.»
29 Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
یعقوب از او پرسید: «نام تو چیست؟» آن مرد گفت: «چرا نام مرا می‌پرسی؟» آنگاه یعقوب را در آنجا برکت داد.
30 Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
یعقوب گفت: «در اینجا من خدا را رو به رو دیدم و با وجود این هنوز زنده هستم.» پس آن مکان را فنی‌ئیل (یعنی «چهرهٔ خدا») نامید.
31 Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
یعقوب هنگام طلوع آفتاب به راه افتاد. او به خاطر صدمه‌ای که به رانش وارد شده بود، می‌لنگید.
32 Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.
(بنی‌اسرائیل تا به امروز ماهیچهٔ عِرق النِساء را که در ران است نمی‌خورند، زیرا این قسمت از رانِ یعقوب بود که در آن شب صدمه دید.)

< Genesis 32 >