< Genesis 32 >

1 Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
UJakobe wasehamba indlela yakhe, lengilosi zikaNkulunkulu zamhlangabeza.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
UJakobe ezibona wasesithi: Leli libutho likaNkulunkulu. Wayitha ibizo laleyondawo iMahanayimi.
3 Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
UJakobe wasethuma izithunywa phambi kwakhe kuEsawu umnewabo, elizweni iSeyiri, ilizwe lakoEdoma.
4 Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
Wasezilaya esithi: Likhulume kanje enkosini yami uEsawu lithi: Itsho njalo inceku yakho uJakobe ithi: KoLabani bengihlala njengowezizwe ngalibala kuze kube khathesi;
5 Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
njalo ngilezinkabi labobabhemi, izimvu lezinceku lezincekukazi; sengithumele ukubika enkosini yami ukuthi ngithole umusa emehlweni akho.
6 Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
Izithunywa zasezibuyela kuJakobe zathi: Sifikile kumnewenu, kuEsawu, laye uyeza ukukuhlangabeza lamadoda angamakhulu amane laye.
7 Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
UJakobe wasesesaba kakhulu, wakhathazeka. Wehlukanisa abantu ababelaye lezimvu lezinkomo lamakamela, kwaba ngamaqembu amabili;
8 Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
ngoba wathi: Uba uEsawu efika kwelinye iqembu alitshaye, iqembu eliseleyo lizaphepha.
9 Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
UJakobe wathi futhi: Nkulunkulu kababa uAbrahama, loNkulunkulu kababa uIsaka, Nkosi owathi kimi: Buyela elizweni lakini lezihlotsheni zakho, njalo ngizakwenzela okuhle;
10 Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
kangiwufanele wonke umusa lakho konke ukuthembeka okwenzele inceku yakho; ngoba ngilodondolo lwami ngachapha le iJordani, khathesi-ke sengingamaqembu amabili.
11 Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
Ake ungophule esandleni somnewethu, esandleni sikaEsawu; ngoba ngiyamesaba, hlezi afike angitshaye, unina phezu kwabantwana.
12 Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
Wena-ke wathi: Ukwenza okuhle ngizakwenzela okuhle, njalo ngizayenza inzalo yakho ibe njengetshebetshebe lolwandle elingelakubalwa ngenxa yobunengi.
13 Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
Waselala lapho ngalobobusuku; wathatha kulokho okwafika esandleni sakhe, isipho sikaEsawu umfowabo,
14 Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
izibhuzikazi ezingamakhulu amabili lempongo ezingamatshumi amabili, izimvukazi ezingamakhulu amabili lenqama ezingamatshumi amabili,
15 ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
amakamela enyisayo angamatshumi amathathu lamathole awo, amankomokazi angamatshumi amane, lamajongosi alitshumi, obabhemikazi abangamatshumi amabili lamathole abobabhemi alitshumi.
16 Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
Wasezinikela esandleni senceku zakhe umhlambi ngomhlambi wodwa, wathi ezincekwini zakhe: Dlulani phambi kwami, libeke ibanga phakathi komhlambi lomhlambi.
17 Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
Waselaya eyokuqala esithi: Nxa uEsawu umnewethu ehlangana lawe, ekubuza esithi: Ungokabani? Njalo uya ngaphi? Ngezikabani-ke lezi eziphambi kwakho?
18 Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
Ubususithi: Ngezenceku yakho ngezikaJakobe, yisipho esithunyelwa enkosini yami uEsawu; khangela-ke, laye uqobo ungemva kwethu.
19 Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
Waselaya leyesibili leyesithathu labo bonke ababelandela imihlambi esithi: Njengalelilizwi lizakhuluma kuEsawu, lapho limthola;
20 Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
lithi futhi: Khangela, inceku yakho uJakobe ingemva kwethu. Ngoba uthe: Ngizathoba ubuso bakhe ngesipho esihamba phambi kwami, langemva kwalokho ngizabona ubuso bakhe; mhlawumbe uzakwemukela ubuso bami.
21 Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
Lesipho sahamba phambi kwakhe; kodwa yena walala lobobusuku enkambeni.
22 Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
Wasesukuma ngalobobusuku, wathatha omkakhe bobabili lencekukazi ezimbili labantwana bakhe abalitshumi lanye, wachapha izibuko leJaboki.
23 Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
Wabathatha, wabachaphisa isifudlana, wachaphisa lokho ayelakho.
24 Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
UJakobe watshiywa yedwa; njalo indoda yabindana laye kwaze kwaba semadabukakusa.
25 Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
Kodwa isibonile ukuthi kayimehluli, yathinta isikhoxo senyonga yakhe, isikhoxo senyonga kaJakobe saqhuzuka ebindana layo.
26 Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
Yasisithi: Ngiyekela ngihambe ngoba sekusemadabukakusa. Kodwa wathi: Kangiyikukuyekela uhambe ngaphandle kokuthi ungibusise.
27 Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
Yasisithi kuye: Ungubani ibizo lakho? Wasesithi: UJakobe.
28 Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
Yasisithi: Ibizo lakho kalisayikuthiwa nguJakobe, kodwa uIsrayeli, ngoba ulwile loNkulunkulu labantu, wanqoba.
29 Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
UJakobe wasebuza wathi: Ake utsho ibizo lakho. Yasisithi: Kungani ubuza ibizo lami? Yambusisa lapho.
30 Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
UJakobe waseyitha ibizo lendawo iPeniyeli, ngoba ngibonile uNkulunkulu ubuso ngobuso, njalo impilo yami isindisiwe.
31 Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
Njalo ilanga lamphumela esedlula iPenuyeli; wayeqhula enyongeni yakhe.
32 Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.
Ngakho abantwana bakoIsrayeli kabawudli umsipha womthambo osesikhoxweni senyonga kuze kube lamuhla, ngoba wathinta isikhoxo senyonga kaJakobe esisemsipheni womthambo wenyonga.

< Genesis 32 >