< Genesis 32 >
1 Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
Jacob poursuivit son chemin, et les anges de Dieu vinrent à sa rencontre.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
Quand il les vit, Jacob dit: « C'est l'armée de Dieu. » Il donna à ce lieu le nom de Mahanaïm.
3 Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
Jacob envoya devant lui des messagers à Ésaü, son frère, au pays de Séir, dans le champ d'Édom.
4 Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
Il leur donna cet ordre: « Voici ce que vous direz à mon seigneur Ésaü: « Voici ce que dit ton serviteur Jacob. J'ai vécu comme un étranger chez Laban, et j'y suis resté jusqu'à présent.
5 Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
J'ai du bétail, des ânes, des troupeaux, des serviteurs et des servantes. J'ai envoyé le dire à mon seigneur, afin que je trouve grâce à tes yeux. »
6 Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
Les messagers retournèrent auprès de Jacob, en disant: « Nous sommes allés voir ton frère Ésaü. Il vient à ta rencontre, et quatre cents hommes sont avec lui. »
7 Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
Alors Jacob eut une grande crainte et fut bouleversé. Il divisa en deux groupes les gens qui étaient avec lui, ainsi que les troupeaux, les bœufs et les chameaux.
8 Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
Il dit: « Si Ésaü vient vers la première troupe et la frappe, la troupe qui reste échappera. »
9 Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
Jacob dit: « Dieu de mon père Abraham et Dieu de mon père Isaac, Yahvé, qui m'a dit: Retourne dans ton pays et dans ta famille, et je te ferai du bien,
10 Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
je ne suis pas digne de la moindre de toutes les bontés et de toute la vérité que tu as montrées à ton serviteur, car c'est avec mon seul bâton que j'ai traversé ce Jourdain, et maintenant je suis devenu deux compagnies.
11 Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
Délivre-moi de la main de mon frère, de la main d'Ésaü, car je le crains, de peur qu'il ne vienne me frapper, moi et les mères avec les enfants.
12 Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
Tu as dit: « Je te ferai du bien, et je rendrai ta postérité comme le sable de la mer, qu'on ne peut compter, tant il est nombreux. »
13 Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
Il resta là cette nuit-là, et prit dans ce qu'il avait avec lui un présent pour Ésaü, son frère:
14 Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
deux cents chèvres et vingt boucs, deux cents brebis et vingt béliers,
15 ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
trente chameaux de lait et leurs ânes, quarante vaches, dix taureaux, vingt ânesses et dix poulains.
16 Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
Il les remit entre les mains de ses serviteurs, chaque troupeau séparément, et dit à ses serviteurs: « Passez devant moi, et mettez un espace entre chaque troupeau. »
17 Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
Il donna cet ordre aux premiers: « Quand Ésaü, mon frère, viendra à ta rencontre et t'interrogera en disant: « De qui es-tu? Où vas-tu? A qui sont ces choses devant toi?
18 Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
Tu répondras: « Elles sont à ton serviteur, Jacob. C'est un présent envoyé à mon seigneur Ésaü. Voici qu'il est aussi derrière nous ».
19 Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
Il donna aussi des ordres au second, au troisième et à tous ceux qui suivaient les troupeaux, en disant: « Voici comment vous parlerez à Ésaü, lorsque vous le trouverez.
20 Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
Vous direz: « Non seulement cela, mais voici que ton serviteur Jacob est derrière nous ». Car, dit-il, « je l'apaiserai avec le présent qui me précède, et après, je verrai son visage. Peut-être m'acceptera-t-il. »
21 Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
Et le présent passa devant lui, et il resta lui-même cette nuit-là dans le camp.
22 Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
Il se leva cette nuit-là, prit ses deux femmes, ses deux serviteurs et ses onze fils, et traversa le gué du Jabbok.
23 Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
Il les prit, leur fit traverser le torrent, et leur fit passer ce qui lui appartenait.
24 Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
Jacob resta seul, et il lutta là avec un homme jusqu'au point du jour.
25 Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
Comme il voyait qu'il ne l'emportait pas sur lui, l'homme toucha le creux de sa cuisse, et le creux de la cuisse de Jacob était tendu pendant qu'il luttait.
26 Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
L'homme dit: « Laisse-moi partir, car le jour se lève. » Jacob a dit: « Je ne te laisserai pas partir si tu ne me bénis pas. »
27 Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
Il lui dit: « Quel est ton nom? » Il a dit, « Jacob ».
28 Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
Il dit: « Ton nom ne sera plus Jacob, mais Israël; car tu as combattu avec Dieu et avec les hommes, et tu as vaincu. »
29 Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
Jacob lui demanda: « Dis-moi ton nom, s'il te plaît. » Il a dit: « Pourquoi demandez-vous mon nom? » Alors il l'a béni là.
30 Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
Jacob donna à ce lieu le nom de Peniel, car il dit: « J'ai vu Dieu face à face, et ma vie est sauve. »
31 Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
Le soleil se leva sur lui lorsqu'il passa à Peniel, et il boitait à cause de sa cuisse.
32 Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.
C'est pourquoi les enfants d'Israël ne mangent pas le tendon de la hanche, qui se trouve au creux de la cuisse, jusqu'à ce jour, car il a touché le creux de la cuisse de Jacob dans le tendon de la hanche.