< Genesis 32 >

1 Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
But Iacob went forth on his iourney. And the angells of God came and mett him.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
And when Iacob sawe them he sayde: this is godes hoost: and called the name of that same place Mahanaim.
3 Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
Iacob sente meessengers before him to Esau his brother vnto the lande of Seir and the felde of Edom.
4 Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
And he comaunded them saynge: se that ye speake after this maner to my lorde Esau: thy seruaunte Iacob sayth thus. I haue sogerned ad bene a straunger with Laban vnto this tyme:
5 Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
and haue gotten oxen asses and shepe menservauntes and wemanseruauntes and haue sent to shewe it mi lorde that I may fynde grace in thy syghte.
6 Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
And the messengers came agayne to Iacob sainge: we came vnto thi brother Esau and he cometh ageynst the and. iiij. hundred men with hi.
7 Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
Than was Iacob greatlye afrayde and wist not which waye to turne him selfe and devyded the people that was with him and the shepe oxen and camels in to. ij. companies
8 Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
and sayde: Yf Esau come to the one parte and smyte it the other may saue it selfe.
9 Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
And Iacob sayde: O god of my father Abraham and God of my father Isaac: LORde which saydest vnto me returne vnto thy cuntre and to thy kynrede and I will deall wel with the.
10 Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
I am not worthy of the leaste of all the mercyes and treuth which thou hast shewed vnto thy seruaunte. For with my staf came I over this Iordane and now haue Igoten. ij. droves
11 Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
Delyver me from the handes of my brother Esau for I feare him: lest he will come and smyte the mother with the childeru.
12 Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
Thou saydest that thou woldest surely do me good and woldest make mi seed as the sonde of the see which can not be nombred for multitude.
13 Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
And he taried there that same nyghte and toke of that which came to hande a preasent vnto Esau his brother:
14 Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
ij hundred she gootes ad xx he gootes: ij hundred shepe and xx rammes:
15 ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
thyrtye mylch camels with their coltes: xl kyne ad x bulles: xx she asses ad foles
16 Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
and delyuered them vnto his seruauntes euery drooue by them selues ad sayde vnto them: goo forth before me and put a space betwyxte euery drooue.
17 Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
And he comaunded the formest sayngeWhe Esau my brother meteth the ad axeth the saynge: whose seruaute art thou and whither goost thou and whose ar these that goo before ye:
18 Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
thou shalt say they be thy seruaunte Iacobs and are a present sent vnto my lorde Esau and beholde he him selfe cometh after vs.
19 Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
And so comaunded he the seconde ad euen so the thirde and lykewyse all that folowed the drooues sainge of this maner se that ye speake vnto Esau whe ye mete him
20 Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
ad saye more ouer. Beholde thy seruaunte Iacob cometh after vs for he sayde. I will pease his wrath with the present yt goth before me and afterward I will see him myself so peradventure he will receaue me to grace.
21 Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
So went the preset before him ad he taried all that nyghte in the tente
22 Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
ad rose vp the same nyghte ad toke his. ij. wyves and his. ij. maydens and his. xi. sonnes and went ouer the foorde Iabok.
23 Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
And he toke them ad sent the ouer the ryuer ad sent ouer that he had
24 Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
ad taried behinde him selfe alone. And there wrastled a man with him vnto the breakynge of the daye.
25 Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
And when he sawe that he coude not prevayle agaynst him he smote hi vnder the thye and the senowe of Iacobs thy shranke as he wrastled with him.
26 Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
And he sayde: let me goo for the daye breaketh. And he sayde: I will not lett the goo excepte thou blesse me.
27 Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
And he sayde vnto him: what is thy name? He answered: Iacob.
28 Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
And he sayde: thou shalt be called Iacob nomore but Israell. For thou hast wrastled with God and with men ad hast preuayled.
29 Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
And Iacob asked him sainge tell me thi name. And he sayde wherfore dost thou aske after my name? and he blessed him there.
30 Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
And Iacob called the name of the place Peniel for I haue sene God face to face and yet is my lyfe reserved.
31 Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
And as he went ouer Peniel the sonne rose vpon him and he halted vpon his thye:
32 Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.
wherfore the childern of Israell eate not of the senow that shrancke vnder the thye vnto this daye: because that he smote Iacob vnder the thye in the senow that shroncke.

< Genesis 32 >