< Genesis 32 >

1 Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
As Jacob and his family continued traveling, some angels, whom God sent, met him.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
When Jacob saw them, he said, “This is God’s army camp!” So he named that place Mahanaim, [which means ‘two camps’].
3 Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
Jacob told some of the men to go ahead of him to his older brother Esau, who was living in Seir, the land where the descendants of Edom lived.
4 Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
He told them, “This is what I want you to say to Esau: 'I, Jacob, want to be your servant and I want you to be my master. I have been living with our uncle Laban, and I have stayed there until now.
5 Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
I now own many cattle, donkeys, sheep, goats, and male and female slaves. Now I am sending this message to you, sir, hoping that you will (be friendly toward me/treat me kindly) when I arrive.’ “
6 Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
The messengers went and gave that message to Esau. When they returned to Jacob, they said, “We went to your older brother Esau. Now he is coming to you, and 400 men are coming with him.”
7 Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
Jacob was very afraid and worried. So he divided the people who were with him into two groups. He also divided the sheep and goats, the cattle, and the camels, into two groups.
8 Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
He was thinking, “If Esau and his men come and attack us, perhaps one of the groups will be left and will be able to escape.”
9 Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
Then Jacob prayed, “O Yahweh God, whom my grandfather Abraham worshiped and my father Isaac worships, you said to me, ‘Go back to your own land and to your relatives, and I will (cause good things happen to/do good things for) you.’
10 Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
I am not worthy for you to have been so kind and faithful to me in so many ways, your servant. I had only this walking stick with me when I crossed the Jordan [River on my way to Haran], but now I am so wealthy that there are two large groups of my family and possessions.
11 Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
So now I pray that you will rescue me from [MTY] my [older] brother Esau, because I am afraid that he and his men will come and attack and kill me and the children and their mothers.
12 Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
But do not forget that you have said, ‘I will certainly enable you to prosper, and I will cause your descendants to be as numerous as the grains of sand on the seashore, which are so many that no one can count them.’”
13 Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
Jacob slept there that night. The next morning he selected some animals to give to his brother Esau.
14 Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
He selected 200 female goats and 20 male goats, 200 female sheep and 20 male sheep,
15 ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
30 female camels and their offspring, 40 cows and ten bulls, 20 female donkeys and 10 male donkeys.
16 Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
He divided them into small herds, and put each herd into the care of one of his servants. He said to his servants, “Go ahead of me, one group at a time, and keep some space between each herd.”
17 Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
He said to the servant who was going with the first group, “When my brother Esau meets you, and he asks you, ‘To whom do you belong, and where are you going, and to whom do these animals in front of you belong?’
18 Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
tell him, ‘They belong to your servant Jacob. He has sent them to you as a gift, sir. And he is coming behind us.’”
19 Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
He also said the same thing to the servants who were taking care of the second and third groups, and to the other herdsmen. He said to them, “When you meet Esau, I want you to say to him the same thing that I told the first servant.
20 Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
And be sure to say ‘Jacob, who wants to serve you, is coming behind us.’” Jacob told them to say that because he was thinking, “Perhaps these gifts that I am sending ahead of me will cause him to (act peacefully toward/stop being angry with) me. Then later, when I see him, perhaps he will be kind to me.”
21 Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
So the men taking the gifts [PRS] went ahead, but Jacob himself stayed in the camp that night.
22 Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
Some time during that night, Jacob got up and took his two wives, his two female slaves, and his eleven sons and his daughter, and he sent them across the ford at the Jabbok River.
23 Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
After he had done that, he sent other slaves, carrying all his possessions, across the river.
24 Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
So Jacob was left there alone. But a man came and wrestled with him until dawn.
25 Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
When the man realized that he was not winning against Jacob, he struck Jacob’s hip and caused the thigh bone to pull away from the hip socket.
26 Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
Then the man said, “Let me go, because it will soon be daylight.” [Then Jacob realized who he was really wrestling with]. So he replied, “No, if you will not bless me, I will not let you go!”
27 Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
The man said to him, “What is your name?” He replied, “Jacob.”
28 Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
The man said, “Your name will no longer be Jacob. Your name will be Israel, [which means ‘he struggles with God’, ] because you have struggled with God and with people, and you have won.”
29 Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
Jacob said, “Now, please tell me your name!” The man replied, “(Why do you ask me what my name is?/You should not have to ask me what my name is!)” [RHQ] But he blessed Jacob there.
30 Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
So Jacob named the place Peniel, [which means ‘God’s face’, ] saying “I looked directly at God, but I did not die because of doing that.”
31 Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
The sun was rising as Jacob left Peniel, and he was limping because of what had happened to his hip.
32 Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.
The muscle on his hip joint had been injured. So to this present time, because of what happened to Jacob, the Israeli people do not eat the muscle/tendon that is attached to the socket of the hips of animals.

< Genesis 32 >