< Genesis 32 >

1 Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
Likewise, Jacob continued on the journey that he had begun. And the Angels of God met him.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
When he had seen them, he said, “These are the Encampments of God.” And he called the name of that place Mahanaim, that is, ‘Encampments.’
3 Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
Then he also sent messengers before him to his brother Esau, in the land of Seir, in the region of Edom.
4 Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
And he instructed them, saying: “You shall speak in this way to my lord Esau: ‘Your brother Jacob says these things: “I have sojourned with Laban, and I have been with him until the present day.
5 Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
I have oxen, and donkeys, and sheep, and men servants, and women servants. And now I send an ambassador to my lord, so that I may find favor in your sight.”’”
6 Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
And the messengers returned to Jacob, saying, “We went to your brother Esau, and behold, he rushes to meet you with four hundred men.”
7 Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
Jacob was very afraid. And in his terror, he divided the people who were with him, likewise the flocks, and the sheep, and the oxen, and the camels, into two companies,
8 Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
saying: “If Esau goes to one company, and strikes it, the other company, which is left behind, will be saved.”
9 Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
And Jacob said: “God of my father Abraham, and God of my father Isaac, O Lord who said to me: ‘Return to your land, and to the place of your nativity, and I will do well for you.’
10 Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
I am less than any of your compassions and your truth, which you have fulfilled to your servant. With my staff I crossed over this Jordan. And now I go back with two companies.
11 Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
Rescue me from the hand of my brother Esau, for I am very afraid of him, lest perhaps he may come and strike down the mother with the sons.
12 Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
You did say that you would do well by me, and that you would expand my offspring like the sand of the sea, which, because of its multitude, cannot be numbered.”
13 Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
And when he had slept there that night, he separated, from the things that he had, gifts for his brother Esau:
14 Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
two hundred she-goats, twenty he-goats, two hundred ewes, and twenty rams,
15 ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
thirty milking camels with their young, forty cows, and twenty bulls, twenty she-donkeys, and ten of their young.
16 Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
And he sent them by the hands of his servants, each flock separately, and he said to his servants: “Pass before me, and let there be a space between flock and flock.”
17 Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
And he instructed the first, saying: “If you happen to meet my brother Esau, and he questions you: “Whose are you?” or, “Where are you going?” or, “Whose are these which follow you?”
18 Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
you shall respond: “Your servant Jacob’s. He has sent them as a gift to my lord Esau. And he is also coming after us.”
19 Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
Similarly, he gave orders to the second, and the third, and to all who followed the flocks, saying: “Speak these same words to Esau, when you find him.
20 Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
And you will add: ‘Your servant Jacob himself also follows after us, for he said: “I will appease him with the gifts that go ahead, and after this, I will see him; perhaps he will be gracious to me.”’”
21 Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
And so the gifts went before him, but he himself lodged that night in the camp.
22 Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
And when he had arisen early, he took his two wives, and the same number of handmaids, with his eleven sons, and he crossed over the ford of Jabbok.
23 Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
And having delivered over all the things that belonged to him,
24 Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
he remained alone. And behold, a man wrestled with him until morning.
25 Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
And when he saw that he would not be able to overcome him, he touched the nerve of his thigh, and immediately it withered.
26 Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
And he said to him, “Release me, for now the dawn ascends.” He responded, “I will not release you, unless you bless me.”
27 Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
Therefore he said, “What is your name?” He answered, “Jacob.”
28 Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
But he said, “Your name will not be called Jacob, but Israel; for if you have been strong against God, how much more will you prevail against men?”
29 Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
Jacob questioned him, “Tell me, by what name are you called?” He responded, “Why do you ask my name?” And he blessed him in the same place.
30 Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
And Jacob called the name of the place Peniel, saying, “I have seen God face to face, and my soul has been saved.”
31 Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
And immediately the sun rose upon him, after he had crossed beyond Peniel. Yet in truth, he limped on his foot.
32 Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.
For this reason, the sons of Israel, even to the present day, do not eat the nerve that withered in Jacob’s thigh, because he touched the nerve of his thigh and it was obstructed.

< Genesis 32 >