< Genesis 31 >
1 Yakobo anamva zimene ana aamuna a Labani ankanena kuti, “Yakobo watenga chilichonse cha abambo athu ndipo wapeza chuma chonsechi pogwiritsa ntchito chuma cha abambo athu.”
Then heard he the words of the sons of Laban, saying, Jacob hath taken away all that belonged to our father; Yea out of what belonged to our father, hath he made all this wealth.
2 Choncho Yakobo anaona kuti Labani sankamuonetsanso nkhope yabwino monga kale.
And Jacob looked upon the face of Laban, —and lo! it was not with him as afore-time.
3 Pamenepo Yehova anati kwa Yakobo, “Bwerera ku dziko la makolo ako ndi kwa abale ako, ndipo Ine ndidzakhala nawe.”
Then said Yahweh unto Jacob, Return unto the land of thy fathers and to thy kindred, —that I may be with thee.
4 Choncho Yakobo anatumiza mawu kukayitana Rakele ndi Leya kuti abwere ku busa kumene ankaweta ziweto zake.
So Jacob sent, and called for Rachel and for Leah, to the field unto his flock;
5 Iye anawawuza kuti, “Abambo anu sakundionetsanso nkhope yabwino monga kale, koma Mulungu wa makolo anga wakhala ali nane.
and said to them, Beholding, am I the face of your father, that it is not towards me as aforetime, —nevertheless, the God of my father, hath been with me;
6 Inu mukudziwa kuti ndagwirira ntchito abambo anu ndi mphamvu zanga zonse,
and, ye, know that with all my vigour, have I served your father.
7 chonsecho abambo anu akhala akundinyenga posintha malipiro anga kakhumi konse. Komabe Mulungu sanalole kuti andichitire choyipa
But, your father, hath deceived me, and hath changed my wages ten times, —yet God hath not suffered him to deal harmfully with me.
8 Pamene abambo anu anati, ‘Zamawangamawanga zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana amawangamawanga; ndipo pamene anati, ‘Zamichocholozi zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana a michocholozi.
If thus he saith, The speckled, shall be thy wages, then do all the flock bring forth speckled, —But if thus he saith, The ring-straked, shall be thy wages, then do all the flock bring forth ring-straked.
9 Motero Mulungu walanda abambo anu ziweto zawo ndi kundipatsa.
So hath God stripped away the herds of your father, and given them to me.
10 “Pa nthawi imene ziweto zimatenga mawere ndinalota maloto, ndipo ndinaona kuti atonde onse amene ankakwerawo anali amichocholozi, amawangamawanga kapena amathothomathotho
And it came to pass in the season when the flock were in heat, then lifted I mine eyes and beheld in a dream, —and lo! the he-goats that were leaping upon the flock, were ring-straked speckled and dappled.
11 Kutulo komweko, mngelo wa Mulungu anati, ‘Yakobo.’ Ine ndinayankha, ‘Ee, Ambuye.’
And the messenger of God said unto me in a dream, Jacob! and I said, Behold me!
12 Ndipo iye anati, ‘Tayangʼana ndipo taona kuti atonde onse okwerana ndi ziweto ali amichocholozi, amawangamawanga kapena a mathothomathotho, popeza ndaona zonse zimene Labani wakhala akukuchitira.
Then he said Lift, I pray thee, thine eyes and behold All, the he-goats that are leaping upon the flock are ring-straked, speckled, and dappled, —for I have seen all that Laban, has been doing to thee.
13 Ine ndine Mulungu amene ndinadza kwa iwe pa Beteli paja. Beteli ndi kumalo kuja kumene unayimika mwala ndi kuwudzoza mafuta, komanso kulumbira kwa Ine. Tsopano choka mʼdziko lino msanga ndi kubwerera ku dziko la kwanu.’”
I, am the GOD of Beth-el, where thou didst anoint a pillar, where thou didst vow to me a vow, —Now, rise, go forth out of this land, and return unto the land of thy kindred.
14 Pamenepo Rakele ndi Leya anayankha, “Kodi ngati ife tilinso ndi gawo ngati cholowa pa chuma cha abambo athu?
Then responded Rachel and Leah, and said to him, —Have we any longer a portion or an inheritance in the house of our father?
15 Kodi abambo athu samationa ife ngati alendo? Iwo anatigulitsa ndi kuwononga ndalama zonse anazipeza pa ifezo.
Are we not accounted, aliens, to him seeing that having sold us, he hath then gone on devouring, our silver?
16 Chuma chonse chimene Mulungu walanda abambo athu, ndi chathu ndi ana athu. Tsono inu chitani zimene Mulungu wakuwuzani.”
Surely all the riches which God hath stripped off from our father, unto us, it belongeth, and unto our sons, —Now, therefore, whatsoever God hath said unto thee, do.
17 Pamenepo Yakobo anakonzeka nakweza ana ake ndi akazi ake pa ngamira,
So Jacob arose, —and mounted his sons and his wives on the camels;
18 anakusa ziweto zake zonse patsogolo natenga katundu wake yense amene anamupeza ku Padanaramu, ndipo ananyamuka kupita ku Kanaani, ku dziko la abambo ake, Isake.
and drave away all his herds and all his goods which he had gathered, the gains he had gained, which he had gathered in Padan-aram; that he might go in unto Isaac his father unto the land of Canaan.
19 Labani atachoka pa khomo kupita kukameta nkhosa, mʼmbuyomu Rakele anaba timafano ta milungu ta abambo ake.
Now, Laban, had gone, to shear his sheep, —so Rachel stole the household gods that belonged to her father,
20 Komanso nthawi iyi nʼkuti Yakobo atamunamiza Labani Mwaramu posamuwuza zoona kuti afuna kuthawa.
Thus Jacob stole away unawares to Laban, the Syrian, —in that he had not told him that he was about to flee.
21 Choncho anathawa ndi zonse anali nazo. Ananyamuka nawoloka mtsinje wa Yufurate kupita cha ku Giliyadi, dziko la mapiri.
So he fled, he—and all that he had, and he arose, and passed over the River, —and set his face towards the mountain of Gilead.
22 Patapita masiku atatu, Labani anawuzidwa kuti Yakobo wathawa.
And it was told Laban, on the third day, —that Jacob had fled.
23 Pomwepo anatengana ndi abale ake namulondola Yakobo kwa masiku asanu ndi awiri ndipo anakamupezera ku Giliyadi, dziko la mapiri.
So he took his brethren with him, and pursued after him a journey of seven days—and overtook him in the mountain of Gilead.
24 Koma Mulungu anabwera kwa Labani, Mwaramu kutulo usiku nati kwa iye, “Samala kuti usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.”
And God went in unto Laban the Syrian in a dream of the night, —and said to him Take heed to thyself that thou speak not with Jacob either good or bad.
25 Pamene Labani amamupeza Yakobo, nʼkuti Yakobo atamanga matenti ake ku mapiri a dziko la Giliyadi. Nayenso Labani ndi abale ake anamanga matenti awo komweko.
So then Laban came up with Jacob, —Jacob, having pitched his tent in the mountain, Laban, also, with his brethren pitched in the mountain of Gilead.
26 Tsono Labani anati kwa Yakobo, “Kodi ndakuchita chiyani kuti iwe undinamize ndi kutenga ana anga ngati anthu ogwidwa ku nkhondo?
Then said Laban to Jacob, What hadst thou done, that thou shouldst steal away unawares to me, —and shouldst carry off my daughters, as captives of the sword?
27 Chifukwa chiyani unandinamiza ndi kuthawa mozemba wosandiwuza? Ukanandiwuza, bwezi titatsanzikana mwa chisangalalo ndi kuyimba nyimbo ndi zisekese ndi azeze.
Wherefore didst thou secretly flee, and rob me, —and didst not tell me, that I might send thee away with rejoicing and with songs, with timbrel and with lyre;
28 Sunandilole kuti ndingopsompsona adzukulu anga ndi ana anga aakazi motsanzikana nawo. Unachita zopusa.
and didst not suffer me to kiss my sons and my daughters? Now, hast thou done, foolishly.
29 Ndili nayo mphamvu yakukuchita choyipa; koma usiku wapitawu, Mulungu wa abambo ako wandiwuza ine kuti, ‘Usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.’
It is in the power of my hand, to deal with thee for harm, —but the God of your father, last night, spake unto me, saying, Take heed to thyself that thou speak not with Jacob, either good or bad.
30 Ndikudziwa kuti unachoka chifukwa unapukwa kufuna kubwerera kwanu kwa abambo ako. Koma nʼchifukwa chiyani unaba milungu yanga?”
But, now, though thou, didst even take thy journey, because thou, didst sorely long, for the house of thy father, wherefore didst thou steal away my gods?
31 Yakobo anayankha Labani kuti, “Ine ndinkaopa chifukwa ndinkaganiza kuti mukhoza kundilanda anawa.
And Jacob answered and said unto Laban, —Because I was afraid, for I said, Lest thou take by force thy daughters from me!
32 Koma mukapeza wina aliyense ndi milungu yanu, ameneyo sakhala ndi moyo. Anthu onse akupenya, lozani chilichonse chanu chimene chili ndi ine, ndipo ngati muchipeze tengani. Koma Yakobo sankadziwa kuti Rakele anabadi milunguyo.”
He with whom thou find thy gods, shall not live! Before our brethren, note thou for thyself what is with me and take what is thine. Neither did Jacob know that, Rachel, had stolen them.
33 Choncho Labani analowadi mu tenti ya Yakobo, ya Leya ndi mʼmatenti a adzakazi awiri aja, koma sanapeze kalikonse. Atatuluka mu tenti ya Leya, analowa ya Rakele.
Then entered Laban into the tent of Jacob and into the tent of Leah and into the tent of the two handmaids, and found nothing, —then went he forth out of the tent of Leah, and entered into the tent of Rachel.
34 Koma Rakele anatengadi milungu ija ndi kuyiika mʼkati mwa chokhalira cha pa ngamira, iye nʼkukhalapo. Choncho Labani anafunafuna mu tenti monse koma wosapeza kanthu.
Now Rachel, had taken the household gods and put them in the basket-saddle of the camel, and taken her seat upon them. And Laban felt about throughout all the tent, and found them not.
35 Rakele anati kwa abambo ake, “Pepanitu musandikwiyire mbuye wanga chifukwa choti sinditha kuyimirira pamaso panu chifukwa ndili kumwezi.” Choncho Labani anafunafuna koma sanayipeze milungu ija.
And she said unto her father, Let it not be vexing in the eyes of my lord that I cannot rise up at thy presence, for, the way of women, is upon me. So he made search, but found not the household gods,
36 Yakobo anapsa mtima nafunsa Labani mwaukali kuti, “Kodi ndalakwa chiyani? Ndi tchimo lanji limene ndachita kuti muchite kundisaka chonchi?
And it was vexing to Jacob and he contended with Laban, —and Jacob responded and said to Laban, What was my trespass, what my sin, that thou shouldst have come burning after me?
37 Chifukwa chiyani mwafunyulula katundu wanga? Ndipo mwapeza chiyani cha inu pamenepa? Chimene mwapezapo chiyikeni poyera pamaso pa abale anu ndi anga kuti atiweruze.
Now that thou hast felt about among all my goods, what hast thou found of the goods of thine own house? Set it out here, right before my brethren and thy brethren, —that they may give sentence betwixt us two.
38 “Ndakhala nanu kwa zaka makumi awiri tsopano ndipo nkhosa ndi mbuzi zanu sizinapoloze, kapena ine kudyapo nkhosa za mʼkhola mwanu.
This twenty years’ time, have, I, been with thee—Thy ewes and thy she-goats, have not cast their young, —And the rams of thy flock, have I not eaten,
39 Chiweto chikakhadzulidwa ndi chirombo, sindinkabwera nacho kwa inu. Ineyo ndinkalipira. Inuyo munkandilipiritsa kalikonse kobedwa masana kapena usiku.
The torn, have I not brought in unto thee—I bare the loss, At my hand, didst thou require it, —Stolen by day, or stolen by night.
40 Moyo wanga unali wotere: Dzuwa limanditentha masana ndipo usiku ndimazunzika ndi kuzizira. Tulo sindimalipeza konse.
Thus have I been—By day, drought hath consumed me, And, frost, by, night, —So that my sleep fled away from mine eyes.
41 Zinthu zinali chonchi kwa zaka makumi awiri zimene ndinali mʼnyumba mwanu. Ndinakugwirirani ntchito kwa zaka khumi ndi zinayi chifukwa cha ana anu aakazi awiri ndipo zaka zina zisanu ndi chimodzi chifukwa cha ziweto zanu, ndipo munandisinthira malipiro kakhumi konse.
This, hath been my lot twenty years in thy house, —I served thee fourteen years for thy two daughters, And six years for thy sheep—And thou didst change my wages ten times: —
42 Akanapanda kukhala nane Mulungu wa abambo anga, Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu amene Isake ankamuopa, mosakayika inu mukanandichotsa chimanjamanja. Koma Mulungu waona zovuta zanga ndi kulimbikira ntchito kwanga, ndipo usiku wapitawu anakudzudzulani.”
But that the God of my father—The God of Abraham, and the Dread of Isaac—Proved to be mine, Surely even now, empty, hadst thou let me go? My humiliation and the wearying toil of my hands, God had seen, And therefore gave sentence last night!
43 Labani anayankha Yakobo nati, “Ana aakaziwa ndi anga, ana awo ndi anganso. Ziwetozi ndi zanga. Chilichonse ukuona apa ndi changa. Koma tsopano ndingachite chiyani ndi ana anga aakaziwa kapena ndi ana awo?
Then responded Laban and said unto Jacob—the daughters, are my daughters, And the sons, are my sons, And the sheep are my sheep, And, all that, thou, beholdest, To me doth it belong! But to my daughters, what can I do to these this day, Or to their sons whom they have borne?
44 Tsono, tiye tichite pangano pakati pa iwe ndi ine, ndipo likhale mboni pakati pathu.”
Now, therefore, come on! Let us solemnise a covenant, I and thou, —So shall it be a witness betwixt me and thee.
45 Choncho Yakobo anayimiritsa mwala ngati chipilala.
So Jacob took a stone, —and set it up as a pillar.
46 Nati kwa abale ake, “Tutani miyala ina.” Choncho anawunjika miyalayo, ndipo anadya chakudya atakhala pa mbali pa muluwo.
Then said Jacob to his brethren—Gather stones. And they took stones and made a heap, —and they did eat there, by the heap.
47 Labani anawutcha muluwo Yegara-sahaduta, ndipo Yakobo anawutcha Galeeda.
And Laban called it, Jegar-sahadutha, —but, Jacob, called it, Galeed.
48 Labani anati, “Mulu uwu ndi mboni pakati pa inu ndi ine lero.” Ndi chifukwa chake unatchedwa Galeeda.
Then said Laban: This heap, be witness betwixt me, and thee, to-day. For this cause, is the name thereof called Galeed;
49 Unatchedwanso Mizipa, chifukwa iye anati, “Yehova aonetsetsa kuti palibe mmodzi mwa ife adzaswe panganoli ngakhale titatalikirana.
also, The Watch Tower, as to which it is said, Yahweh watch betwixt me and thee, when we are parted one from another.
50 Ngati ukazunza ana anga kapena kukwatira akazi enanso, ngakhale kuti palibe wina amene ali nafe pano, koma kumbukira kuti Mulungu ndiye mboni pakati pathu.”
If thou oppress my daughters, or if thou take wives besides my daughters, —there may be no man with us—see! God, be witness betwixt me, and thee!
51 Labani anatinso kwa Yakobo, “Taona pano pali miyala ndi chipilala chimene ndayimika pakati pa iwe ndi ine.
And Laban said to Jacob—Behold this heap, and behold this pillar, which I have set betwixt me, and thee:
52 Mulu wa miyala uwu ndi chipilalachi ndi mboni. Ine sindidzadutsa mulu wa miyalawu kudzalimbana ndi iwe. Iwenso usadzadutse mulu wa miyalawu kudzalimbana nane.
A witness, be this heap, and, a witness, the pillar, —That, I, am not to pass, unto thee, over this heap, And, thou, art not to pass, unto me, over this heap and this pillar for harm.
53 Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu wa Nahori ndiye adzatiweruze.” Choncho Yakobo analumbira mʼdzina la Mulungu amene Isake, abambo ake ankamuopa.
The Gods of Abraham and the Gods of Nahor judge betwixt us—the Gods of their fathers. And Jacob sware by the Dread of his father Isaac:
54 Yakobo anapereka nsembe pa phiri paja, ndipo anayitana abale ake kuti adzadye chakudya. Atadya chakudya anagona pa phiri pomwepo.
and Jacob offered sacrifice in the mountain, and called on his brethren to eat bread. So they did eat bread, and tarried the night in the mountain.
55 Mmamawa wake, Labani anapsompsona zidzukulu zake ndi ana ake nawadalitsa. Kenaka ananyamuka kubwerera ku mudzi.
And Laban rose up early in the morning, and kissed his sons and his daughters, and blessed them: and Laban went his way and returned to his place.