< Genesis 30 >

1 Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”
Кынд а вэзут Рахела кэ ну фаче копий луй Иаков, а пизмуит пе сорэ-са ши а зис луй Иаков: „Дэ-мь копий орь мор!”
2 Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”
Иаков с-а мыният пе Рахела ши а зис: „Сунт еу оаре ын локул луй Думнезеу, каре те-а оприт сэ ай копий?”
3 Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”
Еа а зис: „Ятэ роаба мя Билха; кулкэ-те ку еа, ка сэ наскэ пе ӂенункий мей ши сэ ам ши еу копий прин еа.”
4 Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha,
Ши й-а дат де невастэ пе роаба ей Билха, ши Иаков с-а кулкат ку еа.
5 ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna.
Билха а рэмас ынсэрчинатэ ши а нэскут луй Иаков ун фиу.
6 Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.
Рахела а зис: „Мь-а фэкут Думнезеу дрептате, мь-а аузит гласул ши мь-а дэруит ун фиу.” Де ачея й-а пус нумеле Дан.
7 Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
Билха, роаба Рахелей, а рэмас яр ынсэрчинатэ ши а нэскут луй Иаков ун ал дойля фиу.
8 Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.
Рахела а зис: „Ам луптат ку Думнезеу ымпотрива сурорий меле ши ам бируит.” Де ачея й-а пус нумеле Нефтали.
9 Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye.
Кынд а вэзут Лея кэ ну май наште, а луат пе роаба са Зилпа ши а дат-о луй Иаков де невастэ.
10 Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna.
Зилпа, роаба Леей, а нэскут луй Иаков ун фиу.
11 Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.
„Ку норок!” а зис Лея. Де ачея й-а пус нумеле Гад.
12 Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
Зилпа, роаба Леей, а нэскут ун ал дойля фиу луй Иаков.
13 Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.
„Че феричитэ сунт!” а зис Лея; „кэч фемеиле мэ вор нуми феричитэ.” Де ачея й-а пус нумеле Ашер.
14 Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”
Рубен а ешит одатэ афарэ, пе время сечератулуй грыулуй, ши а гэсит мандрагоре пе кымп. Ле-а адус мамей сале Лея. Атунч, Рахела а зис Леей: „Дэ-мь, те рог, дин мандрагореле фиулуй тэу.”
15 Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.” Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”
Еа й-а рэспунс: „Ну-ць ажунӂе кэ мь-ай луат бэрбатул, де врей сэ ей ши мандрагореле фиулуй меу?” Ши Рахела а зис: „Ей бине! Поате сэ се кулче ку тине ын ноаптя ачаста пентру мандрагореле фиулуй тэу.”
16 Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.
Сяра, пе кынд се ынторчя Иаков де ла кымп, Лея й-а ешит ынаинте ши а зис: „Ла мине ай сэ вий, кэч те-ам кумпэрат ку мандрагореле фиулуй меу.” Ши ын ноаптя ачея с-а кулкат ку еа.
17 Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu.
Думнезеу а аскултат пе Лея, каре а рэмас ынсэрчинатэ ши а нэскут луй Иаков ал чинчиля фиу.
18 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.
Лея а зис: „М-а рэсплэтит Думнезеу, пентру кэ ам дат бэрбатулуй меу пе роаба мя.” Де ачея й-а пус нумеле Исахар.
19 Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi.
Лея а рэмас ярэшь ынсэрчинатэ ши а нэскут ун ал шаселя фиу луй Иаков.
20 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.
Лея а зис: „Фрумос дар мь-а дат Думнезеу! Де дата ачаста, бэрбатул меу ва локуи ку мине, кэч й-ам нэскут шасе фий.” Де ачея й-а пус нумеле Забулон.
21 Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.
Ын урмэ, а нэскут о фатэ, кэрея й-а пус нумеле Дина.
22 Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana.
Думнезеу Шь-а адус аминте де Рахела, а аскултат-о ши а фэкут-о сэ айбэ копий.
23 Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.”
Еа а рэмас ынсэрчинатэ ши а нэскут ун фиу, ши а зис: „Мь-а луат Думнезеу окара!”
24 Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”
Ши й-а пус нумеле Иосиф, зикынд: „Домнул сэ-мь май адауӂе ун фиу!”
25 Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu.
Дупэ че а нэскут Рахела пе Иосиф, Иаков а зис луй Лабан: „Ласэ-мэ сэ плек, ка сэ мэ дук акасэ, ын цара мя.
26 Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”
Дэ-мь невестеле ши копиий, пентру каре ць-ам служит, ши вой плека, фииндкэ штий че службэ ць-ам фэкут.”
27 Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.”
Лабан й-а зис: „Дакэ ам кэпэтат тречере ынаинтя та, май зэбовеште; вэд бине кэ Домнул м-а бинекувынтат дин причина та;
28 Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”
хотэрэште-мь симбрия та ши ць-о вой да.”
29 Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira.
Иаков й-а рэспунс: „Штий кум ць-ам служит ши кум ць-ау пропэшит вителе ку мине,
30 Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”
кэч пуцинул пе каре-л авяй ынаинте де вениря мя а крескут мулт ши Домнул те-а бинекувынтат орьынкотро ам мерс еу. Акум, кынд ам сэ мунческ ши пентру каса мя?”
31 Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?” Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira:
Лабан а зис: „Че сэ-ць дау?” Ши Иаков а рэспунс: „Сэ ну-мь дай нимик. Дакэ те ынвоешть ку че-ць вой спуне, ыць вой паште турма ши май департе ши о вой пэзи.
32 Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga.
Азь ам сэ трек прин тоатэ турма та; ам сэ пун деопарте дин ой орьче мел сеин ши пестриц ши орьче мел негру, ши дин капре, тот че есте пестриц ши сеин. Ачаста сэ фие симбрия мя.
33 Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”
Ятэ кум се ва доведи чинстя мя: де акум ынколо, кынд ай сэ вий сэ-мь везь симбрия, тот че ну ва фи сеин ши пестриц ынтре капре ши негру ынтре мей ши се ва гэси ла мине сэ фие сокотит ка фурат.”
34 Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.”
Лабан а зис: „Бине! Фие аша кум ай зис.”
35 Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta.
Ын ачеяшь зи, а пус деопарте цапий бэлцаць ши пестриць, тоате капреле сеине ши пестрице, тоате челе че авяу алб пе еле ши тоць меий каре ерау негри. Ле-а дат ын мыниле фиилор сэй.
36 Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.
Апой а пус о депэртаре де трей зиле де друм ынтре ел ши Иаков, ши Иаков пэштя челелалте ой але луй Лабан.
37 Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera.
Иаков а луат нуеле верзь де плоп, де мигдал ши де платан; а деспуят де пе еле фыший де коажэ ши а фэкут сэ се вадэ албяца каре ера пе нуеле.
38 Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana.
Апой а пус нуелеле пе каре ле деспуясе де коажэ ын жгябурь, ын адэпэторь, суб окий оилор каре веняу сэ бя, ка, атунч кынд вор вени сэ бя, сэ зэмисляскэ.
39 Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho.
Оиле зэмисляу уйтынду-се ла нуеле ши фэчяу мей бэлцаць, сеинь ши пестриць.
40 Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani.
Иаков деспэрця меий ачештя ши абэтя фецеле оилор дин турма луй Лабан кэтре челе сеине ши бэлцате. Шь-а фэкут астфел турме деосебите, пе каре ну ле-а ымпреунат ку турма луй Лабан.
41 Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija.
Орь де кыте орь се ынфербынтау оиле челе май тарь, Иаков пуня нуелеле ын жгябурь, суб окий оилор, ка еле сэ зэмисляскэ уйтынду-се ла нуеле.
42 Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo.
Кынд оиле ерау слабе, ну пуня нуелеле; аша кэ челе слабе ерау пентру Лабан, яр челе тарь, пентру Иаков.
43 Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.
Омул ачеста с-а ымбогэцит астфел дин че ын че май мулт; а авут мулте турме, робь ши роабе, кэмиле ши мэгарь.

< Genesis 30 >