< Genesis 30 >

1 Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”
Kwathi uRasheli esebonile ukuthi wayengamzaleli uJakobe, uRasheli waba lomona ngodadewabo, wathi kuJakobe: Nginika abantwana, kodwa nxa kungenjalo ngife.
2 Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”
Ngakho lwavutha ulaka lukaJakobe kuRasheli, wathi: Ngisesikhundleni sikaNkulunkulu okwenqabele isithelo sesizalo yini?
3 Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”
Wasesithi: Khangela, incekukazi yami uBiliha, ngena kuye, ukuze azalele emadolweni ami, ukuze lami ngakhiwe kuye.
4 Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha,
Wasemnika uBiliha incekukazi yakhe abe ngumkakhe; uJakobe wasengena kuye.
5 ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna.
UBiliha wasethatha isisu, wamzalela uJakobe indodana.
6 Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.
URasheli wasesithi: UNkulunkulu ungahlulele, njalo uzwile ilizwi lami, wanginika indodana. Ngakho wayitha ibizo layo uDani.
7 Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
UBiliha incekukazi kaRasheli wasebuya ethatha isisu, wamzalela uJakobe indodana yesibili.
8 Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.
URasheli wasesithi: Ngibindene lokubindana okulamandla lodadewethu, njalo ngehlula; ngakho wayitha ibizo layo uNafithali.
9 Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye.
Kwathi uLeya esebonile ukuthi usemi ukuzala, wathatha uZilipa incekukazi yakhe, wamnika uJakobe abe ngumkakhe.
10 Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna.
UZilipa incekukazi kaLeya wasemzalela uJakobe indodana.
11 Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.
ULeya wasesithi: Kuyeza inhlanhla. Wayitha ibizo layo uGadi.
12 Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
UZilipa incekukazi kaLeya wasemzalela uJakobe indodana yesibili.
13 Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.
ULeya wasesithi: Kungokwentokozo yami, ngoba amadodakazi azakuthi ngilentokozo. Wayitha ibizo layo uAsheri.
14 Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”
URubeni wasehamba ngensuku zokuvuna ingqoloyi, wafica amamandrake ensimini, wawaletha kuLeya unina. URasheli wasesithi kuLeya: Ake ungiphe emamandrakeni endodana yakho.
15 Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.” Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”
Wasesithi kuye. Kuyinto encinyane yini ukuthi uthethe indoda yami? Usuzathatha lamamandrake endodana yami yini? URasheli wasesithi: Ngakho uzalala lawe ngalobubusuku ngenxa yamamandrake endodana yakho.
16 Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.
Kwathi uJakobe esebuya evela emasimini kusihlwa, uLeya waphuma ukumhlangabeza, wathi: Kimi uzangena, ngoba ukukuqhatsha ngikuqhatshile ngamamandrake endodana yami. Waselala laye ngalobobusuku.
17 Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu.
UNkulunkulu wasemuzwa uLeya; wasethatha isisu, wamzalela uJakobe indodana yesihlanu.
18 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.
ULeya wasesithi: UNkulunkulu unginikile umvuzo wami, ngoba ngayinika indoda yami incekukazi yami; waseyitha ibizo layo uIsakari.
19 Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi.
ULeya wasephinda ethatha isisu, wamzalela uJakobe indodana yesithupha.
20 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.
ULeya wasesithi: UNkulunkulu unginikile mina isipho esihle; khathesi indoda yami izahlala lami, ngoba ngiyizalele amadodana ayisithupha, waseyitha ibizo layo uZebuluni.
21 Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.
Emva kwalokhu wasezala indodakazi, wayitha ibizo layo uDina.
22 Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana.
UNkulunkulu wasemkhumbula uRasheli, uNkulunkulu wasemuzwa, wavula isizalo sakhe.
23 Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.”
Wasethatha isisu, wazala indodana, wathi: UNkulunkulu ususile ihlazo lami.
24 Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”
Waseyitha ibizo layo uJosefa, esithi: INkosi kayengeze kimi enye indodana.
25 Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu.
Kwasekusithi uRasheli esemzele uJosefa, uJakobe wathi kuLabani: Ngiyekela ngihambe ukuze ngiye endaweni yakithi, lelizweni lakithi.
26 Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”
Ngipha omkami labantwana bami engibasebenzele kuwe ukuze ngihambe, ngoba wena uyazi umsebenzi wami engikusebenzele wona.
27 Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.”
ULabani wasesithi kuye: Uba-ke ngithole umusa emehlweni akho; sengibonile ngokukhangela ukuthi iNkosi ingibusisile ngenxa yakho.
28 Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”
Wathi futhi: Ngimisela iholo lakho, njalo ngizakupha.
29 Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira.
Wasesithi kuye: Wena yazi ukuthi ngikusebenzele njani lokuthi izifuyo zakho bezinjani lami.
30 Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”
Ngoba okulutshwana owawulakho mandulo kwami, kwanda kakhulu kwaba yinkithinkithi; iNkosi ikubusisile ekufikeni kwami; pho-ke, ngizayisebenzela nini lami indlu yami?
31 Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?” Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira:
Wasesithi: Ngizakuphani? UJakobe wasesithi: Kawuyikunginika lutho, uba uzangenzela le into; ngizabuya ngeluse izimvu zakho ngizilinde.
32 Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga.
Ngizadabula phakathi komhlambi wonke wakho lamuhla, ngehlukanise lapho yonke imvu elamabala lelamachatha, layo yonke imvu ensundu phakathi kwezimvu, lezilamabala lezilamachatha ezimbuzini, zibe liholo lami.
33 Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”
Njalo ukulunga kwami kuzangifakazela ngosuku oluzayo, uba usiza mayelana leholo lami, phambi kwakho; konke okungelamabala lamachatha ezimbuzini, lokunsundu emawundlwini, kuyabe kuntshontshiwe uba kukimi.
34 Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.”
ULabani wasesithi: Khangela, ye, kakube njengelizwi lakho.
35 Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta.
Wasezehlukanisa mhlalokho impongo ezingamaqamule lezilamabala lazo zonke izibhuzikazi ezilamabala lezilamachatha, lakho konke okulokumhlophe, lakho konke okunsundu emawundlwini, wakunikela esandleni samadodana akhe.
36 Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.
Wabeka ummango wensuku ezintathu phakathi kwakhe loJakobe. UJakobe waseselusa imihlambi eseleyo kaLabani.
37 Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera.
UJakobe wasezithathela ingatsha ezimanzi zephophula leze-alimondi lezingelamaxolo, webula kuzo imizila emhlophe, wembula okumhlophe okwakusezingatsheni.
38 Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana.
Wasefaka ingatsha ayezebulile emigelweni lemikolweni yokunathela yamanzi maqondana lemihlambi, lapho imihlambi efika khona ukunatha; yamitha ekufikeni kwayo ukuzanatha.
39 Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho.
Kwathi imihlambi isimithi ezingatsheni, imihlambi yazala amaqamule, alamabala lalamachatha.
40 Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani.
UJakobe wasesehlukanisa amawundlu; wakhangelisa ubuso bomhlambi kwezingamaqamule lazo zonke ezinsundu zomhlambi kaLabani; wabeka imihlambi yakhe yodwa, engayibeki emhlanjini kaLabani.
41 Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija.
Kwasekusithi loba nini eziqinileyo zomhlambi sezimitha, uJakobe wafaka izingatsha phambi kwamehlo omhlambi emigelweni, ukuze zidabule phakathi kwezingatsha.
42 Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo.
Kodwa nxa umhlambi ububuthakathaka kazifakanga; ngalokhu ebuthakathaka yaba ngekaLabani, leqinileyo ngekaJakobe.
43 Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.
Lendoda yaqhamuka yaba nkulu kakhulu, yaba lemihlambi eminengi lezincekukazi lezinceku lamakamela labobabhemi.

< Genesis 30 >