< Genesis 30 >
1 Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”
Forsothe Rachel seiy, that sche was vnfruytful, and hadde enuye to the sister, and seide to hir hosebonde, Yyue thou fre children to me, ellis Y schal die.
2 Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”
To whom Jacob was wrooth, and answerde, Wher Y am for God, which haue priued thee fro the fruyt of thi wombe?
3 Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”
And sche seide, Y haue `a seruauntesse Bala, entre thou to hir that she childe on my knees, and that Y haue sones of hir.
4 Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha,
And sche yaf to hym Bala in to matrimony;
5 ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna.
and whanne the hosebonde hadde entrid to hir, sche conseyuede, and childide a sone.
6 Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.
And Rachel seide, the Lord demede to me, and herde my preier, and yaf a sone to me; and therfor sche clepide his name Dan.
7 Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
And eft Bala conseyuede, and childide anothir sone,
8 Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.
for whom Rachel seide, The Lord hath maad me lijk to my sistir, and Y wexide strong; and sche clepide hym Neptalym.
9 Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye.
Lya feelide that sche ceesside to bere child, and sche yaf Selfa, hir handmayde, to the hosebonde.
10 Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna.
And whanne Selfa aftir conseyuyng childide a sone, Lya seide, Blessidly;
11 Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.
and therfor sche clepide his name Gad.
12 Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
Also Selfa childide anothir sone,
13 Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.
and Lia seide, This is for my blis, for alle wymmen schulen seie me blessid; therfor sche clepide hym Aser.
14 Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”
Forsothe Ruben yede out in to the feeld in the tyme of wheete heruest, and foond mandragis, whiche he brouyte to Lya, his modir. And Rachel seide, Yyue thou to me a part of the mandragis of thi sone.
15 Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.” Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”
Lya answeride, Whether it semeth litil to thee, that thou hast rauyschid the hosebonde fro me, no but thou take also the mandragis of my sone? Rachel seide, The hosebonde sleepe with thee in this nyyt for the mandragis of thi sone.
16 Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.
And whanne Jacob cam ayen fro the feeld at euentid, Lya yede out in to his comyng, and seide, Thou shalt entre to me, for Y haue hired thee with hire for the mandragis of my sone. He slepte with hir in that nyyt;
17 Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu.
and God herde hir preiers, and sche conseyuede, and childide the fyuethe sone;
18 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.
and seide, God yaf meede to me, for Y yaf myn handmayde to myn hosebond; and sche clepide his name Isacar.
19 Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi.
Eft Lia conseyuede, and childide the sixte sone,
20 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.
and seide, The Lord hath maad me riche with a good dower, also in this tyme myn hosebonde schal be with me, for Y childide sixe sones to hym; and therfore sche clepide his name Sabulon.
21 Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.
Aftir whom sche childide a douyter, Dyna bi name.
22 Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana.
Also the Lord hadde mynde on Rachel, and herde hir, and openyde hir wombe.
23 Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.”
And sche conseyuede, and childide a sone, and seide, God hath take a wey my schenschipe; and sche clepid his name Joseph,
24 Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”
and seide, The Lord yyue to me another sone.
25 Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu.
Sotheli whanne Joseph was borun, Jacob seide to his wyues fadir, Delyuere thou me, that Y turne ayen in to my cuntrey and to my lond.
26 Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”
Yyue thou to me my wyues and fre children for whiche Y seruede thee, that Y go; forsothe thou knowist the seruyce bi which Y seruede thee.
27 Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.”
Laban seide to hym, Fynde Y grace in thi siyt, Y haue lerned bi experience that God blesside me for thee;
28 Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”
ordeyne thou the meede which Y schal yyue to thee.
29 Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira.
And he answeride, Thou woost hou Y seruede thee, and hou greet thi possessioun was in myn hondis;
30 Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”
thou haddist litil bifore that Y cam to thee, and now thou art maad riche, and the Lord blesside thee at myn entryng; therfor it is iust that Y purueye sum tyme also to myn hows.
31 Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?” Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira:
And Laban seide, What schal Y yyue to thee? And Jacob seide, Y wole no thing but if thou doist that that Y axe, eft Y schal fede and kepe thi scheep.
32 Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga.
Cumpasse thou alle thi flockis, and departe thou alle diuerse scheep and of spottid flees, and what euer thing schal be dun, and spottid, and dyuerse, as wel in scheep as in geet, it schal be my mede.
33 Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”
And my riytfulnesse schal answere to me to morewe, whanne the tyme of couenaunt schal come bifor thee; and alle that ben not dyuerse and spottid and dunne, as well in sheep as in geet, schulen repreue me of thefte.
34 Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.”
And Laban seide, Y haue acceptable that that thou axist.
35 Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta.
And he departide in that dai the geet, and scheep, geet buckis, and rammes, dyuerse and spottid. Sothely he bitook al the flok of o coloure, that is, of white and of blak flees in the hond of hise sones;
36 Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.
and he settide the space of weie of thre daies bitwixe hise sones and the hosebonde of hise douytris, that fedde othere flockis` of hym.
37 Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera.
Therfor Jacob took greene yerdis of popeleris, and of almoundis, and of planes, and in parti dide awei the rynde of tho, and whanne the ryndis weren `drawun a wei, whitnesse apperide in these that weren maad bare; sothely tho that weren hoole dwelliden grene, and bi this maner the coloure was maad dyuerse.
38 Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana.
And Jacob puttide tho yerdis in the trowis, where the watir was held out, that whanne the flockis schulden come to drynke, thei schulden haue the yerdis bifor the iyen, and schulden conseyue in the siyt of the yerdis.
39 Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho.
And it was doon that in thilke heete of riding the sheep schulde biholde the yerdis, and that thei schulden brynge forth spotti beestis, and dyuerse, and bispreynt with dyuerse colour.
40 Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani.
And Jacob departide the floc, and puttide the yerdis in the trowis bifor the iyen of the rammys. Sotheli alle the white and blake weren Labans; sotheli the othere weren Jacobis; for the flockis weren departid bytwixe hem silf.
41 Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija.
Therfor whanne the scheep weren ridun in the firste tyme, Jacob puttide the yerdis in the `trouyis of watir bifor the iyen of rammys and of scheep, that thei schulden conseyue in the siyt of tho yerdis.
42 Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo.
Forsothe whanne the late medlyng and the laste conseyuyng weren, Jacob puttide not tho yerdis; and tho that weren late, weren maad Labans, and tho that weren of the firste tyme weren Jacobis.
43 Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.
And he was maad ful riche, and hadde many flockis, handmaydis, and seruauntis, camels, and assis.