< Genesis 30 >
1 Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”
and to see: see Rachel for not to beget to/for Jacob and be jealous Rachel in/on/with sister her and to say to(wards) Jacob to give [emph?] to/for me son: child and if: surely yes nothing to die I
2 Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”
and to be incensed face: anger Jacob in/on/with Rachel and to say underneath: instead God I which to withhold from you fruit belly: womb
3 Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”
and to say behold maidservant my Bilhah to come (in): come to(wards) her and to beget upon knee my and to build also I from her
4 Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha,
and to give: give to/for him [obj] Bilhah maidservant her to/for woman: wife and to come (in): come to(wards) her Jacob
5 ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna.
and to conceive Bilhah and to beget to/for Jacob son: child
6 Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.
and to say Rachel to judge me God and also to hear: hear in/on/with voice my and to give: give to/for me son: child upon so to call: call by name his Dan
7 Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
and to conceive still and to beget Bilhah maidservant Rachel son: child second to/for Jacob
8 Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.
and to say Rachel wrestling God to twist with sister my also be able and to call: call by name his Naphtali
9 Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye.
and to see: see Leah for to stand: stand from to beget and to take: take [obj] Zilpah maidservant her and to give: give [obj] her to/for Jacob to/for woman: wife
10 Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna.
and to beget Zilpah maidservant Leah to/for Jacob son: child
11 Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.
and to say Leah (to come (in): come fortune *Q(K)*) and to call: call by [obj] name his Gad
12 Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
and to beget Zilpah maidservant Leah son: child second to/for Jacob
13 Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.
and to say Leah in/on/with happy my for to bless me daughter and to call: call by [obj] name his Asher
14 Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”
and to go: went Reuben in/on/with day harvest wheat and to find mandrake in/on/with land: country and to come (in): bring [obj] them to(wards) Leah mother his and to say Rachel to(wards) Leah to give: give please to/for me from mandrake son: child your
15 Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.” Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”
and to say to/for her little to take: take you [obj] man: husband my and to/for to take: take also [obj] mandrake son: child my and to say Rachel to/for so to lie down: have sex with you [the] night underneath: instead mandrake son: child your
16 Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.
and to come (in): come Jacob from [the] land: country in/on/with evening and to come out: come Leah to/for to encounter: meet him and to say to(wards) me to come (in): come for to hire to hire you in/on/with mandrake son: child my and to lie down: have sex with her in/on/with night he/she/it
17 Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu.
and to hear: hear God to(wards) Leah and to conceive and to beget to/for Jacob son: child fifth
18 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.
and to say Leah to give: give God wages my which to give: give maidservant my to/for man: husband my and to call: call by name his Issachar
19 Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi.
and to conceive still Leah and to beget son: child sixth to/for Jacob
20 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.
and to say Leah to endow me God [obj] me dowry pleasant [the] beat to honour me man: husband my for to beget to/for him six son: child and to call: call by [obj] name his Zebulun
21 Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.
and after to beget daughter and to call: call by [obj] name her Dinah
22 Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana.
and to remember God [obj] Rachel and to hear: hear to(wards) her God and to open [obj] womb her
23 Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.”
and to conceive and to beget son: child and to say to gather God [obj] reproach my
24 Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”
and to call: call by [obj] name his Joseph to/for to say to add LORD to/for me son: child another
25 Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu.
and to be like/as as which to beget Rachel [obj] Joseph and to say Jacob to(wards) Laban to send: depart me and to go: went to(wards) place my and to/for land: country/planet my
26 Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”
to give: give [emph?] [obj] woman: wife my and [obj] youth my which to serve [obj] you in/on/with them and to go: went for you(m. s.) to know [obj] service my which to serve you
27 Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.”
and to say to(wards) him Laban if please to find favor in/on/with eye: seeing your to divine and to bless me LORD in/on/with because of you
28 Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”
and to say to pierce [emph?] wages your upon me and to give: pay
29 Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira.
and to say to(wards) him you(m. s.) to know [obj] which to serve you and [obj] which to be livestock your with me
30 Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”
for little which to be to/for you to/for face: before my and to break through to/for abundance and to bless LORD [obj] you to/for foot my and now how to make: offer also I to/for house: household my
31 Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?” Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira:
and to say what? to give: give to/for you and to say Jacob not to give: give to/for me anything if to make: do to/for me [the] word: thing [the] this to return: again to pasture flock your to keep: guard
32 Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga.
to pass in/on/with all flock your [the] day to turn aside: remove from there all sheep speckled and to spot and all sheep darkened in/on/with sheep and to spot and speckled in/on/with goat and to be wages my
33 Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”
and to answer in/on/with me righteousness my in/on/with day tomorrow for to come (in): come upon wages my to/for face of your all which nothing he speckled and to spot in/on/with goat and darkened in/on/with sheep to steal he/she/it with me
34 Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.”
and to say Laban look! if to be like/as word: speaking your
35 Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta.
and to turn aside: remove in/on/with day [the] he/she/it [obj] [the] male goat [the] striped and [the] to spot and [obj] all [the] goat [the] speckled and [the] to spot all which white in/on/with him and all darkened in/on/with sheep and to give: put in/on/with hand: power son: child his
36 Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.
and to set: make way: journey three day between him and between Jacob and Jacob to pasture [obj] flock Laban [the] to remain
37 Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera.
and to take: take to/for him Jacob rod poplar fresh and almond and plane tree and to peel in/on/with them stripe white exposing [the] white which upon [the] rod
38 Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana.
and to set [obj] [the] rod which to peel in/on/with trough in/on/with trough [the] water which to come (in): come [the] flock to/for to drink to/for before [the] flock and to conceive in/on/with to come (in): come they to/for to drink
39 Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho.
and to conceive [the] flock to(wards) [the] rod and to beget [the] flock striped speckled and to spot
40 Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani.
and [the] sheep to separate Jacob and to give: put face [the] flock to(wards) striped and all darkened in/on/with flock Laban and to set: make to/for him flock to/for alone him and not to set: put them upon flock Laban
41 Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija.
and to be in/on/with all to conceive [the] flock [the] to conspire and to set: put Jacob [obj] [the] rod to/for eye [the] flock in/on/with trough to/for to conceive her in/on/with rod
42 Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo.
and in/on/with to enfeeble [the] flock not to set: put and to be [the] to enfeeble to/for Laban and [the] to conspire to/for Jacob
43 Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.
and to break through [the] man much much and to be to/for him flock many and maidservant and servant/slave and camel and donkey