< Genesis 30 >

1 Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”
Then Rachel, discerning that she was infertile, envied her sister, and so she said to her husband, “Give me children, otherwise I will die.”
2 Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”
Jacob, being angry, responded to her, “Am I in the place of God, who has deprived you of the fruit of your womb?”
3 Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”
But she said: “I have a handmaid Bilhah. Go in to her, so that she may give birth upon my knees, and I may have sons by her.”
4 Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha,
And she gave him Bilhah in marriage.
5 ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna.
And when her husband had gone in to her, she conceived and bore a son.
6 Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.
And Rachel said, “The Lord has judged for me, and he has heeded my voice, giving me a son.” And because of this, she called his name Dan.
7 Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
And conceiving again, Bilhah bore another,
8 Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.
about whom Rachel said, “God has compared me with my sister, and I have prevailed.” And she called him Naphtali.
9 Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye.
Leah, perceiving that she had desisted from child-bearing, delivered Zilpah, her handmaid, to her husband.
10 Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna.
And she, after having borne a son with difficulty,
11 Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.
said: “Happiness!” And for this reason, she called his name Gad.
12 Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
Likewise, Zilpah bore another.
13 Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.
And Leah said, “This one is for my happiness. Indeed, women will call me blessed.” Because of this, she called him Asher.
14 Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”
Then Reuben, going out into the field at the time of the wheat harvest, found mandrakes. These he brought to his mother Leah. And Rachel said, “Give me a portion of your son’s mandrakes.”
15 Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.” Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”
She responded, “Does it seem like such a small matter to you, that you have usurped from me my husband, unless you will also take my son’s mandrakes?” Rachel said, “He will sleep with you this night because of your son’s mandrakes.”
16 Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.
And when Jacob returned from the field in the evening, Leah went out to meet him, and she said, “You will enter to me, because I have hired you for the reward of my son’s mandrakes.” And he slept with her that night.
17 Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu.
And God heard her prayers. And she conceived and bore a fifth son.
18 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.
And she said, “God has given a reward to me, because I gave my handmaid to my husband.” And she called his name Issachar.
19 Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi.
Conceiving again, Leah bore a sixth son.
20 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.
And she said: “God has endowed me with a good dowry. And now, at this turn, my husband will be with me, because I have conceived six sons for him.” And therefore she called his name Zebulun.
21 Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.
After him, she bore a daughter, named Dinah.
22 Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana.
The Lord, likewise remembering Rachel, heeded her and opened her womb.
23 Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.”
And she conceived and bore a son, saying, “God has taken away my reproach.”
24 Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”
And she called his name Joseph, saying, “The Lord has added to me another son.”
25 Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu.
But when Joseph was born, Jacob said to his father-in-law: “Release me, so that I may return to my native country and to my land.
26 Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”
Give me my wives, and my children, for whom I have served you, so that I may depart. You know the servitude with which I have served you.”
27 Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.”
Laban said to him: “May I find grace in your sight. I have learned by experience that God has blessed me because of you.
28 Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”
Choose your wages, which I will give you.”
29 Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira.
But he responded: “You know how I have served you, and how great your possession became in my hands.
30 Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”
You had little before I came to you, and now you have achieved riches. And the Lord has blessed you since my arrival. It is just, therefore, that at some time I also should provide for my own house.”
31 Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?” Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira:
And Laban said, “What shall I give to you?” But he said, “I want nothing. But if you will do what I ask, I will feed and guard your sheep again.
32 Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga.
Go around through all your flocks and separate all the sheep of variegated or spotted fleece; and whatever will be darkened or blemished or variegated, as much among the sheep as among the goats, will be my wages.
33 Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”
And my justice will answer on my behalf tomorrow, when the time of settlement arrives before you. And all that is not variegated or blemished or darkened, as much among the sheep as among the goats, these will prove me to be a thief.”
34 Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.”
And Laban said, “I hold favor for this request.”
35 Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta.
And on that day he separated the she-goats, and the sheep, and the he-goats, and the rams with variegations or with blemishes. But every one of the flock which was of one color, that is, of white or of black fleece, he delivered into the hands of his sons.
36 Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.
And he established a distance of three days journey between himself and his son-in-law, who pastured the remainder of his flock.
37 Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera.
Then Jacob, taking green branches of poplar, and almond, and sycamore trees, debarked them in part. And when the bark was pulled off, in the parts that were stripped, there appeared whiteness, yet the parts that were left whole, remained green. And so, in this way the color was made variegated.
38 Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana.
And he placed them in the troughs, where the water was poured out, so that when the flocks had arrived to drink, they would have the branches before their eyes, and in their sight they might conceive.
39 Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho.
And it happened that, in the very heat of joining together, the sheep looked upon the branches, and they bore the blemished and the variegated, those speckled with diverse color.
40 Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani.
And Jacob divided the flock, and he set the branches in the troughs before the eyes of the rams. Now whatever was white or black belonged to Laban, but, in truth, the others belonged to Jacob, for the flocks were dispersed among one another.
41 Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija.
Therefore, when the first to arrive were climbing on the ewes, Jacob placed the branches in the troughs of water before the eyes of the rams and the sheep, so that they might conceive while they were gazing upon them.
42 Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo.
Yet when the late arrivals and the last to conceive were let in, he did not place these. And so those that arrived late became Laban’s, and those that arrived first became Jacob’s.
43 Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.
And the man was enriched beyond limit, and he had many flocks, women servants and men servants, camels and donkeys.

< Genesis 30 >