< Genesis 30 >

1 Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”
And when Rachel saw that she bore Jacob no sons, Rachel envied her sister, and she said to Jacob, Give me sons, or else I die.
2 Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”
And Jacob's anger was kindled against Rachel, and he said, Am I in God's stead, who has withheld from thee the fruit of the womb?
3 Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”
And she said, Behold, my maid Bilhah, go in to her, that she may bear upon my knees, and I also may obtain sons by her.
4 Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha,
And she gave him Bilhah her handmaid to wife, and Jacob went in to her.
5 ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna.
And Bilhah conceived, and bore Jacob a son.
6 Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.
And Rachel said, God has judged me, and has also heard my voice, and has given me a son. Therefore she called his name Dan.
7 Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
And Bilhah Rachel's handmaid conceived again, and bore Jacob a second son.
8 Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.
And Rachel said, With mighty wrestlings have I wrestled with my sister, and have prevailed. And she called his name Naphtali.
9 Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye.
When Leah saw that she had left off bearing, she took Zilpah her handmaid, and gave her to Jacob to wife.
10 Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna.
And Zilpah Leah's handmaid bore Jacob a son.
11 Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.
And Leah said, Fortunate! And she called his name Gad.
12 Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri.
And Zilpah Leah's handmaid bore Jacob a second son.
13 Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.
And Leah said, Happy am I! For the daughters will call me happy. And she called his name Asher.
14 Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”
And Reuben went in the days of wheat harvest, and found mandrakes in the field, and brought them to his mother Leah. Then Rachel said to Leah, Give me, I pray thee, of thy son's mandrakes.
15 Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.” Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”
And she said to her, Is it a small matter that thou have taken away my husband? And would thou take away my son's mandrakes also? And Rachel said, Therefore he shall lie with thee tonight for thy son's mandrakes.
16 Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.
And Jacob came from the field in the evening, and Leah went out to meet him, and said, Thou must come in to me, for I have surely hired thee with my son's mandrakes. And he lay with her that night.
17 Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu.
And God hearkened to Leah, and she conceived, and bore Jacob a fifth son.
18 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.
And Leah said, God has given me my hire, because I gave my handmaid to my husband. And she called his name Issachar.
19 Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi.
And Leah conceived again, and bore a sixth son to Jacob.
20 Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.
And Leah said, God has endowed me with a good dowry. Now my husband will dwell with me, because I have borne him six sons. And she called his name Zebulun.
21 Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.
And afterwards she bore a daughter, and called her name Dinah.
22 Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana.
And God remembered Rachel. And God hearkened to her, and opened her womb.
23 Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.”
And she conceived, and bore a son, and said, God has taken away my reproach.
24 Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”
And she called his name Joseph, saying, Jehovah adds another son to me.
25 Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu.
And it came to pass, when Rachel had borne Joseph, that Jacob said to Laban, Send me away, that I may go to my own place, and to my country.
26 Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”
Give me my wives and my children for whom I have served thee, and let me go, for thou know my service with which I have served thee.
27 Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.”
And Laban said to him, If now I have found favor in thine eyes, tarry, for I have learned by experience that Jehovah has blessed me for thy sake.
28 Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”
And he said, Appoint for me thy wages, and I will give it.
29 Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira.
And he said to him, Thou know how I have served thee, and how thy cattle have fared with me.
30 Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”
For it was little which thou had before I came, and it has increased to a multitude, and Jehovah has blessed thee wherever I turned. And now when shall I provide for my own house also?
31 Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?” Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira:
And he said, What shall I give thee? And Jacob said, Thou shall not give me anything. If thou will do this thing for me, I will again feed thy flock and keep it.
32 Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga.
I will pass through all thy flock today, removing from there every speckled and spotted one, and every black one among the sheep, and the spotted and speckled among the goats, and of such shall be my hire.
33 Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”
So shall my righteousness answer for me after this, when thou shall come concerning my hire that is before thee. Every one that is not speckled and spotted among the goats, and black among the sheep, that is with me, shall be considered stolen.
34 Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.”
And Laban said, Behold, O that it might be according to thy word.
35 Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta.
And he removed that day the he-goats that were ringstreaked and spotted, and all the she-goats that were speckled and spotted, every one that had white in it, and all the black ones among the sheep, and gave them into the hand of his sons.
36 Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.
And he set three days' journey between himself and Jacob. And Jacob fed the rest of Laban's flocks.
37 Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera.
And Jacob took for him rods of fresh poplar, and of the almond and of the plane tree, and peeled white streaks in them, and made the white which was in the rods appear.
38 Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana.
And he set the rods which he had peeled before the flocks in the gutters in the watering troughs where the flocks came to drink. And they conceived when they came to drink.
39 Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho.
And the flocks conceived before the rods, and the flocks brought forth ringstreaked, speckled, and spotted.
40 Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani.
And Jacob separated the lambs, and set the faces of the flocks toward the ringstreaked and all the black in the flock of Laban. And he put his own herds apart, and did not put them near Laban's flock.
41 Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija.
And it came to pass, whenever the stronger of the flock conceived, that Jacob laid the rods before the eyes of the flock in the gutters, that they might conceive among the rods,
42 Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo.
but when the flock were weak, he did not put them in. So the weaker were Laban's, and the stronger Jacob's.
43 Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.
And the man increased exceedingly, and had large flocks, and maid-servants and men-servants, and camels and donkeys.

< Genesis 30 >