< Genesis 3 >
1 Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’”
Али змија беше лукава мимо све звери пољске, које створи Господ Бог; па рече жени: Је ли истина да је Бог казао да не једете са сваког дрвета у врту?
2 Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu,
А жена рече змији: Ми једемо род са сваког дрвета у врту;
3 koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’”
Само род с оног дрвета усред врта, казао је Бог, не једите и не дирајте у њ, да не умрете.
4 “Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo.
А змија рече жени: Нећете ви умрети;
5 “Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”
Него зна Бог да ће вам се у онај дан кад окусите с њега отворити очи, па ћете постати као богови и знати шта је добро шта ли зло.
6 Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso.
И жена видећи да је род на дрвету добар за јело и да га је милина гледати и да је дрво врло драго ради знања, узабра род с њега и окуси, па даде и мужу свом, те и он окуси.
7 Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.
Тада им се отворише очи, и видеше да су голи; па сплетоше лишћа смоковог и начинише себи прегаче.
8 Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo.
И зачуше глас Господа Бога, који иђаше по врту кад захлади; и сакри се Адам и жена му испред Господа Бога међу дрвета у врту.
9 Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”
А Господ Бог викну Адама и рече му: Где си?
10 Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”
А он рече: Чух глас Твој у врту, па се поплаших, јер сам го, те се сакрих.
11 Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”
А Бог рече: Ко ти каза да си го? Да ниси јео с оног дрвета што сам ти забранио да не једеш с њега?
12 Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”
А Адам рече: Жена коју си удружио са мном, она ми даде с дрвета, те једох.
13 Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?” Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”
А Господ Бог рече жени: Зашто си то учинила? А жена одговори: Змија ме превари, те једох.
14 Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi, “Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse ndi nyama zakuthengo zonse. Udzayenda chafufumimba ndipo udzadya fumbi masiku onse a moyo wako.
Тада рече Господ Бог змији: Кад си то учинила, да си проклета мимо свако живинче и мимо све звери пољске; на трбуху да се вучеш и прах да једеш до свог века.
15 Ndipo ndidzayika chidani pakati pa iwe ndi mkaziyo, pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake; Iye adzaphwanya mutu wako ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”
И још мећем непријатељство између тебе и жене и између семена твог и семена њеног; оно ће ти на главу стајати а ти ћеш га у пету уједати.
16 Kwa mkaziyo Iye anati, “Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati; ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana. Udzakhumba mwamuna wako, ndipo adzakulamulira.”
А жени рече: Теби ћу многе муке задати кад затрудниш, с мукама ћеш децу рађати, и воља ће твоја стајати под влашћу мужа твог, и он ће ти бити господар.
17 Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’ “Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe, movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo masiku onse a moyo wako.
Па онда рече Адаму: Што си послушао жену и окусио с дрвета с ког сам ти забранио рекавши да не једеш с њега, земља да је проклета с тебе, с муком ћеш се од ње хранити до свог века;
18 Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula ndipo udzadya zomera zakuthengo.
Трње и коров ће ти рађати, а ти ћеш јести зеље пољско;
19 Kuti upeze chakudya udzayenera kukhetsa thukuta, mpaka utabwerera ku nthaka pakuti unachokera kumeneko; pakuti ndiwe fumbi ku fumbi komweko udzabwerera.”
Са знојем лица свог јешћеш хлеб, докле се не вратиш у земљу од које си узет; јер си прах, и у прах ћеш се вратити.
20 Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.
И Адам надеде жени својој име Јева, зато што је она мати свима живима.
21 Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka.
И начини Господ Бог Адаму и жени његовој хаљине од коже, и обуче их у њих.
22 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.”
И рече Господ Бог: Ето, човек поста као један од нас знајући шта је добро шта ли зло; али сада да не пружи руку своју и узбере и с дрвета од живота, и окуси, те до века живи.
23 Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera.
И Господ Бог изагна га из врта едемског да ради земљу, од које би узет;
24 Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.
И изагнав човека постави пред вртом едемским херувима с пламеним мачем, који се вијаше и тамо и амо, да чува пут ка дрвету од живота.