< Genesis 3 >
1 Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’”
Inyoka yayiliqili ukwedlula zonke izinyamazana zeganga uThixo uNkulunkulu ayezenzile. Yathi kowesifazane, “Kambe uNkulunkulu watsho ngeqiniso ukuthi, ‘Lingadli noma yisiphi isihlahla esivandeni’?”
2 Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu,
Owesifazane wathi enyokeni, “Singadla izithelo zezihlahla esivandeni,
3 koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’”
kodwa uNkulunkulu wathi, ‘Lingazidli izithelo zesihlahla esiphakathi laphakathi kwesivande, njalo lingasithinti, hlezi life.’”
4 “Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo.
Inyoka yathi kowesifazane, “Kalisoze life ngempela.
5 “Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”
Ngoba uNkulunkulu uyazi ukuthi lingasidla amehlo enu azavuleka, beselisiba njengoNkulunkulu, lazi okuhle lokubi.”
6 Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso.
Kwathi owesifazane ngokubona ukuthi izithelo zesihlahla leso zaziyikudla okuhle njalo zibukeka emehlweni, njalo kudingeka ukuzuza ukuhlakanipha, wakha ezinye wadla. Wapha njalo ezinye indoda yakhe ayelayo khonapho, layo yadla.
7 Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.
Amehlo abo bobabili asevuleka, basebenanzelela ukuthi babenqunu; yikho basebethungela ndawonye amahlamvu omkhiwa bazenzela izembatho ngawo.
8 Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo.
Indoda lomkayo basebesizwa umsindo kaThixo uNkulunkulu ehamba esivandeni ilanga selithambeme, basebemcatshela uThixo uNkulunkulu phakathi kwezihlahla zesivande.
9 Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”
Kodwa uThixo uNkulunkulu wayimemeza indoda wathi, “Ungaphi?”
10 Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”
Yaphendula yathi, “Ngikuzwile esivandeni, ngesaba ngoba benginqunu; yikho ngasengicatsha.”
11 Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”
Wasesithi, “Ngubani okutshelileyo ukuthi unqunu? Usudlile yini isihlahla engalilaya ukuthi lingasidli?”
12 Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”
Indoda yathi, “Umfazi owangipha yena, ungiphile ezinye izithelo zesihlahla ngazidla.”
13 Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?” Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”
Ngakho uThixo uNkulunkulu wathi kowesifazane, “Kuyini lokhu osukwenzile na?” Owesifazane wathi, “Inyoka ingikhohlisile, ngadla.”
14 Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi, “Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse ndi nyama zakuthengo zonse. Udzayenda chafufumimba ndipo udzadya fumbi masiku onse a moyo wako.
Ngakho uThixo uNkulunkulu wasesithi enyokeni, “Ngoba usukwenzile lokhu, Uqalekisiwe ngaphezu kwezifuyo zonke kanye lezinyamazana zonke zeganga! Uzahuba phansi ngesisu sakho njalo uzakudla uthuli zonke insuku zokuphila kwakho.
15 Ndipo ndidzayika chidani pakati pa iwe ndi mkaziyo, pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake; Iye adzaphwanya mutu wako ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”
Njalo ngizafaka ubutha phakathi kwakho lowesifazane, laphakathi kwenzalo yakho leyowesifazane; uzacobodisa ikhanda lakho, njalo wena uzagamula isithende sakhe.”
16 Kwa mkaziyo Iye anati, “Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati; ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana. Udzakhumba mwamuna wako, ndipo adzakulamulira.”
Kowesifazane wathi, “Ngizakwandisa ngokuphindiweyo inhlungu zakho nxa ubeletha; ngobuhlungu uzazala abantwana. Inkanuko yakho izakuba sendodeni yakho, njalo yona izabusa phezu kwakho.”
17 Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’ “Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe, movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo masiku onse a moyo wako.
Ku-Adamu wathi, “Ngoba ulalele umkakho wadla isihlahla engakulaya ngathi, ‘Ungasidli,’ Uqalekisiwe umhlabathi ngenxa yakho; ngokusebenza nzima uzakudla okuphuma kuwo zonke insuku zokuphila kwakho.
18 Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula ndipo udzadya zomera zakuthengo.
Uzamila ameva lezihlahlakazana zameva azahlaba wena, njalo uzakudla izihlahla zeganga.
19 Kuti upeze chakudya udzayenera kukhetsa thukuta, mpaka utabwerera ku nthaka pakuti unachokera kumeneko; pakuti ndiwe fumbi ku fumbi komweko udzabwerera.”
Ngezithukuthuku zebunzi lakho uzakudla ukudla kwakho uze ubuyele emhlabathini, njengoba wathathwa kuwo; ngoba uluthuli njalo uzabuyela othulini.”
20 Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.
U-Adamu wamutha umkakhe wathi ngu-Eva, ngoba wayezakuba ngunina wabo bonke abaphilayo.
21 Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka.
UThixo uNkulunkulu wenza imvunulo yesikhumba, wenzela u-Adamu lomkakhe, wabagqokisa.
22 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.”
Njalo uThixo uNkulunkulu wathi, “Umuntu manje usenjengomunye wethu, usekwazi okuhle lokubi. Kangavunyelwa ukuthi elule isandla sakhe akhe njalo isihlahla sokuphila adle, aphile laphakade.”
23 Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera.
Ngakho uThixo uNkulunkulu wamxotsha eSivandeni se-Edeni ukuthi asebenze umhlabathi ayethethwe kuwo.
24 Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.
Esemxotshile umuntu wamisa ngempumalanga kweSivande se-Edeni amakherubhi lenkemba ebhebhayo, iphazima isiyale lale ukulinda indlela eya esihlahleni sokuphila.