< Genesis 3 >

1 Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’”
And the snake was shrewd more than every animal of the field which he had made Yahweh God and he said to the woman indeed? that did he say God not you must eat from any tree of the garden.
2 Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu,
And she said the woman to the snake from [the] fruit of [the] tree[s] of the garden we will eat.
3 koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’”
And from [the] fruit of the tree which [is] in [the] middle of the garden he said God not you must eat from it and not you will touch it lest you should die!
4 “Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo.
And he said the snake to the woman not certainly you will die!
5 “Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”
For [is] knowing God that on [the] day eat you from it and they will be opened eyes your and you will be like God [those who] know good and evil.
6 Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso.
And she saw the woman that [was] good the tree for food and that [was] a delight it to the eyes and [it was] desirable the tree to make wise and she took some of fruit its and she ate and she gave [it] also to husband her with her and he ate.
7 Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.
And they were opened [the] eyes of both of them and they knew that [were] naked they and they sewed together leafage of a fig tree and they made for themselves loin coverings.
8 Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo.
And they heard [the] sound of Yahweh God walking about in the garden to [the] wind of the day and he hid himself the man and wife his from before Yahweh God in among [the] tree[s] of the garden.
9 Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”
And he called Yahweh God to the man and he said to him where [are]? you.
10 Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”
And he said sound your I heard in the garden and I was afraid for [was] naked I and I hid myself.
11 Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”
And he said who? did he tell to you that [were] naked you ¿ from the tree which I commanded you to not to eat from it have you eaten.
12 Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”
And he said the man the woman whom you put with me she she gave to me from the tree and I ate.
13 Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?” Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”
And he said Yahweh God to the woman what? this have you done and she said the woman the snake deceived me and I ate.
14 Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi, “Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse ndi nyama zakuthengo zonse. Udzayenda chafufumimba ndipo udzadya fumbi masiku onse a moyo wako.
And he said Yahweh God - to the snake for you have done this [are] cursed you more than all livestock and more than every animal of the field on belly your you will go and dust you will eat all [the] days of life your.
15 Ndipo ndidzayika chidani pakati pa iwe ndi mkaziyo, pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake; Iye adzaphwanya mutu wako ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”
And enmity - I will put between you and between the woman and between offspring your and between offspring her he he will bruise you head and you you will bruise him heel.
16 Kwa mkaziyo Iye anati, “Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati; ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana. Udzakhumba mwamuna wako, ndipo adzakulamulira.”
To the woman he said certainly I will increase pain your and pregnancy your with pain you will bear children and [will be] to husband your desire your and he he will rule over you.
17 Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’ “Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe, movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo masiku onse a moyo wako.
And to Adam he said (for *LA(bh)*) you listened to [the] voice of wife your and you ate from the tree which I commanded you saying not you must eat from it [is] cursed the ground for sake of you in pain you will eat it all [the] days of life your.
18 Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula ndipo udzadya zomera zakuthengo.
And thorn[s] and thistle[s] will cause to sprout for you and you will eat [the] vegetation of the field.
19 Kuti upeze chakudya udzayenera kukhetsa thukuta, mpaka utabwerera ku nthaka pakuti unachokera kumeneko; pakuti ndiwe fumbi ku fumbi komweko udzabwerera.”
By [the] sweat of face your you will eat food until return you to the ground for from it you were taken for [are] dust you and to dust you will return.
20 Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.
And he called the man [the] name of wife his Eve for she she was [the] mother of every living [person].
21 Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka.
And he made Yahweh God for Adam and for wife his garments of skin and he clothed them.
22 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.”
And he said - Yahweh God here! the man he has become like one of us by knowing good and evil and therefore - lest he should stretch out hand his and he will take also from [the] tree of life and he will eat and he will live for ever.
23 Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera.
And he sent out him Yahweh God from [the] garden of Eden to till the ground where he was taken from there.
24 Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.
And he drove out the man and he caused to dwell from east of [the] garden of Eden the cherubim and [the] flame of the sword whirling to guard [the] way of [the] tree of life.

< Genesis 3 >