< Genesis 3 >

1 Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’”
And the two were naked, both Adam and his wife, and were not ashamed. Now the serpent was the most crafty of all the brutes on the earth, which the Lord God made, and the serpent said to the woman, Therefore has God said, Eat not of every tree of the garden?
2 Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu,
And the woman said to the serpent, We may eat of the fruit of the trees of the garden,
3 koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’”
but of the fruit of the tree which is in the midst of the garden, God said, You shall not eat of it, neither shall you touch it, lest you die.
4 “Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo.
And the serpent said to the woman, You shall not surely die.
5 “Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”
For God knew that in whatever day you should eat of it your eyes would be opened, and you would be as gods, knowing good and evil.
6 Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso.
And the woman saw that the tree was good for food, and that it was pleasant to the eyes to look upon and beautiful to contemplate, and having taken of its fruit she ate, and she gave to her husband also with her, and they ate.
7 Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.
And the eyes of both were opened, and they perceived that they were naked, and they sewed fig leaves together, and made themselves aprons to go round them.
8 Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo.
And they heard the voice of the Lord God walking in the garden in the afternoon; and both Adam and his wife hid themselves from the face of the Lord God in the midst of the trees of the garden.
9 Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”
And the Lord God called Adam and said to him, Adam, where are you?
10 Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”
And he said to him, I heard your voice as you walked in the garden, and I feared because I was naked and I hid myself.
11 Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”
And God said to him, Who told you that you were naked, unless you have eaten of the tree concerning which I charged you of it alone not to eat?
12 Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”
And Adam said, The woman whom you gave to be with me—she gave me of the tree and I ate.
13 Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?” Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”
And the Lord God said to the woman, Why have you done this? And the woman said, The serpent deceived me and I ate.
14 Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi, “Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse ndi nyama zakuthengo zonse. Udzayenda chafufumimba ndipo udzadya fumbi masiku onse a moyo wako.
And the Lord God said to the serpent, Because you have done this you are cursed above all cattle and all the brutes of the earth, on your breast and belly you shall go, and you shall eat earth all the days of your life.
15 Ndipo ndidzayika chidani pakati pa iwe ndi mkaziyo, pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake; Iye adzaphwanya mutu wako ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”
And I will put enmity between you and the woman and between your seed and her seed, he shall watch against your head, and you shall watch against his heel.
16 Kwa mkaziyo Iye anati, “Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati; ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana. Udzakhumba mwamuna wako, ndipo adzakulamulira.”
And to the woman he said, I will greatly multiply your pains and your groanings; in pain you shall bring forth children, and your submission shall be to your husband, and he shall rule over you.
17 Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’ “Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe, movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo masiku onse a moyo wako.
And to Adam he said, Because you have listened to the voice of your wife, and eaten of the tree concerning which I charged you of it only not to eat—of that you have eaten, cursed [is] the ground in your labors, in pain shall you eat of it all the days of your life.
18 Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula ndipo udzadya zomera zakuthengo.
Thorns and thistles shall it bring forth to you, and you shall eat the herb of the field.
19 Kuti upeze chakudya udzayenera kukhetsa thukuta, mpaka utabwerera ku nthaka pakuti unachokera kumeneko; pakuti ndiwe fumbi ku fumbi komweko udzabwerera.”
In the sweat of your face shall you eat your bread until you return to the earth out of which you were taken, for earth you are and to earth you shall return.
20 Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.
And Adam called the name of his wife Life, because she was the mother of all living.
21 Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka.
And the Lord God made for Adam and his wife garments of skin, and clothed them.
22 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.”
And God said, Behold, Adam is become as one of us, to know good and evil, and now lest at any time he stretch forth his hand, and take of the tree of life and eat, and [so] he shall live forever—
23 Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera.
So the Lord God sent him forth out of the garden of Delight to cultivate the ground out of which he was taken.
24 Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.
And he cast out Adam and caused him to dwell over against the garden of Delight, and stationed the cherubs and the fiery sword that turns about to keep the way of the tree of life.

< Genesis 3 >