< Genesis 29 >

1 Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
И востав Иаков на нозе, иде в землю восточную к Лавану сыну Вафуила Сирина, брату же Ревекки матере Иаковли и Исавли.
2 Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
Узре же, и се, кладязь на поли: и бяху тамо три стада овец, почивающе при нем: от того бо кладязя напаяхуся стада. Камень же велий бяше над устием кладязя.
3 Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
И собирахуся тамо вся стада: и отваляху камень от устия кладязя и напаяху овцы: и паки полагаху камень на устии кладязя на месте своем.
4 Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
Рече же им Иаков: братия, откуду есте вы? Они же реша: от Харрана есмы.
5 Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
Рече же им: знаете ли Лавана сына Нахорова? Они же реша: знаем.
6 Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
Рече же им: здравствует ли? Они же реша: здравствует. И се, Рахиль дщи его идяше со овцами.
7 Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
И рече Иаков: еще есть дне много, не у час собирати скота: напоивше овцы, шедше пасите.
8 Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
Они же реша: не можем, дондеже соберутся вси пастуси и отвалят камень от устия кладязя, и напоим овцы.
9 Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
Еще ему глаголющу к ним, и се, Рахиль дщи Лаваня грядяше со овцами отца своего: она бо пасяше овцы отца своего.
10 Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
Бысть же яко узре Иаков Рахиль дщерь Лавана брата матере своея и овцы Лавана брата матере своея, и приступив Иаков отвали камень от устия кладязя:
11 Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
и напои овцы Лавана брата матере своея, и целова Иаков Рахиль, и возопив гласом своим, восплакася:
12 Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
и поведа Рахили, яко брат отца ея есть и яко сын Ревеккин есть. И текши поведа отцу своему по словесем сим.
13 Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
Бысть же яко услыша Лаван имя Иакова сына сестры своея, тече во сретение ему и объемь его лобза, и введе его в дом свой. И поведа Лавану вся словеса сия.
14 Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
И рече ему Лаван: от костей моих и от плоти моея еси ты. И бе с ним месяц дний.
15 Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
Рече же Лаван Иакову: понеже брат мой еси ты, да не поработаеши мне туне: повеждь ми, что мзда твоя есть?
16 Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
У Лавана же бесте две дщери: имя старейшей Лиа, имя же юнейшей Рахиль.
17 Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
Очи же Лиины болезненны: Рахиль же бе добра видом и красна взором зело.
18 Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
Возлюби же Иаков Рахиль. И рече: поработаю тебе седмь лет за Рахиль дщерь твою меншую.
19 Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
Рече же ему Лаван: лучше ми тебе дати ю, нежели иному отдати мужеви: со мною живи.
20 Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
И работа Иаков за Рахиль седмь лет: и быша пред ним яко малы дни, занеже любяше ю.
21 Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
Рече же Иаков Лавану: даждь ми жену мою, понеже совершишася дние, да вниду к ней.
22 Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
Собра же Лаван вся мужы места того, и сотвори брак.
23 Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
И бысть вечер, и поемь Лаван Лию дщерь свою, введе ко Иакову: и вниде к ней Иаков.
24 Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
Даде же Лаван Лии дщери своей Зелфу рабыню свою, ей в рабу.
25 Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
Бысть же заутра, и се, бяше Лиа, и рече Иаков Лавану: что сие сотворил ми еси? Не Рахили ли ради работах у тебе? Вскую же обидел мя еси?
26 Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
Отвеща же Лаван: несть тако в нашем месте вдати меншую прежде старейшия.
27 Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
Скончай убо седмины сея, и дам ти и сию за дело, еже делаеши у мене еще седмь лет другия.
28 Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
Сотвори же Иаков тако: и исполни седмины сея: и даде ему Лаван Рахиль дщерь свою ему в жену.
29 Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
Даде же Лаван Рахили дщери своей Валлу рабу свою, ей в рабу.
30 Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
И вниде (Иаков) к Рахили: возлюби же Рахиль паче, неже Лию: и работа ему седмь лет другия.
31 Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
Видев же Господь Бог, яко ненавидима бяше Лиа, отверзе ложесна ея: Рахиль же бяше неплоды.
32 Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
И зачат Лиа и роди сына Иакову: нарече же имя ему Рувим, глаголя: яко призре Господь на мое смирение и даде ми сына: ныне убо возлюбит мя муж мой.
33 Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
И зачат паки Лиа и роди сына втораго Иакову и рече: зане услыша Господь, яко ненавидима есмь, и придаде ми и сего. И нарече имя ему Симеон.
34 Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
И зачат еще и роди сына и рече: в нынешнее время у мене будет муж мой, родих бо ему три сыны. Сего ради нарече имя ему Левий.
35 Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.
И заченши еще роди сына и рече: ныне еще сие исповем Господу. Сего ради нарече имя ему Иуда, и преста раждати.

< Genesis 29 >