< Genesis 29 >

1 Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
Wtedy Jakub wyruszył w drogę i poszedł do ziemi ludów Wschodu.
2 Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
I spojrzał, a oto w polu studnia i trzy stada owiec leżących przy niej. Z tej studni pojono bowiem stada, a wielki kamień [przykrywał] wierzch tej studni.
3 Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
A gdy schodziły się wszystkie stada, odsuwano kamień z wierzchu studni i pojono owce. Potem znów zasuwano kamień na wierzch studni na jego miejsce.
4 Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
Jakub zapytał ich: Moi bracia, skąd jesteście? I odpowiedzieli: Jesteśmy z Charanu.
5 Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
Zapytał ich: Czy znacie Labana, syna Nachora? Odpowiedzieli: Znamy.
6 Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
Potem zapytał: Czy dobrze się miewa? A oni odpowiedzieli: Dobrze. Oto właśnie jego córka Rachela nadchodzi ze stadem.
7 Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
Wtedy powiedział: Oto jeszcze jest jasny dzień i nie czas zganiać stada. Napójcie owce i idźcie, popaście je.
8 Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
Oni odpowiedzieli: Nie możemy, dopóki nie zbiorą się wszystkie stada i nie odsuną kamienia z wierzchu studni. Wtedy napoimy stada.
9 Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
A gdy jeszcze tak z nimi rozmawiał, nadeszła Rachela z owcami swego ojca, bo [je] pasła.
10 Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
I gdy Jakub ujrzał Rachelę, córkę Labana, brata swej matki, z owcami Labana, brata swej matki, podszedł, odsunął kamień z wierzchu studni i napoił owce Labana, brata swojej matki.
11 Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
Potem Jakub pocałował Rachelę i głośno zapłakał.
12 Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
I Jakub powiedział Racheli, że jest bratem jej ojca i że jest synem Rebeki. Ona pobiegła więc i oznajmiła to swemu ojcu.
13 Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
A gdy Laban usłyszał wieść o Jakubie, synu swojej siostry, wybiegł mu naprzeciw, objął go, ucałował i zaprowadził do swego domu. A [on] opowiedział Labanowi o wszystkim.
14 Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
Wtedy Laban powiedział mu: Ty naprawdę [jesteś] z moich kości i z mojego ciała. I [Jakub] mieszkał u niego przez cały miesiąc.
15 Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
Potem Laban powiedział do Jakuba: Czyż dlatego, że jesteś moim bratem, będziesz mi służyć za darmo? Powiedz mi, jaka [ma być] twoja zapłata.
16 Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
A Laban miał dwie córki: starsza miała na imię Lea, młodsza zaś Rachela.
17 Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
Lea miała czułe oczy, Rachela zaś była piękna i miła dla oka.
18 Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
Jakub kochał Rachelę i powiedział: Będę ci służył siedem lat za twoją młodszą córkę Rachelę.
19 Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
Laban odpowiedział: Lepiej mi ją dać tobie niż innemu mężczyźnie. Zamieszkaj ze mną.
20 Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
I Jakub służył za Rachelę siedem lat, które wydawały mu się jak kilka dni, bo ją kochał.
21 Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
Potem Jakub powiedział do Labana: Daj mi moją żonę, bo wypełniły się moje dni, abym z nią obcował.
22 Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
Wtedy Laban zebrał wszystkich mężczyzn tego miejsca i wyprawił ucztę.
23 Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
A gdy nastał wieczór, wziął swoją córkę Leę i wprowadził ją do [Jakuba], a on obcował z nią.
24 Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
Laban dał też swoją służącą Zilpę swej córce Lei za służącą.
25 Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
Rano okazało się, że to była Lea. Powiedział więc do Labana: Cóż mi zrobiłeś? Czy nie za Rachelę ci służyłem? Dlaczego mnie oszukałeś?
26 Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
Laban odpowiedział: Nie ma u nas zwyczaju, aby młodszą wydawać za mąż przed starszą.
27 Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
Dopełnij jej tydzień, a dam ci i tę za służbę, którą mi odsłużysz drugie siedem lat.
28 Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
I Jakub tak zrobił, i dopełnił jej tydzień. Potem [Laban] dał mu swoją córkę Rachelę za żonę.
29 Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
Laban dał też swoją służącą Bilhę swej córce Racheli za służącą.
30 Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
Wtedy [Jakub] obcował też z Rachelą i kochał Rachelę bardziej niż Leę, [i] służył mu jeszcze drugie siedem lat.
31 Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
A gdy PAN widział, że Lea była znienawidzona, otworzył jej łono. Rachela zaś [była] bezpłodna.
32 Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
Lea poczęła więc i urodziła syna, i nadała mu imię Ruben. Powiedziała bowiem: PAN naprawdę wejrzał na moje utrapienie. Dlatego teraz mój mąż będzie mnie kochać.
33 Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
Gdy znów poczęła i urodziła syna, powiedziała: PAN usłyszał, że byłam znienawidzona. Dlatego dał mi także tego [syna]. I nadała mu imię Symeon.
34 Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
Potem znów poczęła i urodziła syna, i powiedziała: Tym razem mój mąż przywiąże się do mnie, bo urodziłam mu trzech synów. Dlatego nadała mu imię Lewi.
35 Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.
Gdy jeszcze raz poczęła i urodziła syna, powiedziała: Teraz już będę chwalić PANA. Dlatego nadała mu imię Juda. I przestała rodzić.

< Genesis 29 >