< Genesis 29 >

1 Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
Så gav Jakob sig atter på veien og drog til Østens barns land.
2 Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
Og da han så sig omkring, fikk han se en brønn på marken, og ved den lå det tre flokker småfe. for av denne brønn vannet de feet; men stenen som lå over brønnens åpning, var stor.
3 Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
Der samlet alle feflokkene sig, og gjæterne veltet stenen fra brønnens åpning og vannet småfeet, og så la de stenen tilbake på sitt sted, over brønnens åpning.
4 Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
Jakob spurte dem: Mine brødre, hvor er I fra? De svarte: Vi er fra Karan.
5 Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
Så spurte han dem: Kjenner I Laban, sønn til Nakor? De svarte: Ja, vi kjenner ham.
6 Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
Da spurte han dem: Står det vel til med ham? De svarte: Ja, det gjør det, og se, der kommer hans datter Rakel med småfeet.
7 Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
Da sa han: Det er jo ennu høi dag, det er ennu ikke tid til å samle buskapen; vann småfeet og gå avsted igjen og gjæt!
8 Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
Men de sa: Det kan vi ikke før alle feflokkene er samlet, og stenen blir veltet fra brønnens åpning; da vanner vi småfeet.
9 Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
Mens han ennu talte med dem, kom Rakel med sin fars småfe; for det var hun som gjætte.
10 Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
Og da Jakob så Rakel, sin morbror Labans datter, og så småfeet som hørte hans morbror til, gikk han frem og veltet stenen fra brønnens åpning og vannet sin morbror Labans småfe.
11 Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
Og Jakob kysset Rakel og brast i gråt.
12 Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
Og Jakob fortalte Rakel at han var hennes fars frende, og at han var sønn til Rebekka; da sprang hun avsted og fortalte det til sin far.
13 Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
Da nu Laban fikk høre om Jakob, sin søstersønn, løp han ham i møte og omfavnet ham og kysset ham og førte ham inn i sitt hus; og han fortalte Laban alt det som hadde hendt.
14 Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
Da sa Laban til ham: Sannelig, vi er av samme kjød og blod. Og han blev hos ham en måneds tid.
15 Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
Så sa Laban til Jakob: Skulde du tjene mig for intet, fordi om du er min frende? Si mig hvad du vil ha i lønn!
16 Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
Nu hadde Laban to døtre, den eldste hette Lea, og den yngste hette Rakel.
17 Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
Lea hadde matte øine; men Rakel var vakker av skapning og vakker å se til.
18 Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
Og Jakob hadde Rakel kjær; derfor sa han: Jeg vil tjene dig syv år for Rakel, din yngste datter.
19 Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
Laban svarte: Det er bedre at jeg gir henne til dig, enn at jeg gir henne til en annen mann; bli hos mig!
20 Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
Så tjente Jakob i syv år for Rakel; og disse år syntes han var nogen få dager, fordi han hadde henne kjær.
21 Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
Derefter sa Jakob til Laban: La mig nu få min hustru, for min tid er ute, og jeg vil gå inn til henne.
22 Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
Da samlet Laban alle menn der på stedet og gjorde et gjestebud.
23 Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
Og om aftenen tok han sin datter Lea og førte henne inn til ham, og han gikk inn til henne.
24 Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
Og Laban gav sin trælkvinne Silpa til sin datter Lea som trælkvinne.
25 Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
Men om morgenen - se, da var det Lea. Da sa han til Laban: Hvad er det du har gjort mot mig? Var det ikke for Rakel jeg tjente hos dig? Hvorfor har du sveket mig?
26 Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
Laban svarte: Det er ikke skikk her hos oss å gi den yngste bort før den eldste.
27 Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
La nu Leas bryllups-uke gå til ende, så vil vi også gi dig den andre, hvis du vil tjene hos mig i syv år til.
28 Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
Og Jakob gjorde så, og han lot bryllups-uken gå til ende. Da gav han ham sin datter Rakel til hustru.
29 Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
Og Laban gav sin trælkvinne Bilha til sin datter Rakel som trælkvinne.
30 Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
Så gikk han også inn til Rakel, og han holdt mere av Rakel enn av Lea. Siden tjente han ennu syv år til hos Laban.
31 Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
Da Herren så at Lea blev tilsidesatt, åpnet han hennes morsliv; men Rakel var barnløs.
32 Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
Og Lea blev fruktsommelig og fødte en sønn, og hun kalte ham Ruben; for hun sa: Herren har sett til mig i min ulykke; nu vil min mann elske mig.
33 Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
Og hun blev atter fruktsommelig og fødte en sønn og sa: Herren har hørt at jeg var tilsidesatt; derfor har han gitt mig også denne sønn. Så kalte hun ham Simeon.
34 Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
Og hun blev atter fruktsommelig og fødte en sønn og sa: Nu må vel endelig min mann holde sig til mig, for jeg har født ham tre sønner. Derfor kalte de ham Levi.
35 Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.
Og hun blev atter fruktsommelig og fødte en sønn og sa: Nu vil jeg prise Herren. Derfor kalte hun ham Juda. Så fikk hun ikke flere barn da.

< Genesis 29 >