< Genesis 29 >

1 Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
Puis Jacob se mit en chemin, et s'en alla au pays des Orientaux.
2 Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
Et il regarda; et voici, il vit un puits dans les champs, et là même trois troupeaux de brebis couchés auprès; car on y abreuvait les troupeaux. Et la pierre qui couvrait l'ouverture du puits était grande.
3 Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
Tous les troupeaux se rassemblaient là; alors on roulait la pierre de dessus l'ouverture du puits, et on abreuvait les troupeaux; ensuite on remettait la pierre à sa place, sur l'ouverture du puits.
4 Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
Et Jacob dit aux bergers: Mes frères, d'où êtes-vous? Et ils répondirent: Nous sommes de Charan.
5 Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
Et il leur dit: Connaissez-vous Laban, fils de Nachor? Et ils répondirent: Nous le connaissons.
6 Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
Il leur dit: Se porte-t-il bien? Ils lui répondirent: Il se porte bien; et voici Rachel, sa fille, qui vient avec le troupeau.
7 Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
Et il dit: Voici, il est encore grand jour; il n'est pas temps de rassembler le bétail; abreuvez les brebis, et allez les paître.
8 Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
Ils répondirent: Nous ne pouvons pas, jusqu'à ce que tous les troupeaux soient rassemblés; alors on roule la pierre de dessus l'ouverture du puits, et nous abreuvons les troupeaux.
9 Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
Comme il parlait encore avec eux, Rachel arriva avec le troupeau de son père; car elle était bergère.
10 Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
Et dès que Jacob vit Rachel, fille de Laban, frère de sa mère, et le troupeau de Laban, frère de sa mère, il s'approcha, roula la pierre de dessus l'ouverture du puits, et abreuva le troupeau de Laban, frère de sa mère.
11 Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
Et Jacob baisa Rachel; et, élevant la voix, il pleura.
12 Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
Et Jacob apprit à Rachel qu'il était parent de son père, et qu'il était fils de Rébecca; et elle courut le rapporter à son père.
13 Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
Et aussitôt que Laban entendit parler de Jacob, fils de sa sœur, il courut au-devant de lui, l'embrassa, et le baisa, et le fit venir dans sa maison; et il raconta à Laban toutes ces choses.
14 Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
Et Laban lui dit: Certainement, tu es mon os et ma chair; et il demeura avec lui un mois de temps.
15 Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
Puis Laban dit à Jacob: Parce que tu es mon frère, me serviras-tu pour rien? Dis-moi quel sera ton salaire.
16 Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
Or, Laban avait deux filles, dont l'aînée s'appelait Léa, et la plus jeune Rachel.
17 Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
Mais Léa avait les yeux délicats, et Rachel était belle de taille, et belle de visage.
18 Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
Et Jacob aimait Rachel; et il dit: Je te servirai sept ans pour Rachel, ta plus jeune fille.
19 Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
Et Laban répondit: Il vaut mieux que je te la donne que si je la donnais à un autre; demeure avec moi.
20 Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
Jacob servit donc sept ans pour Rachel; et ils ne lui semblèrent que quelques jours, parce qu'il l'aimait.
21 Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
Et Jacob dit à Laban: Donne-moi ma femme; car mon temps est accompli, et je viendrai vers elle.
22 Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
Alors Laban rassembla tous les gens du lieu, et fit un festin.
23 Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
Et le soir il prit Léa, sa fille, et l'amena à Jacob, qui vint vers elle.
24 Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
Et Laban donna sa servante Zilpa pour servante à Léa, sa fille.
25 Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
Et le matin, voici, c'était Léa; et Jacob dit à Laban: Qu'est-ce que tu m'as fait? N'est-ce pas pour Rachel que j'ai servi chez toi? Et pourquoi m'as-tu trompé?
26 Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
Laban répondit: On ne fait pas ainsi dans ce lieu, de donner la plus jeune avant l'aînée.
27 Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
Achève la semaine de celle-ci, et nous te donnerons aussi l'autre, pour le service que tu feras encore chez moi sept autres années.
28 Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
Et Jacob fit ainsi, il acheva la semaine de celle-ci; puis Laban lui donna pour femme Rachel, sa fille.
29 Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
Et Laban donna sa servante Bilha pour servante à Rachel, sa fille.
30 Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
Il vint donc aussi vers Rachel, et il aima Rachel plus que Léa, et il servit chez Laban encore sept autres années.
31 Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
Et l'Éternel, voyant que Léa était haïe, la rendit féconde; mais Rachel était stérile.
32 Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
Et Léa conçut et enfanta un fils, qu'elle appela Ruben (voyez un fils! ). Car elle dit: L'Éternel a regardé mon affliction; maintenant mon mari m'aimera.
33 Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
Elle conçut encore, et enfanta un fils, et dit: L'Éternel a entendu que j'étais haïe, et il m'a encore donné celui-ci; et elle l'appela Siméon (exaucement).
34 Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
Elle conçut encore, et enfanta un fils, et dit: Pour cette fois, mon mari s'attachera à moi; car je lui ai enfanté trois fils; c'est pourquoi on l'appela Lévi (attachement).
35 Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.
Elle conçut encore et enfanta un fils, et dit: Cette fois je louerai l'Éternel; c'est pourquoi elle l'appela Juda (louange). Et elle cessa d'avoir des enfants.

< Genesis 29 >