< Genesis 29 >

1 Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
And he lifted up Jacob feet his and he went [the] land of towards [the] people of [the] east.
2 Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
And he saw and there! a well [was] in the field and there! there three flocks of sheep [were] lying down at it for from the well that people watered the flocks and the stone [was] large over [the] mouth of the well.
3 Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
And they were gathered there towards all the flocks and they rolled the stone from over [the] mouth of the well and they watered the sheep and they put back the stone over [the] mouth of the well to place its.
4 Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
And he said to them Jacob O brothers my from where? [are] you and they said [are] from Haran we.
5 Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
And he said to them ¿ do you know Laban [the] son of Nahor and they said we know [him].
6 Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
And he said to them ¿ [does] health [belong] to him and they said health and there! Rachel daughter his [is] coming with the sheep.
7 Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
And he said here! still the day [is] great not [the] time of [the] being gathered of the livestock water the sheep and go pasture [them].
8 Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
And they said not we are able until that they will be gathered all the flocks and people will roll the stone from over [the] mouth of the well and we will water the sheep.
9 Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
Still [was] he speaking with them and Rachel - she came with the sheep which [belonged] to father her for [was] a shepherdess she.
10 Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
And it was just as he saw Jacob Rachel [the] daughter of Laban [the] brother of mother his and [the] sheep of Laban [the] brother of mother his and he drew near Jacob and he rolled the stone from over [the] mouth of the well and he watered [the] sheep of Laban [the] brother of mother his.
11 Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
And he kissed Jacob Rachel and he lifted up voice his and he wept.
12 Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
And he told Jacob to Rachel that [was] [the] relative of father her he and that [was] [the] son of Rebekah he and she ran and she told to father her.
13 Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
And it was when heard Laban [the] report of - Jacob [the] son of sister his and he ran to meet him and he embraced him and he kissed him and he brought him to house his and he recounted to Laban all the things these.
14 Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
And he said to him Laban surely [are] bone my and flesh my you and he remained with him a month of days.
15 Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
And he said Laban to Jacob ¿ for relative my [are] you and you will serve me for nothing tell! to me what? [is] wage[s] your.
16 Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
And [belonged] to Laban two daughters [the] name of the old [one] [was] Leah and [the] name of the young [one] [was] Rachel.
17 Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
And [the] eyes of Leah [were] weak and Rachel she was beautiful of form and beautiful of appearance.
18 Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
And he loved Jacob Rachel and he said I will serve you seven years for Rachel daughter your young.
19 Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
And he said Laban ([is] good *LB(ah)*) to give I her to you more than to give I her to a man another remain! with me.
20 Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
And he served Jacob for Rachel seven years and they were in view his like days one in love his her.
21 Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
And he said Jacob to Laban give! wife my for they have been completed days my so I may go into her.
22 Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
And he gathered Laban all [the] people of the place and he prepared a feast.
23 Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
And it was in the evening and he took Leah daughter his and he brought her to him and he went into her.
24 Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
And he had given Laban to her Zilpah maidservant his to Leah daughter his a maidservant.
25 Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
And it was in the morning and there! she [was] Leah and he said to Laban what? this have you done to me ¿ not for Rachel have I served with you and why? have you deceived me.
26 Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
And he said Laban not it is done thus in place our to give the young before the firstborn.
27 Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
Complete [the] week of this [one] so let us give to you also this [one] for [the] service which you will serve with me again seven years another.
28 Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
And he did Jacob thus and he completed [the] week of this [one] and he gave to him Rachel daughter his of him to a wife.
29 Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
And he had given Laban to Rachel daughter his Bilhah maidservant his to her to [be] a maidservant.
30 Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
And he went also into Rachel and he loved also Rachel more than Leah and he served with him again seven years another.
31 Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
And he saw Yahweh that [was] hated Leah and he opened womb her and Rachel [was] barren.
32 Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
And she conceived Leah and she bore a son and she called name his Reuben for she said that he has looked Yahweh on affliction my for now he will love me husband my.
33 Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
And she conceived again and she bore a son and she said that he has heard Yahweh that [am] hated I and he has given to me also this [one] and she called name his Simeon.
34 Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
And she conceived again and she bore a son and she said now this time he will join himself husband my to me for I have borne to him three sons there-fore he called name his Levi.
35 Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.
And she conceived again and she bore a son and she said this time I will praise Yahweh there-fore she called name his Judah and she stopped from bearing children.

< Genesis 29 >