< Genesis 28 >

1 Choncho Isake anayitanitsa Yakobo namudalitsa nʼkumuwuzitsa kuti, “Usakwatire mkazi wa kuno ku Kanaani.
UIsaka wasebiza uJakobe, wambusisa, wamlaya wathi kuye: Ungathathi umfazi kumadodakazi eKhanani.
2 Panopo upite ku Padanaramu, ku nyumba kwa Betueli abambo a amayi akowa, kumeneko ukakwatire mmodzi mwa ana aakazi a Labani, mlongo wa amayi akowa.
Sukuma uye ePadani-Arama, endlini kaBethuweli uyise kanyoko, uzithathele khona umfazi kumadodakazi kaLabani umalumakho.
3 Mulungu Wamphamvuzonse akudalitse iwe nakupatse ana ambiri mpaka udzasanduke gulu lalikulu la mitundu ya anthu.
Njalo uNkulunkulu uSomandla akubusise, akwenze ube lenzalo akwandise, ukuze ube ngumbuthano wezizwe;
4 Mulunguyo akudalitse iwe monga mmene anamudalitsira Abrahamu kuti zidzukulu zako zidzalandira dziko limene ukukhalamo ngati mlendo kuti lidzakhale lawo. Ili ndi dziko limene Mulungu anapereka kwa Abrahamu.”
abesekupha isibusiso sikaAbrahama, kuwe lenzalweni yakho kanye lawe, ukuze udle ilifa lelizwe lapho ohlala khona njengowezizwe, uNkulunkulu alinika uAbrahama.
5 Ndipo Isake anamulola Yakobo kuti anyamuke kupita ku Padanaramu kwa Labani mwana wa Betueli Mwaramu. Labani anali mlongo wa Rebeka, mayi wa Yakobo ndi Esau.
UIsaka wasethuma uJakobe waya ePadani-Arama kuLabani indodana kaBethuweli umSiriya, umfowabo kaRebeka unina kaJakobe loEsawu.
6 Tsopano Esau anadziwa kuti Isake anadalitsa Yakobo ndi kumutumiza ku Padanaramu kuti akakwatire kumeneko. Anawuzidwanso kuti, “Usakwatire mkazi wa ku Kanaani.”
UEsawu wasebona ukuthi uIsaka umbusisile uJakobe, wamthuma ePadani-Arama ukuze azithathele khona umfazi, lapho embusisa wamlaya esithi: Ungathathi umfazi kumadodakazi eKhanani;
7 Yakobo anamvera abambo ake ndi amayi ake ndi kupita ku Padanaramu.
lokuthi uJakobe walalela oyise lonina, waya ePadani-Arama.
8 Ndiye pamenepo Esau anazindikira kuti abambo ake Isake sankakondwera ndi akazi a ku Kanaani;
UEsawu wasebona ukuthi amadodakazi eKhanani ayemabi emehlweni kaIsaka uyise.
9 anapita kwa Ismaeli mwana wa Abrahamu nakwatira Mahalati mwana wa Ismaeli, mlongo wake wa Nebayoti. Anatero kuwonjezera akazi amene anali nawo kale.
Ngakho uEsawu waya kuIshmayeli, wazithathela uMahalathi indodakazi kaIshmayeli, indodana kaAbrahama, udadewabo kaNebayothi, abe ngumkakhe phezu kwabafazi ayelabo.
10 Yakobo ananyamuka pa ulendo kuchoka ku Beeriseba kupita ku Harani.
UJakobe wasephuma eBherishebha waya eHarani.
11 Atafika pa malo pena, anayima kuti agonepo chifukwa dzuwa linali litalowa. Anatenga mwala wina pomwepo natsamiritsapo mutu wake, ndipo anagona.
Wafika endaweni, achitha khona ubusuku ngoba ilanga lalitshonile. Wasethatha ilitshe ematsheni aleyondawo, wenza umqamelo wakhe, walala kuleyondawo.
12 Mʼmaloto, anaona makwerero oyimikidwa pansi ndipo anakafika kumwamba. Angelo a Mulungu amakwera ndi kutsika pa makwereropo.
Waphupha, khangela-ke, ilele limisiwe emhlabeni, isihloko salo sifinyelela emazulwini, khangela-ke, ingilosi zikaNkulunkulu zisenyuka zisehla kulo.
13 Tsono Yehova anayimirira pambali pake, nati, “Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu kholo lake la Isake abambo ako. Ndidzakupatsa iwe ndi zidzukulu zako dziko limene ukugonamolo.
Khangela-ke, iNkosi yema phezu kwalo, yathi: NgiyiNkosi uNkulunkulu kaAbrahama uyihlo loNkulunkulu kaIsaka; ilizwe olele kulo, ngizakunika lona, lenzalo yakho;
14 Zidzukulu zako zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi ndipo zidzabalalikira kumadzulo ndi kummawa, kumpoto ndi kummwera. Anthu onse adzalandira madalitso kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako.
njalo inzalo yakho izakuba ngangothuli lomhlaba, uzasabalalela entshonalanga lempumalanga lenyakatho leningizimu; njalo zizabusiswa kuwe zonke insendo zomhlaba, lasenzalweni yakho.
15 Ine ndili nawe pamodzi ndipo ndidzakuyangʼanira kulikonse upiteko, ndipo ndidzakubwezera ku dziko lino. Sindidzakusiya mpaka nditachita zimene ndakulonjezazi.”
Khangela-ke, ngilawe, ngizakulondoloza kuzo zonke indawo lapha oya khona, ngikubuyise kulelilizwe; ngoba kangiyikukutshiya ngize ngikwenze lokho engikhulume ngakho kuwe.
16 Yakobo atadzidzimuka, anati, “Zoonadi Yehova ali pa malo ano, ndipo ine sindinadziwe.”
Kwathi uJakobe ephaphama ebuthongweni bakhe, wathi: Isibili iNkosi ikulindawo, mina-ke bengingakwazi.
17 Tsono anachita mantha ndipo anati, “Malo ano ndi woopsa ndithu. Zoonadi pano ndi pa nyumba ya Mulungu ndi khomo la kumwamba.”
Wasesesaba wathi: Yesabeka kangakanani lindawo! Kayisilutho ngaphandle kokuthi yindlu kaNkulunkulu, laleli lisango lamazulu.
18 Mmamawa mwake Yakobo anatenga mwala umene anatsamira mutu wake uja nawuyimika ngati chipilala ndi kuthira mafuta pamwamba pake
UJakobe wasevuka ekuseni kakhulu, wathatha ilitshe alenza laba ngumqamelo wakhe, walimisa laba yinsika, wathela amagcobo phezu kwesihloko salo.
19 Iye anawatcha malowo Beteli, ngakhale kuti poyamba mzindawo ankawutcha Luzi.
Wasebiza ibizo laleyondawo iBhetheli; kodwa-ke kuqala ibizo lomuzi laliyiLuzi.
20 Pamenepo Yakobo analumbira kwa Yehova nati, “Ngati inu Mulungu mukhala ndi ine, kundiyangʼanira pa ulendo wangawu ndi kundipatsa chakudya ndi chovala;
UJakobe wasethembisa isithembiso esithi: Uba uNkulunkulu ezakuba lami, angilondoloze kulindlela engiyihambayo, angiphe isinkwa sokudla, lesembatho sokwembatha,
21 ngati inu mudzandibweretsa kwathu mu mtendere, ndiye kuti mudzakhala Mulungu wanga,
njalo ngibuyele ngokuthula endlini kababa, khona iNkosi izakuba nguNkulunkulu wami,
22 ndipo mwala uwu ndawuyimikawu udzakhala Nyumba ya Mulungu. Ine ndidzakupatsani chakhumi cha zinthu zonse zimene mudzandipatse.”
lelitshe leli engilimise ukuthi libe yinsika lizakuba yindlu kaNkulunkulu; kukho konke ozangipha khona, isibili ngizakunika okwetshumi.

< Genesis 28 >