< Genesis 28 >

1 Choncho Isake anayitanitsa Yakobo namudalitsa nʼkumuwuzitsa kuti, “Usakwatire mkazi wa kuno ku Kanaani.
Than Isaac called Iacob his sonne and blessed him ad charged him and sayde vnto him: se thou take not a wife of the doughters of Canaan
2 Panopo upite ku Padanaramu, ku nyumba kwa Betueli abambo a amayi akowa, kumeneko ukakwatire mmodzi mwa ana aakazi a Labani, mlongo wa amayi akowa.
but aryse ad gett the to Mesopotamia to the house of Bethuel thy mothers father: and there take the a wife of the doughters of Laban thi mothers brother.
3 Mulungu Wamphamvuzonse akudalitse iwe nakupatse ana ambiri mpaka udzasanduke gulu lalikulu la mitundu ya anthu.
And God allmightie blesse the increase the and multiplie the that thou mayst be a nombre of people
4 Mulunguyo akudalitse iwe monga mmene anamudalitsira Abrahamu kuti zidzukulu zako zidzalandira dziko limene ukukhalamo ngati mlendo kuti lidzakhale lawo. Ili ndi dziko limene Mulungu anapereka kwa Abrahamu.”
and geue the the blessynge of Abraham: both to the and to thy seed with the that thou mayst possesse the lade (wherein thou art a strangere) which God gaue vnto Abraham.
5 Ndipo Isake anamulola Yakobo kuti anyamuke kupita ku Padanaramu kwa Labani mwana wa Betueli Mwaramu. Labani anali mlongo wa Rebeka, mayi wa Yakobo ndi Esau.
Thus Isaac sent forth Iacob to goo to Mesopotamia vnto Laban sonne of Bethuel the Sirien and brother to Rebecca Iacobs and Esaus mother.
6 Tsopano Esau anadziwa kuti Isake anadalitsa Yakobo ndi kumutumiza ku Padanaramu kuti akakwatire kumeneko. Anawuzidwanso kuti, “Usakwatire mkazi wa ku Kanaani.”
When Esau sawe that Isaac had blessed Iacob and sent him to Mesopotamia to fett him a wife thence and that as he blessed him he gaue him a charge saynge: se thou take not a wife of the doughters of Canaan:
7 Yakobo anamvera abambo ake ndi amayi ake ndi kupita ku Padanaramu.
and that Iacob had obeyed his father and mother and was gone vnto Mesopotamia:
8 Ndiye pamenepo Esau anazindikira kuti abambo ake Isake sankakondwera ndi akazi a ku Kanaani;
and seynge also that the doughters of Canaan pleased not Isaac his father:
9 anapita kwa Ismaeli mwana wa Abrahamu nakwatira Mahalati mwana wa Ismaeli, mlongo wake wa Nebayoti. Anatero kuwonjezera akazi amene anali nawo kale.
Then went he vnto Ismael and toke vnto the wiues which he had Mahala the doughter of Ismael Abrahams sonne the sister of Nabaioth to be his wife.
10 Yakobo ananyamuka pa ulendo kuchoka ku Beeriseba kupita ku Harani.
Iacob departed from Berseba and went toward Haran
11 Atafika pa malo pena, anayima kuti agonepo chifukwa dzuwa linali litalowa. Anatenga mwala wina pomwepo natsamiritsapo mutu wake, ndipo anagona.
and came vnto a place and taried there all nyghte because the sonne was downe. And toke a stone of the place and put it vnder his heade and layde him downe in the same place to slepe.
12 Mʼmaloto, anaona makwerero oyimikidwa pansi ndipo anakafika kumwamba. Angelo a Mulungu amakwera ndi kutsika pa makwereropo.
And he dreamed: and beholde there stode a ladder apon the erth and the topp of it reached vpp to heaue. And se the angells of God went vp and downe apon it
13 Tsono Yehova anayimirira pambali pake, nati, “Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu kholo lake la Isake abambo ako. Ndidzakupatsa iwe ndi zidzukulu zako dziko limene ukugonamolo.
yee ad the LORde stode apon it and sayde. I am the LORde God of Abraham thi father and the God of Isaac: The londe which thou slepest apon will I geue the and thy seed.
14 Zidzukulu zako zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi ndipo zidzabalalikira kumadzulo ndi kummawa, kumpoto ndi kummwera. Anthu onse adzalandira madalitso kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako.
And thy seed shalbe as the dust of the erth: And thou shalt spreade abrode: west east north and south. And thorow the and thy seed shall all the kynreddes of the erth be blessed.
15 Ine ndili nawe pamodzi ndipo ndidzakuyangʼanira kulikonse upiteko, ndipo ndidzakubwezera ku dziko lino. Sindidzakusiya mpaka nditachita zimene ndakulonjezazi.”
And se I am with the and wylbe thy keper in all places whother thou goost and wyll brynge ye agayne in to this lande: Nether will I leaue the vntill I haue made good all that I haue promysed the.
16 Yakobo atadzidzimuka, anati, “Zoonadi Yehova ali pa malo ano, ndipo ine sindinadziwe.”
When Iacob was awaked out of his slepe he sayde: surely the LORde is in this place ad I was not aware.
17 Tsono anachita mantha ndipo anati, “Malo ano ndi woopsa ndithu. Zoonadi pano ndi pa nyumba ya Mulungu ndi khomo la kumwamba.”
And he was afrayde and sayde how fearfull is this place? it is none other but euen the house of God and the gate of heaue.
18 Mmamawa mwake Yakobo anatenga mwala umene anatsamira mutu wake uja nawuyimika ngati chipilala ndi kuthira mafuta pamwamba pake
And Iacob stode vp early in the mornynge and toke the stone that he had layde vnder his heade and pitched it vp an ende and poured oyle on the topp of it.
19 Iye anawatcha malowo Beteli, ngakhale kuti poyamba mzindawo ankawutcha Luzi.
And he called the name of the place Bethell for in dede the name of the citie was called Lus before tyme.
20 Pamenepo Yakobo analumbira kwa Yehova nati, “Ngati inu Mulungu mukhala ndi ine, kundiyangʼanira pa ulendo wangawu ndi kundipatsa chakudya ndi chovala;
And Iacob vowed a vowe saynge: Yf God will be with me and wyll kepe me in this iourney which I goo and will geue me bread to eate and cloothes to put on
21 ngati inu mudzandibweretsa kwathu mu mtendere, ndiye kuti mudzakhala Mulungu wanga,
so that I come agayne vnto my fathers house in saftie: then shall the LORde be my God
22 ndipo mwala uwu ndawuyimikawu udzakhala Nyumba ya Mulungu. Ine ndidzakupatsani chakhumi cha zinthu zonse zimene mudzandipatse.”
and this stone which I haue sett vp an ende shalbe godes house And of all that thou shalt geue me will I geue the tenth vnto the.

< Genesis 28 >