< Genesis 27 >

1 Isake atakalamba maso ake anachita khungu mwakuti sankatha kuona. Iye anayitana mwana wake wamkulu Esau nati kwa iye, “Mwana wanga.” Iye anayankha, “Ine abambo.”
and to be for be old Isaac and to grow dim eye his from to see: see and to call: call to [obj] Esau son: child his [the] great: old and to say to(wards) him son: child my and to say to(wards) him behold I
2 Isake anati, “Tsopano ine ndakalamba, ndipo sindidziwa tsiku langa lakufa.
and to say behold please be old not to know day death my
3 Tsono tenga zida zako, muvi wako ndi uta, pita kuthengo ukandiphere nyama.
and now to lift: raise please article/utensil your quiver your and bow your and to come out: come [the] land: country and to hunt [emph?] to/for me (wild game *Q(K)*)
4 Undikonzere chakudya chabwino monga muja ndimakonderamu ndipo ubwere nacho kwa ine kuti ndidye ndi kuti ndikudalitse ndisanamwalire.”
and to make to/for me delicacy like/as as which to love: lover and to come (in): bring [emph?] to/for me and to eat in/on/with for the sake of to bless you soul: myself my in/on/with before to die
5 Koma Rebeka amamvetsera pamene Isake amayankhula ndi mwana wake Esau. Esau atanyamuka kupita kuthengo kukaphera abambo ake nyama,
and Rebekah to hear: hear in/on/with to speak: speak Isaac to(wards) Esau son: child his and to go: went Esau [the] land: country to/for to hunt wild game to/for to come (in): bring
6 Rebeka anati kwa mwana wake Yakobo, “Taona ndamva abambo ako akuwuza mʼbale wako Esau kuti,
and Rebekah to say to(wards) Jacob son: child her to/for to say behold to hear: hear [obj] father your to speak: speak to(wards) Esau brother: male-sibling your to/for to say
7 ‘Bweretsere nyama yakutchire ndipo undikonzere chakudya chokoma kuti ndidye; kuti ndikudalitse pamaso pa Yehova ndisanamwalire.’
to come (in): bring [emph?] to/for me wild game and to make to/for me delicacy and to eat and to bless you to/for face: before LORD to/for face: before death my
8 Tsopano mwana wanga, mvetsetsa ndipo uchite zimene ndikuwuze:
and now son: child my to hear: obey in/on/with voice my to/for which I to command [obj] you
9 Pita ku khola, ukatenge ana ambuzi abwino awiri, kuti ndikonzere abambo ako chakudya chokoma monga amakondera.
to go: went please to(wards) [the] flock and to take: bring to/for me from there two kid goat pleasant and to make [obj] them delicacy to/for father your like/as as which to love: lover
10 Kenaka upite nacho chakudyacho kwa abambo ako kuti adye ndi kukudalitsa asanafe.”
and to come (in): bring to/for father your and to eat in/on/with for the sake of which to bless you to/for face: before death his
11 Koma Yakobo anati kwa Rebeka amayi ake, “Komatu mʼbale wanga Esau ndi munthu wa khungu la ubweya zedi, ndipo ine ndine munthu wa khungu losalala.
and to say Jacob to(wards) Rebekah mother his look! Esau brother: male-sibling my man hairy and I man smooth
12 Mwina abambo anga adzandikhudza, ndipo ndidzaoneka kuti ndawapusitsa. Tsono ndizadzitengera temberero mʼmalo mwa madalitso.”
perhaps to feel me father my and to be in/on/with eye: appearance his like/as to mock and to come (in): bring upon me curse and not blessing
13 Amayi ake anati kwa iye, “Mwana wanga, temberero limenelo ligwere ine. Iwe ungochita zimene ine ndikukuwuza; pita kanditengere timbuzito.”
and to say to/for him mother his upon me curse your son: child my surely to hear: obey in/on/with voice my and to go: went to take: bring to/for me
14 Choncho anapita nakatenga timbuzito ndi kubwera nato kwa amayi ake. Choncho Rebeka anaphika chakudya chokoma monga momwe Isake amakondera.
and to go: went and to take: take and to come (in): bring to/for mother his and to make mother his delicacy like/as as which to love: lover father his
15 Tsono Rebeka anatenga zovala zabwino kwambiri za Esau mwana wake wamkulu zimene zinali mʼnyumba namuveka Yakobo.
and to take: take Rebekah [obj] garment Esau son: child her [the] great: old [the] desirable thing which with her in/on/with house: home and to clothe [obj] Jacob son: child her [the] small
16 Anamuvekanso manja ake ndi khosi lake ndi zikopa za mwana wambuzi.
and [obj] skin kid [the] goat to clothe upon hand his and upon smoothness neck his
17 Kenaka, anamupatsa Yakobo chakudya chokoma chija chimene anaphika pamodzi ndi buledi.
and to give: put [obj] [the] delicacy and [obj] [the] food: bread which to make in/on/with hand: power Jacob son: child her
18 Yakobo anapita kwa abambo ake ndipo anati, “Abambo anga.” Ndipo anayankha, “Eya, kodi ndiwe mwana wanga uti?”
and to come (in): come to(wards) father his and to say father my and to say behold I who? you(m. s.) son: child my
19 Yakobo anati kwa abambo ake, “Ndine Esau mwana wanu woyamba. Ndachita monga munandiwuzira. Chonde dzukani ndi kukhala tsonga kuti mudyeko nyama ndakukonzeraniyi kuti tsono mundidalitse.”
and to say Jacob to(wards) father his I Esau firstborn your to make: do like/as as which to speak: speak to(wards) me to arise: rise please to dwell [emph?] and to eat [emph?] from wild game my in/on/with for the sake of to bless me soul: myself your
20 Isake anafunsa mwana wake, “Wayipeza msanga chotere bwanji mwana wanga?” Iye anayankha, “Yehova Mulungu wanu anandithandiza kuti ndiyipeze.”
and to say Isaac to(wards) son: child his what? this to hasten to/for to find son: child my and to say for to meet LORD God your to/for face of my
21 Pamenepo Isake anati kwa Yakobo, “Tabwera pafupi ndikukhudze mwana wanga, kuti ndidziwedi ngati uli mwana wanga Esau kapena ayi.”
and to say Isaac to(wards) Jacob to approach: approach [emph?] please and to feel you son: child my you(m. s.) this son: child my Esau if not
22 Yakobo anasendera kufupi ndi abambo ake Isake ndipo anamukhudza nati, “Mawuwa ndi mawu a Yakobo koma mikonoyi ndi mikono ya Esau.”
and to approach: approach Jacob to(wards) Isaac father his and to feel him and to say [the] voice voice Jacob and [the] hand hand Esau
23 Sanamuzindikire, popeza mikono yake inali ndi ubweya ngati ya mʼbale wake Esau; choncho anamudalitsa.
and not to recognize him for to be hand his like/as hand Esau brother: male-sibling his hairy and to bless him
24 Isake anafunsa, “Kodi ndiwedi mwana wanga Esau?” Yakobo anayankha, “Inde ndine.”
and to say you(m. s.) this son: child my Esau and to say I
25 Ndipo iye anati, “Mwana wanga, patseko nyama yakoyo ndidye kuti ndikudalitse.” Yakobo anabwera ndi nyama ija kwa Isake ndipo anadya. Kenaka anamupatsanso vinyo ndipo anamwa.
and to say to approach: bring [emph?] to/for me and to eat from wild game son: child my because to bless you soul: myself my and to approach: bring to/for him and to eat and to come (in): bring to/for him wine and to drink
26 Tsono Isake anati kwa Yakobo, “Bwera kuno mwana wanga undipsompsone.”
and to say to(wards) him Isaac father his to approach: approach [emph?] please and to kiss [emph?] to/for me son: child my
27 Choncho anapita namupsompsona. Apa Isake anamva fungo la zovala zake, ndipo anamudalitsa nati, “Haa, fungo la mwana wanga lili ngati fungo la munda umene Yehova waudalitsa.
and to approach: approach and to kiss to/for him and to smell [obj] aroma garment his and to bless him and to say to see: see aroma son: child my like/as aroma land: country which to bless him LORD
28 Mulungu akugwetsere mame akumwamba ndipo minda yako ibale tirigu wambiri ndi vinyo watsopano.
and to give: give to/for you [the] God from dew [the] heaven and from fat [the] land: soil and abundance grain and new wine
29 Mitundu ya anthu ikutumikire iwe ndipo anthu akugwadire iwe. Ukhale wolamula abale ako, ndipo ana aamuna a amayi ako akugwadire. Amene akutemberera iwe atembereredwe ndipo amene adalitsa iwe adalitsike.”
to serve you people (and to bow *Q(K)*) to/for you people to be lord to/for brother: male-sibling your and to bow to/for you son: child mother your to curse you to curse and to bless you to bless
30 Isake atatsiriza kudalitsa Yakobo, atangochoka pamaso pa abambo akewo, Esau anabwera kuchokera kosaka kuja.
and to be like/as as which to end: finish Isaac to/for to bless [obj] Jacob and to be surely to come out: come to come out: come Jacob from with face Isaac father his and Esau brother: male-sibling his to come (in): come from wild game his
31 Nayenso anakonza chakudya chokoma nabwera nacho kwa abambo ake. Ndipo anati kwa iye, “Chonde abambo, dzukani mukhale tsonga kuti mudye nyamayi ndi kuti mundidalitse.”
and to make also he/she/it delicacy and to come (in): bring to/for father his and to say to/for father his to arise: rise father my and to eat from wild game son: child his in/on/with for the sake of to bless me soul: myself your
32 Abambo ake, Isake, anamufunsa kuti, “Ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine mwana wanu woyamba Esau.”
and to say to/for him Isaac father his who? you(m. s.) and to say I son: child your firstborn your Esau
33 Isake ananjenjemera kwambiri nati, “Nanga ndani uja anakapha nyama kutchire nʼkudzandipatsa? Ine ndadya kale, ndadya nyamayo iwe utangotsala pangʼono kubwera ndipo ndamudalitsa ndipo adzakhaladi wodalitsika.”
and to tremble Isaac trembling great: large till much and to say who? then he/she/it [the] to hunt wild game and to come (in): bring to/for me and to eat from all in/on/with before to come (in): come and to bless him also to bless to be
34 Esau atamva mawu a abambo ake, analira mokweza ndi mowawidwa mtima nati kwa abambo ake, “Inenso dalitseni abambo anga!”
like/as to hear: hear Esau [obj] word father his and to cry cry great: large and bitter till much and to say to/for father his to bless me also I father my
35 Koma iye anati, “Mʼbale wako anabwera mwachinyengo ndipo watenga madalitso ako.”
and to say to come (in): come brother: male-sibling your in/on/with deceit and to take: take blessing your
36 Esau anati, “Kodi nʼchifukwa chake iyeyu dzina lake lili Yakobo eti? Aka nʼkachiwiri kundinyenga: Anatenga ukulu wanga, pano watenga madalitso anga!” Kenaka anafunsa, “Kodi simunandisungireko ena madalitsowo?”
and to say for to call: call by name his Jacob and to assail me this beat [obj] birthright my to take: take and behold now to take: take blessing my and to say not to reserve to/for me blessing
37 Koma Isake anamuyankha nati, “Ndamudalitsa iye kuti akhale wokulamulira iwe. Ndaperekanso abale ake onse kuti akhale omutumikira iye, ndipo ndamudalitsa ndi tirigu wambiri, ndi vinyo watsopano. Ndiye ndingakuchitirenso chiyani mwana wanga?”
and to answer Isaac and to say to/for Esau look! lord to set: make him to/for you and [obj] all brother: male-sibling his to give: give to/for him to/for servant/slave and grain and new wine to support him and to/for you then what? to make: do son: child my
38 Esau anati kwa abambo ake, “Kodi muli ndi dalitso limodzi lokhali, abambo anga? Inenso mundidalitse chonde abambo anga!” Pomwepo Esau analira mokuwa.
and to say Esau to(wards) father his blessing one he/she/it to/for you father my to bless me also I father my and to lift: loud Esau voice his and to weep
39 Tsono Isake abambo ake anamuyankha kuti, “Malo ako okhalapo sadzabala dzinthu, ndipo mvula sidzagwa pa minda yako.
and to answer Isaac father his and to say to(wards) him behold from fat [the] land: soil to be seat your and from dew [the] heaven from upon
40 Udzakhala ndi moyo podalira lupanga ndipo udzatumikira mʼbale wako. Koma idzafika nthawi pamene udzakhala mfulu udzachotsa goli lake mʼkhosi mwako.”
and upon sword your to live and [obj] brother: male-sibling your to serve and to be like/as as which to roam and to tear yoke his from upon neck your
41 Ndipo Esau anamusungira chiwembu Yakobo chifukwa cha madalitso amene abambo ake anamupatsa. Esau anati kwa iye yekha, “Masiku olira abambo anga ayandikira; pambuyo pake ndidzamupha mʼbale wangayu Yakobo.”
and to hate Esau [obj] Jacob upon [the] blessing which to bless him father his and to say Esau in/on/with heart his to present: come day mourning father my and to kill [obj] Jacob brother: male-sibling my
42 Pamene Rebeka anamva zimene mwana wake wamkulu Esau ankaganiza, anayitanitsa Yakobo nati kwa iye, “Mʼbale wako Esau akulingalira zakuti akuphe kuti akulipsire.
and to tell to/for Rebekah [obj] word Esau son: child her [the] great: old and to send: depart and to call: call to to/for Jacob son: child her [the] small and to say to(wards) him behold Esau brother: male-sibling your to be sorry: comfort to/for you to/for to kill you
43 Tsopano mwana wanga, chita zimene ndinene: Nyamuka tsopano, uthawire kwa mlongo wanga Labani ku Harani.
and now son: child my to hear: obey in/on/with voice my and to arise: rise to flee to/for you to(wards) Laban brother: male-sibling my Haran [to]
44 Ukakhale naye kwa kanthawi mpaka mkwiyo wa mʼbale wako utatsika.
and to dwell with him day one till which to return: turn back rage brother: male-sibling your
45 Tsono mkwiyo wa mʼbale wakoyo ukadzatsika ndi kuyiwala zonse wamuchitirazi, ndidzatuma munthu kuti adzakutenge. Nanga nditayirenji nonse awiri nthawi imodzi?”
till to return: turn back face: anger brother: male-sibling your from you and to forget [obj] which to make: do to/for him and to send: depart and to take: bring you from there to/for what? be bereaved also two your day one
46 Tsono Rebeka anati kwa Isake, “Ine sindikukondwera nawo anamwali a Chihiti. Ndipo ngati Yakobo angapeze mbeta kuno mwa anamwali a Chihitiwa, ndiye kuli bwino kungofa.”
and to say Rebekah to(wards) Isaac to loathe in/on/with life my from face: because daughter Heth if to take: marry Jacob woman: wife from daughter Heth like/as these from daughter [the] land: country/planet to/for what? to/for me life

< Genesis 27 >