< Genesis 25 >
1 Abrahamu anakwatira mkazi wina dzina lake Ketura.
And Abraham took another wife, and her name was Keturah.
2 Iyeyu anamubalira Zimurani, Yokisani, Medani, Midiyani, Isibaki ndi Suwa.
And she bore him Zimran, and Jokshan, and Medan, and Midian, and Ishbak, and Shuah.
3 Yokisani anabereka Seba ndi Dedani ndipo zidzukulu za Dedani ndiwo Aasuri, Aletusi, ndi Aleumi.
And Jokshan begot Sheba, and Dedan. And the sons of Dedan were Asshurim, and Letushim, and Leummim.
4 Ana aamuna a Midiyani anali, Efai, Eferi, Hanoki, Abida ndi Elida. Onsewa anali zidzukulu za Ketura.
And the sons of Midian: Ephah, and Epher, and Hanoch, and Abida, and Eldaah. All these were the children of Keturah.
5 Abrahamu anasiyira Isake chilichonse anali nacho.
And Abraham gave all that he had unto Isaac.
6 Koma pamene anali ndi moyo, Abrahamu anapereka mphatso kwa ana aakazi ake ena onse. Kenaka anawatumiza ku dziko la kummawa kuti akhale kutali ndi mwana wake Isake.
But unto the sons of the concubines, that Abraham had, Abraham gave gifts; and he sent them away from Isaac his son, while he yet lived, eastward, unto the east country.
7 Abrahamu anakhala ndi moyo zaka 175.
And these are the days of the years of Abraham's life which he lived, a hundred threescore and fifteen years.
8 Abrahamu anamwalira atakalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
And Abraham expired, and died in a good old age, an old man, and full of years; and was gathered to his people.
9 Ana ake, Isake ndi Ismaeli anamuyika mʼphanga la Makipela pafupi ndi Mamre, mʼmunda umene kale unali wa Efroni mwana wa Zohari Mhiti,
And Isaac and Ishmael his sons buried him in the cave of Machpelah, in the field of Ephron the son of Zohar the Hittite, which is before Mamre;
10 uwu ndi munda umene Abrahamu anagula kwa Ahiti. Kumeneko Abrahamu anakayikidwa pamodzi ndi mkazi wake Sara.
the field which Abraham purchased of the children of Heth; there was Abraham buried, and Sarah his wife.
11 Atamwalira Abrahamu, Mulungu anadalitsa mwana wake Isake, amene ankakhala pafupi ndi Beeri-lahai-roi (chitsime cha Wamoyo Wondipenya).
And it came to pass after the death of Abraham, that God blessed Isaac his son; and Isaac dwelt by Beer-lahai-roi.
12 Nazi zidzukulu za Ismaeli, mwana wa Abrahamu amene wantchito wa Sara, Hagara Mwigupto uja, anaberekera Abrahamu.
Now these are the generations of Ishmael, Abraham's son, whom Hagar the Egyptian, Sarah's handmaid, bore unto Abraham.
13 Awa ndi mayina a ana a Ismaeli monga mwa mndandanda wa mabadwidwe awo: Nebayoti ndiye anali mwana woyamba wa Ismaeli; kenaka Kedara, Adibeeli, Mibisamu,
And these are the names of the sons of Ishmael, by their names, according to their generations: the first-born of Ishmael, Nebaioth; and Kedar, and Adbeel, and Mibsam,
and Mishma, and Dumah, and Massa;
15 Hadadi, Tema, Yeturi, Nafisi ndi Kedema;
Hadad, and Tema, Jetur, Naphish, and Kedem;
16 Amenewa ndi ana a Ismaeli ndi mayina awo monga mwa midzi ndi misasa yawo. Anali olamulira mafuko khumi ndi awiri.
these are the sons of Ishmael, and these are their names, by their villages, and by their encampments; twelve princes according to their nations.
17 Ismaeli anakhala ndi moyo zaka 137. Iye anamwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
And these are the years of the life of Ishmael, a hundred and thirty and seven years; and he expired and died; and was gathered unto his people.
18 Zidzukulu za Ismaeli zinkakhala mʼdera la pakati pa Havila ndi Suri, kummwera kwa Igupto, mukamapita cha ku Asuri. Choncho anakhala kummawa kwa abale awo.
And they dwelt from Havilah unto Shur that is before Egypt, as thou goest toward Asshur: over against all his brethren he did settle.
19 Iyi ndi mbiri ya Isake mwana wa Abrahamu. Abrahamu anabereka Isake
And these are the generations of Isaac, Abraham's son: Abraham begot Isaac.
20 ndipo Isake anali ndi zaka makumi anayi pamene anakwatira Rebeka mwana wa Betueli Mwaramu wa ku Padanaramu mlongo wa Labani Mwaramu.
And Isaac was forty years old when he took Rebekah, the daughter of Bethuel the Aramean, of Paddan-aram, the sister of Laban the Aramean, to be his wife.
21 Isake anapempherera mkazi wake kwa Yehova popeza iye anali wosabereka. Yehova anayankha pemphero lake ndipo mkazi wake Rebeka anatenga pathupi.
And Isaac entreated the LORD for his wife, because she was barren; and the LORD let Himself be entreated of him, and Rebekah his wife conceived.
22 Koma pamene anawo amalimbana mʼmimba mwake, iye anati, “Bwanji zikundichitikira zoterezi?” Choncho anapita kukafunsa kwa Yehova.
And the children struggled together within her; and she said: 'If it be so, wherefore do I live?' And she went to inquire of the LORD.
23 Yehova anati kwa iye, “Udzabala mafuko awiri a anthu olimbana, ndipo magulu awiri a anthu ochokera mwa iwe adzasiyana; fuko limodzi lidzakhala la mphamvu kuposa linzake, ndipo wamkulu adzatumikira wamngʼono.”
And the LORD said unto her: Two nations are in thy womb, and two peoples shall be separated from thy bowels; and the one people shall be stronger than the other people; and the elder shall serve the younger.
24 Pamene nthawi inakwana yakuti abeleke, Rebeka anaberekadi mapasa.
And when her days to be delivered were fulfilled, behold, there were twins in her womb.
25 Woyamba kubadwa anali wofiira, ndipo thupi lake lonse linali ngati chovala cha ubweya; choncho anamutcha Esau.
And the first came forth ruddy, all over like a hairy mantle; and they called his name Esau.
26 Kenaka mʼbale wake anabadwa atagwira chidendene cha Esau; choncho anamutcha Yakobo. Isake anali ndi zaka 60 pamene Rebeka anabereka mapasawa.
And after that came forth his brother, and his hand had hold on Esau's heel; and his name was called Jacob. And Isaac was threescore years old when she bore them.
27 Anyamatawo anakula ndipo Esau anakhala katswiri wosaka, munthu wamʼthengo, pamene Yakobo anali munthu wofatsa, wokonda kukhala pa nyumba.
And the boys grew; and Esau was a cunning hunter, a man of the field; and Jacob was a quiet man, dwelling in tents.
28 Isake ankakonda Esau chifukwa cha nyama za kutchire zomwe ankakonda kudya, koma Rebeka ankakonda Yakobo.
Now Isaac loved Esau, because he did eat of his venison; and Rebekah loved Jacob.
29 Tsiku lina pamene Yakobo ankaphika chakudya, Esau anabwera kuchokera kuthengo ali wolefuka ndi njala.
And Jacob sod pottage; and Esau came in from the field, and he was faint.
30 Iye anati kwa Yakobo, “Tandipatsako phala lofiiralo, ndimwe! Ndalefuka ndi njala.” (Nʼchifukwa chake amatchedwanso Edomu).
And Esau said to Jacob: 'Let me swallow, I pray thee, some of this red, red pottage; for I am faint.' Therefore was his name called Edom.
31 Yakobo anayankha, “Choyamba undigulitse ukulu wako.”
And Jacob said: 'Sell me first thy birthright.'
32 Esau anati, “Chabwino, ine ndatsala pangʼono kufa, ukulu undithandiza chiyani?”
And Esau said: 'Behold, I am at the point to die; and what profit shall the birthright do to me?'
33 Koma Yakobo anati, “Lumbira kwa ine choyamba.” Kotero Esau analumbiradi, ndipo anagulitsa ukulu wake kwa Yakobo.
And Jacob said: 'Swear to me first'; and he swore unto him; and he sold his birthright unto Jacob.
34 Choncho Yakobo anamupatsa Esau buledi ndi phala lofiira lija. Iye anadya ndi kumwa, nanyamuka kumapita. Motero Esau anapeputsa ukulu wake wachisamba uja.
And Jacob gave Esau bread and pottage of lentils; and he did eat and drink, and rose up, and went his way. So Esau despised his birthright.